LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lff phunzilo 53
  • Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova
  • Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • KUMBANI MOZAMILAPO
  • CIDULE CAKE
  • FUFUZANI
  • Mmene Tingasankhile Zosangalatsa
    Mmene Tingakhalilebe mu Cikondi ca Mulungu
  • Mmene Mungasankhile Zosangulutsa Zabwino
    “Khalanibe m’Cikondi ca Mulungu”
  • Sankhani Zosangalatsa Mwanzelu
    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano—2019
  • Khalani Wodzipeleka kwa Yehova Yekha
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2019
Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
lff phunzilo 53
Phunzilo 53. Tate, mayi, pamodzi na mtsikana wawo akudya mapopukoni pamene akutamba TV.

PHUNZILO 53

Sankhani Zosangalatsa Zovomelezeka kwa Yehova

Yopulinta
Yopulinta
Yopulinta

Yehova ni “Mulungu wacimwemwe.” (1 Timoteyo 1:11) Iye amafuna kuti nafenso tizikhala na umoyo wacimwemwe komanso wosangalatsa. Ndipo amakondwela tikamapatula nthawi yakuti tipumuleko. Mu phunzilo lino, tiona mmene tingagwilitsile nchito nthawi yathu yosanguluka m’njila yabwino komanso yovomelezeka kwa Yehova.

1. Kodi tiyenela kukumbukila ciyani posankha zosangalatsa?

Kodi mumakonda kucita ciyani pamene mukupumula? Ena amakonda kungokhala panyumba—akuŵelenga buku, kumvela nyimbo, kutamba filimu, kapena kuyang’ana zinthu pa intaneti. Ena amakonda kucita zinthu pamodzi na anzawo monga—kupita kokayenda, kukanyaya, kapena kucita maseŵelo. Ciliconse cimene cingakhale makonda athu, tiyeni tionetsetse kuti tikusankha zosangalatsa ‘zovomelezeka kwa Ambuye.’ (Aefeso 5:10) M’pofunika kuimvetsetsa mfundo imeneyi, cifukwa m’zosangalatsa zambili masiku ano, mumakhalanso zinthu zimene Yehova amadana nazo monga ciwawa, zaciwelewele, kapena zamizimu. (Ŵelengani Salimo 11:5.) Kodi n’ciyani cingatithandize kupanga zisankho zanzelu pa nkhani ya zosangalatsa?

Tikasankha mabwenzi okonda Yehova, angatithandize kwambili posankha zosangalatsa. Monga tinaonela m’Phunzilo 48, “munthu woyenda ndi anthu anzelu adzakhala wanzelu.” Koma ngati timakonda kuceza na anthu amene sakonda malamulo a Mulungu, ‘tidzapeza mavuto.’—Miyambo 13:20.

2. N’cifukwa ciyani tiyenela kusamala nayo nthawi imene timathela pa zosangalatsa?

Ngakhale titasankha zosangalatsa zabwino, tiyenelabe kusamala kuti zisatidyele nthawi yoculuka kwambili. Tikapanda kusamala tidzasoŵa nthawi yocita zinthu zofunika kwambili. Baibo imatilimbikitsa ‘kugwilitsa nchito bwino nthawi yathu.’—Ŵelengani Aefeso 5:15, 16.

KUMBANI MOZAMILAPO

Dziŵani mmene mungapangile zisankho zabwino pa nkhani ya zosangalatsa.

3. Pewani zosangalatsa zoipa

N’cifukwa ciyani tiyenela kusamala posankha zosangalatsa? Tambani VIDIYO, kenako kambilanani mafunso otsatila.

VIDIYO: Kodi Niyenela Kusankha Zosangalatsa Zabwanji? (4:39)

  • Kodi maseŵelo a m’nthawi zamakedzana ofika mpaka kuphana, akufanana bwanji na zosangalatsa zina zamakono?

  • Mu vidiyo imeneyi, kodi Danny anaphunzilapo ciyani pa zosangalatsa?

Ŵelengani Aroma 12:9, na kukambilana funso ili:

  • Kodi lemba limeneli lingakuthandizeni bwanji posankha zosangalatsa?

Kodi ni zinthu ziti zimene Yehova amadana nazo? Ŵelengani Miyambo 6:16, 17, komanso Agalatiya 5:19-21. Pambuyo poŵelenga lililonse la malembawa, kambilanani funso ili:

  • Pa zimene zachulidwa pa lembali, ni zinthu ziti zofala m’zosangalatsa za masiku ano?

