-
Yeremiya 10:12-16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 Iye ndi Mulungu amene anapanga dziko lapansi pogwiritsa ntchito mphamvu zake,
Amene anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru zake.+
Amenenso anatambasula kumwamba chifukwa cha kuzindikira kwake.+
13 Mawu ake akamveka,
Madzi akumwamba amachita mkokomo,+
Ndipo amachititsa mitambo* kukwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+
Iye amachititsa kuti kukamagwa mvula mphezi zizingʼanima,
Ndipo amatulutsa mphepo mʼnyumba zake zosungira.+
14 Munthu aliyense akuchita zinthu mopanda nzeru komanso mosazindikira.
Mmisiri wa zitsulo aliyense adzachita manyazi chifukwa cha chifaniziro chake chosula.+
Chifukwa chifaniziro chake chopangidwa ndi chitsulo chosungunula ndi mulungu wonama
15 Iwo ndi achabechabe, oyenera kunyozedwa.+
Tsiku loti aweruzidwe likadzafika adzawonongedwa.
16 Koma Mulungu, amene ndi cholowa cha Yakobo, sali ngati mafano amenewa,
Chifukwa iye ndi amene anapanga china chilichonse,
Ndipo Isiraeli ndi ndodo ya cholowa chake.+
Dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+
-