Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yeremiya 21:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 ‘Yehova wanena kuti: “Kenako Zedekiya mfumu ya Yuda, atumiki ake ndi anthu amumzindawu, onse amene adzapulumuke ku mliri, lupanga ndi njala yaikulu, ndidzawapereka mʼmanja mwa Mfumu Nebukadinezara* ya ku Babulo. Ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo komanso mʼmanja mwa amene akufuna kuchotsa moyo wawo.+ Nebukadinezara adzawapha ndi lupanga ndipo sadzawamvera chisoni, kuwakomera mtima kapena kuwachitira chifundo.”’+

  • Yeremiya 24:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Koma mofanana ndi nkhuyu zoipa zija, zimene ndi zoipa kwambiri moti munthu sangathe kudya,+ Yehova wanena kuti: “Ndi mmenenso ndidzaonere Zedekiya+ mfumu ya Yuda, akalonga ake, anthu onse opulumuka mu Yerusalemu amene atsalira mʼdzikoli komanso anthu okhala mʼdziko la Iguputo.+

  • Yeremiya 34:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Ndipo Mfumu Zedekiya ya Yuda ndi akalonga ake ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo, mʼmanja mwa anthu amene akufuna moyo wawo ndiponso mʼmanja mwa asilikali a mfumu ya ku Babulo+ amene akubwerera osamenyana nanu.’+

  • Ezekieli 12:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Mtsogoleri amene ali pakati pawo adzanyamula katundu wake paphewa nʼkuchoka kuli mdima. Adzabowola khoma nʼkutulutsirapo katundu wake.+ Iye adzaphimba nkhope kuti asaone pansi. 13 Ine ndidzamuponyera ukonde wanga ndipo iye adzakodwa mu ukonde wanga wosakira.+ Kenako ndidzamupititsa ku Babulo, kudziko la Akasidi. Koma iye sadzaliona dzikolo ndipo adzafera komweko.+

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani