Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yobu 30:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Chifukwa ndikudziwa kuti mudzandipereka ku imfa,

      Kunyumba imene aliyense wamoyo adzapitako.

  • Salimo 49:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Aliyense amaona kuti ngakhale anthu anzeru amafa,

      Munthu wopusa komanso munthu wopanda nzeru, onse amawonongeka,+

      Ndipo chuma chawo amasiyira anthu ena.+

  • Salimo 49:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Koma munthu, ngakhale kuti ndi wolemekezeka, sadzapitiriza kukhala ndi moyo mpaka kalekale.+

      Iye amangofanana ndi nyama zimene zimafa.+

  • Mlaliki 8:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Palibe munthu amene ali ndi mphamvu pa mzimu* kapena amene angaletse mzimuwo kuti usachoke. Mofanana ndi zimenezi palibenso amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa.+ Palibe amene amaloledwa kuchoka kunkhondo ndipo mofanana ndi zimenezi, anthu amene amachita zoipa, kuipako sikudzawalola kuti athawe.*

  • Mlaliki 9:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Anthu onse mapeto awo ndi ofanana,+ munthu wolungama komanso munthu woipa,+ munthu wabwino ndi woyera komanso munthu wodetsedwa, munthu amene amapereka nsembe komanso amene sapereka nsembe. Munthu wabwino nʼchimodzimodzi ndi munthu wochimwa. Munthu amene amachita lumbiro nʼchimodzimodzi ndi amene amaganiza kaye asanachite lumbiro.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani