LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 13
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Cikondi ndi njila yopambana (1-13)

1 Akorinto 13:1

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    12/15/2015, tsa. 3

1 Akorinto 13:4

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, tsa. 15

1 Akorinto 13:5

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “cakukhosi.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 21-26

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, masa. 15-16

1 Akorinto 13:6

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, tsa. 16

1 Akorinto 13:7

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, tsa. 16

1 Akorinto 13:8

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “kulankhula zinenelo zina mozizwitsa.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    6/1/2014, tsa. 16

1 Akorinto 13:12

Mawu amunsi

  • *

    Galasi yake inali ya citsulo.

1 Akorinto 13:13

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    10/2016, tsa. 30

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 13:1-13

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

13 Ngati ndimalankhula malilime a anthu komanso a angelo koma ndilibe cikondi, ndiye kuti ndakhala belu yolila kapena cimbale ca citsulo coliza. 2 Ndipo ngati ndili ndi mphatso ya kulosela komanso ndikumvetsa zinsinsi zonse zopatulika ndiponso kudziwa zinthu zonse, ndipo ngati ndili ndi cikhulupililo conse moti ndikutha kusuntha naco mapili, koma ndilibe cikondi, zimene ndimacitazo zilibe nchito. 3 Ngati ndapeleka zinthu zanga zonse kuti ndidyetse ena, komanso ngati ndapeleka thupi langa pofuna kudzitama, koma ndilibe cikondi, sindingapindule m’pang’ono pomwe.

4 Cikondi n’coleza mtima komanso n’cokoma mtima. Cikondi sicicita nsanje, sicidzitama, sicidzitukumula. 5 Cikondi sicicita zosayenela, sicicita zofuna zake zokha, sicikwiya, komanso sicisunga zifukwa.* 6 Sicisangalala ndi zosalungama, koma cimasangalala ndi coonadi. 7 Cimakwilila zinthu zonse, cimakhulupilila zinthu zonse, cimayembekezela zinthu zonse, cimapilila zinthu zonse.

8 Cikondi sicitha. Koma ngati pali mphatso za kulosela zidzatha, kaya kulankhula malilime* kudzatha, ndipo kaya pali mphatso ya kudziwa zinthu, nayonso idzatha. 9 Pakuti sitidziwa zonse ndipo timalosela mopelewela. 10 Koma tikadzadziwa zonse zopelewelazi zidzatha. 11 Ndili mwana, ndinali kulankhula ngati mwana, kuganiza ngati mwana, ndiponso kuona zinthu ngati mwana. Koma popeza tsopano ndakula, ndinaleka kucita zacibwana. 12 Koma palipano sitikutha kuona bwino-bwino cifukwa tikugwilitsa nchito galasi* losaonetsa bwino-bwino. Koma m’tsogolo tidzaona bwino-bwino. Palipano cidziwitso canga n’copelewela, koma cidzakhala colondola ngati mmene Mulungu amandidziwila bwino. 13 Tsopano, patsala zinthu zitatu izi: Cikhulupililo, ciyembekezo, komanso cikondi. Koma cacikulu koposa pa zonsezi ndi cikondi.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani