Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mafumu 24:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Mfumuyo inatenga anthu onse a ku Yerusalemu, akalonga onse,+ asilikali onse amphamvu, amisiri onse ndiponso anthu osula zitsulo*+ nʼkupita nawo ku Babulo. Anthu onse amene inawatenga analipo 10,000. Palibe amene anatsala, kupatulapo anthu osauka kwambiri a mʼdzikolo.+ 15 Choncho iye anatenga Yehoyakini+ nʼkupita naye ku Babulo.+ Ku Yerusalemu anatenganso mayi a mfumuyo, akazi ake, nduna za panyumba yake komanso akuluakulu a mʼdzikolo, nʼkupita nawo ku Babulo.

  • 1 Mbiri 3:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Mwana wa Yehoyakimu+ anali Yekoniya. Yekoniya anabereka Zedekiya.

  • 2 Mbiri 36:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Yehoyakini+ anayamba kulamulira ali ndi zaka 18 ndipo analamulira miyezi itatu ndi masiku 10 ku Yerusalemu. Iye ankachita zoipa pamaso pa Yehova.+ 10 Chakumayambiriro kwa chaka, Mfumu Nebukadinezara inatuma asilikali ake omwe anakamutenga nʼkubwera naye ku Babulo+ limodzi ndi zinthu zabwino zamʼnyumba ya Yehova.+ Komanso Nebukadinezara anasankha Zedekiya, yemwe anali mʼbale wa bambo ake a Yehoyakini, kuti akhale mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.+

  • Yeremiya 22:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Kodi munthu uyu Koniya, wangokhala chiwiya chonyozeka komanso chophwanyika,

      Chiwiya chimene palibe amene akuchifuna?

      Nʼchifukwa chiyani iyeyu ndi ana ake agwetsedwa pansi

      Nʼkuponyedwa mʼdziko limene sakulidziwa?’+

  • Yeremiya 24:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu amene anali patsogolo pa kachisi wa Yehova. Anandionetsa madenguwo pambuyo poti Nebukadinezara* mfumu ya Babulo watenga Yekoniya*+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, pamodzi ndi akalonga a Yuda, amisiri komanso anthu osula zitsulo,* kuchoka ku Yerusalemu nʼkupita nawo ku ukapolo ku Babulo.+

  • Yeremiya 37:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Ndiyeno Mfumu Zedekiya+ mwana wa Yosiya inayamba kulamulira mʼmalo mwa Koniya+ mwana wa Yehoyakimu chifukwa Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo inamuika kuti akhale mfumu mʼdziko la Yuda.+

  • Yeremiya 52:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Kenako mʼchaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini+ mfumu ya Yuda, Evili-merodaki anakhala mfumu ya Babulo. Ndiyeno mʼchaka chomwecho mʼmwezi wa 12, pa tsiku la 25 la mweziwo, iye anamasula* Yehoyakini mfumu ya Yuda nʼkumutulutsa mʼndende.+

  • Mateyu 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani