22 Kodi munthu amapeza chiyani pa ntchito yonse imene wagwira mwakhama, chifukwa cha zimene amalakalaka mumtima mwake padziko lapansi pano?+ 23 Chifukwa masiku onse a moyo wake, ntchito yakeyo imamubweretsera zowawa ndi zokhumudwitsa.+ Ndipo ngakhale usiku mtima wake supuma.+ Izinso nʼzachabechabe.