Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 2 Mbiri 28:19, 20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Yehova anatsitsa Ayuda chifukwa cha Ahazi mfumu ya Isiraeli, popeza analekerera Ayuda kuchita makhalidwe oipa zomwe zinachititsa kuti achite zinthu zambiri zosakhulupirika kwa Yehova.

      20 Patapita nthawi, Tigilati-pilenesere+ mfumu ya Asuri anabwera kwa iye ndipo anangomuwonjezera mavuto+ mʼmalo momulimbikitsa.

  • Yesaya 7:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Yehova adzabweretsera iweyo, anthu ako komanso nyumba ya bambo ako nthawi yovuta imene sinakhaleponso kuyambira tsiku limene Efuraimu anapatukana ndi Yuda.+ Iye adzakubweretserani mfumu ya Asuri.+

  • Yesaya 7:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Pa tsiku limenelo Yehova adzakumetani tsitsi la kumutu ndi tsitsi la mʼmiyendo pogwiritsira ntchito lezala lobwereka la kuchigawo cha ku Mtsinje,* pogwiritsira ntchito mfumu ya Asuri,+ ndipo lezalalo lidzametanso ndevu zanu.

  • Yesaya 10:28-32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Iye wafika ku Ayati.+

      Wadutsa ku Migironi.

      Ndipo katundu wake wamuika ku Mikimasi.+

      29 Iwo adutsa powolokera mtsinje.

      Usiku agona ku Geba.+

      Rama wanjenjemera ndipo Gibeya,+ kwawo kwa Sauli, wathawa.+

      30 Iwe mwana wamkazi wa Galimu, lira ndi kufuula kwambiri.

      Khala tcheru iwe Laisa,

      Iwenso Anatoti womvetsa chisoni!+

      31 Madimena wathawa.

      Anthu okhala ku Gebimu abisala.

      32 Tsiku lomwelo iye akaima ku Nobu.+

      Iye akuopseza ndi chibakera phiri la mwana wamkazi wa Ziyoni,*

      Phiri limene pali Yerusalemu.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani