Mawu a M'munsi
“Mwezi wachiwiri” umene ukutchulidwa mʼvesili unadzakhala mwezi wa 8 pakalendala yopatulika imene Yehova anapatsa Aisiraeli atatuluka mʼdziko la Iguputo. Mwezi umenewu, wotchedwa Buli, unkayambira chapakati pa October nʼkutha chapakati pa November. Onani Zakumapeto B15.