Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 18:12-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Munthu amene anatumidwa kukaitana Mikaya anauza Mikayayo kuti: “Aneneri onse alankhula zabwino kwa mfumu. Nawenso ukalankhule zabwino.”+ 13 Koma Mikaya anati: “Ndikulumbira mʼdzina la Yehova Mulungu wamoyo, zimene Mulungu angandiuze nʼzimene ndikanene.”+ 14 Kenako anafika kwa mfumu ndipo mfumuyo inamufunsa kuti: “Mikaya, kodi tipite kukamenyana ndi Ramoti-giliyadi kapena tisapite?” Nthawi yomweyo Mikaya anayankha kuti: “Pitani mukapambana ndipo mzindawo ukaperekedwa kwa inu mfumu.” 15 Ndiyeno mfumuyo inamufunsa kuti: “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti uzindiuza zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?” 16 Choncho Mikaya anati: “Ndikuona Aisiraeli onse atabalalika mʼmapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa.+ Ndipo Yehova anati: ‘Amenewa alibe mtsogoleri. Aliyense abwerere kunyumba kwake mwamtendere.’”

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani