Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • Yeremiya 5:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Aneneri akulosera zabodza,+

      Ndipo ansembe akugwiritsa ntchito mphamvu zawo kuti azilamulira ena.

      Anthu anga nawonso akukonda zimenezi.+

      Koma kodi mudzachita chiyani mapeto akadzafika?”

  • Yeremiya 6:12-15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Nyumba zawo limodzi ndi minda yawo komanso akazi awo,

      Zidzaperekedwa kwa anthu ena.+

      Chifukwa ndidzatambasula dzanja langa nʼkuwononga anthu okhala mʼdzikolo,” akutero Yehova.

      13 “Chifukwa aliyense kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, akupeza phindu mwachinyengo.+

      Kuyambira mneneri mpaka wansembe, aliyense akuchita zachinyengo.+

      14 Iwo akuyesa kuchiritsa mwachinyengo kuwonongeka kwa anthu anga* ponena kuti,

      ‘Kuli mtendere! Kuli mtendere!’

      Pamene kulibe mtendere.+

      15 Kodi iwo amachita manyazi ndi zinthu zonyansa zimene achita?

      Iwo sachita manyazi ngakhale pangʼono,

      Ndipo sadziwa nʼkomwe kuchita manyazi.+

      Choncho iwo adzagwa pamodzi ndi anthu amene akugwa.

      Ndikamadzawapatsa chilango, iwo adzapunthwa,” akutero Yehova.

  • Yeremiya 27:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 ‘Choncho musamvere aneneri, anthu ochita zamaula, olota maloto, ochita zamatsenga ndi obwebweta amene ali pakati panu ndipo akukuuzani kuti: “Simudzatumikira mfumu ya Babulo.”

  • Maliro 2:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Masomphenya amene aneneri anu anaona ndi abodza komanso achabechabe,+

      Ndipo sanaulule zolakwa zanu nʼcholinga choti musatengedwe kupita ku ukapolo,+

      Koma ankaona masomphenya abodza komanso okusocheretsani.+

  • Ezekieli 22:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Koma aneneri amʼdzikomo apaka laimu zochita za akalongawo. Iwo amaona masomphenya onama ndipo amalosera zinthu zabodza.+ Aneneriwo amanena kuti: “Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti,” pamene Yehova sananene chilichonse.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani