Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • Misonkhano
  • 1 Samueli 21:1-6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Kenako Davide anafika ku Nobu+ kwa Ahimeleki wansembe. Ahimeleki ataona Davide anayamba kunjenjemera, ndipo anamufunsa kuti: “Nʼchifukwa chiyani uli wekhawekha?”+ 2 Davide anayankha Ahimeleki wansembe kuti: “Mfumu yandituma kuti ndikachite zinazake ndipo yandiuza kuti, ‘Usauze aliyense zimene ndakutumazi komanso malangizo amene ndakupatsa.’ Ndapangana ndi anyamata anga kuti ndikumane nawo penapake. 3 Ndiye ngati muli ndi mikate 5 kapena chakudya chilichonse mundipatseko.” 4 Koma wansembeyo anayankha Davide kuti: “Palibe mkate wamba, koma pali mkate wopatulika.+ Nditha kukupatsa umenewu ngati anyamatawo ayesetsa kudzisunga osagona ndi akazi.”+ 5 Davide anayankha wansembeyo kuti: “Akazi sanatiyandikire ngati mmene zinalilinso poyamba pamene ndinapita kukamenya nkhondo.+ Anyamatawo amakhala oyera ngakhale pamene tili pa ntchito wamba, ndiye kuli bwanji lero?” 6 Choncho wansembeyo anamupatsa mkate wopatulika,+ chifukwa panalibe mkate wina koma mkate wachionetsero umene anauchotsa pamaso pa Yehova tsiku limenelo kuti aikepo watsopano.

Mabuku a Chinenero Chamanja cha ku Malawi (1993-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chinenero Chamanja cha ku Malawi
  • tumizirani
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • zachinsinsi
  • JW.ORG
  • Lowani
tumizirani