Mmene mungasankhile zosangalatsa mwanzelu

Dzifunseni kuti:

  • Ciphatikizapo ciyani? Kodi m’cosangalatsa cimeneci muli zinthu zimene Yehova amadana nazo?

  • Cimacitika nthawi yanji? Kodi cimabwela pa nthawi yoyenela kucita zinthu zofunika kwambili?

  • Muli anthu otani? Kodi anthu a m’cosangalatsa cimeneco ni osakonda Yehova, amene angakhale mayanjano oipa kwa ine?

Ni cinthu canzelu kutalikilana naco cinthu coopsa ciliconse. Conco, tiyenelanso kukhala kutali na cosangalatsa ciliconse cimene tikuona kuti sicingakhale cabwino kwa ife

Motoka ikuyendela m’mphepete mwenimweni mwa msewu wa kumbali kwa phili. Kumbuyo kwake yayamba kale kutsetselekela kuphompho.

4. Gwilitsani nchito nthawi yanu mwanzelu

Tambani VIDIYO, kenako kambilanani funso lotsatila.

VIDIYO: N’ciani Cimakulandani Nthawi? (2:45)

  • Ngakhale kuti m’bale wa mu vidiyo iyi sanali kutamba ciliconse coipa, kodi cinayamba kucitika kwa iye n’ciyani cifukwa cosasamala nayo nthawi yopumula?

Ŵelengani Afilipi 1:10, na kukambilana funso ili:

  • Kodi lembali lingatithandize bwanji kusamala nayo nthawi yocita zosangulutsa?

5. Sankhani zosangalatsa zoyenela

Ngakhale kuti zosangalatsa zina sizovomelezeka kwa Yehova, pali zinthu zambili zimene tingacite zosangalatsa. Ŵelengani Mlaliki 8:15, komanso Afilipi 4:8, na kukambilana funso ili:

  • Kodi mungachuleko zosangalatsa zabwino zimene mumakonda?

Zithunzi: Anthu a misinkhu yosiyana-siyana akusangalala na zosangulutsa zabwino. 1. Mtsikana akumvela nyimbo kwinaku akujambula zithunzi. 2. Anyamata atatu akuseŵela mpila wa manja. 3. Anyamata aŵili akuchova njinga. 4. Wacicepele akupanga motoka yoseŵeletsa. 5. Mwamuna akuimba ng’oma. 6. Mnyamata akucita seŵelo la pavidiyo na atate ake. 7. Mkazi akujambula cithunzi.

Zilipo zosangalatsa komanso zosangulutsa zabwino

ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI: “Palibe vuto kutamba zosangalatsa mmene muli zaciwawa, zaciwelewele, kapena zamizimu, malinga inu simucitako zinthu zimenezo.”

  • Nanga inu muganiza bwanji?

CIDULE CAKE

Yehova amafuna kuti tizisankha zosangalatsa zabwino zotikondweletsa.

Mafunso Obweleza

  • Kodi Mkhristu ayenela kupewa zosangalatsa zotani?

  • N’cifukwa ciyani tiyenela kusamala nayo nthawi yotayila pa zosangalatsa?

  • N’cifukwa ciyani muyenela kusankha zosangalatsa zovomelezeka kwa Yehova?

Colinga

FUFUZANI

Onani kuti ndani ali na udindo wotisankhila zosangalatsa.

“Kodi Muli ndi Lamulo Loletsa Mavidiyo Ena, Mabuku Ena Ndiponso Nyimbo Zina?” (Nkhani ya pawebusaiti)

Onani mmene mungapangile zisankho zabwino, pa nkhani ya zosangulutsa zimene mungacite panthawi yopumula.

“Kodi Zimene Mumachita pa Nthawi Yosangalala Zimakhala Zopindulitsa?” (Nsanja ya Olonda, October 15, 2011)

Mu nkhani yakuti “Ndinasiya Ngakhale Kudana ndi Azungu,” onani mmene munthu wina anasinthila zosangalatsa zake.

“Baibulo Limasintha Anthu” (Nsanja ya Olonda, February 1, 2010)

Onani mmene mayi akupangila cisankho canzelu pa zosangalatsa zophatikizapo zamizimu.

Pewani Zosangalatsa Zoonetsa Zamizimu (2:02)

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani