Yobu
18 Bilidadi+ wa ku Shuwa anayankha kuti:
2 “Kodi usiya nthawi yanji kulankhula choncho?
Sonyeza kuti ndiwe wozindikira kuti nafenso tilankhule.
4 Ngakhale utadzikhadzulakhadzula chifukwa choti wakwiya,
Kodi dziko lapansi lingasiyidwe chifukwa cha iwe?
Kapena kodi thanthwe lingasunthe pamalo ake?
5 Inde, kuwala kwa woipa kudzazimitsidwa,
Ndipo malawi a moto wake sadzawala.+
6 Kuwala kwa mutenti yake kudzazima,
Ndipo nyale imene ili mutenti yake idzazimitsidwa.
7 Adzakhala alibe mphamvu zoti nʼkuyendera,
Ndipo mapulani ake adzamubweretsera mavuto.+
8 Mapazi ake adzamugwetsera mu ukonde,
Ndipo adzayenda mʼzingwe za ukondewo.
9 Msampha udzamugwira chidendene.
Khwekhwe lidzamukola.+
10 Chingwe chabisidwa pansi kuti chimukole,
Ndipo msampha uli panjira yake.
11 Zoopsa zimamuchititsa mantha paliponse,+
Ndipo zimamuthamangitsa zili naye pafupi kwambiri.
13 Khungu lake ladyeka.
Matenda oopsa kwambiri agwira* manja ndi miyendo yake.
14 Iye adzachotsedwa mʼmalo otetezeka amutenti yake,+
Ndipo adzamupititsa kwa mfumu ya zinthu zoopsa.*
16 Pansi, mizu yake idzauma,
Ndipo pamwamba, nthambi zake zidzafota.
17 Anthu sadzamukumbukiranso padziko lapansi,
Ndipo mumsewu dzina lake silidzadziwika.*
18 Adzamuchotsa powala nʼkumupititsa kumdima
Ndipo adzamuthamangitsa padziko lapansi.
19 Iye sadzasiya ana kapena mbadwa pakati pa anthu ake,
Ndipo sipadzakhala wopulumuka pamalo amene iye akukhala.*
20 Tsiku la tsoka lake likadzafika, anthu a Kumadzulo adzachita mantha kwambiri,
Ndipo anthu a Kumʼmawa adzagwidwa ndi mantha aakulu.
21 Izi nʼzimene zimachitikira matenti a munthu wochita zoipa,
Komanso malo a munthu amene sadziwa Mulungu.”