3 Ndikanadziwa kumene ndingapeze Mulungu,+
Ndikanapita kumalo kumene iye amakhala.+
4 Bwenzi nditapititsa mlandu wanga kwa iye
Ndipo ndikanafotokoza mfundo zodziikira kumbuyo.
5 Ndikanamvetsera zimene akanandiyankha,
Ndipo ndikanasunga zimene wandiuza.