LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Lelo

Citatu, September 24

Mulimonse mmene tapitila patsogolo, tiyeni tipitilize kupita patsogolo pocita zomwe tikucitazo.​—Afil. 3:16.

Nthawi na nthawi, mumamva zocitika za abale na alongo amene adzipeleka kuti awonjezele utumiki wawo wopatulika. Mwina analoŵa Sukulu ya Alengezi a Ufumu, kapena anasamukila ku malo osoŵa. Ngati mungathe kudziikila zolinga ngati zimenezi, teloni. Anthu a Yehova ni ofunitsitsa kuwonjezela utumiki wawo. (Mac. 16:9) Nanga bwanji ngati pali pano simungakwanitse kucita zimenezi? Musamadzione kuti ndinu wolephela podziyelekezela na amene angakwanitse. Cofunika kwambili kwa Akhristu ni kupitilizabe kutumikila mokhulupilika. (Mat. 10:22) Musaiŵale kuti Yehova amakondwela ngako ngati mum’patsa zonse zimene mungathe malinga na mmene zinthu zilili pa umoyo wanu. Iyi ndiyo njila yabwino kwambili imene mungapitilizile kutsatila Yesu pambuyo pa ubatizo wanu.​—Sal. 26:1. w24.03 10 ¶11

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Cinayi, September 25

Mokoma mtima anatikhululukila macimo athu onse.​—Akol. 2:13.

Atate wathu wa kumwamba analonjeza kutikhululukila macimo athu tikalapa. (Sal. 86:5) Conco ngati talapa macimo athu, tizikhulupilila mawu ake, na kukhala otsimikiza kuti watikhululukila. Kumbukilani kuti Yehova si wokhwimitsa zinthu. Satiyembekezela kucita zoculuka kuposa zimene tingakwanitse. Amayamikila zilizonse zimene timam’patsa, malinga n’zimene tingakwanitse. Komanso, muziganizila zitsanzo za anthu ochulidwa m’Baibo amene anatumikila Yehova na mtima wawo wonse. Ganizilani za Mtumwi Paulo. Iye anatumikila mokangalika kwa zaka, anayenda mitunda itali-itali, ndipo anakhazikitsa mipingo. Koma zinthu zinasintha pa umoyo wake, ndipo sanathenso kulalikila monga kale. Kodi Mulungu analeka kukondwela naye? Ayi. Iye anapitiliza kucita zonse zimene akanatha, ndipo Yehova anamudalitsa. (Mac. 28:30, 31) Mofananamo, zimene timapatsa Yehova sizingafanane nthawi zonse. Nthawi zina zingaculuke, nthawi zina zingacepe. Koma cofunika kwambili kwa iye, ni cimene timacitila zimenezo. w24.03 27 ¶7, 9

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025

Cisanu, September 26

Mʼmawa kwambili kudakali mdima, [Yesu] anapita kumalo kopanda anthu. Kumeneko anayamba kupemphela.​—Maliko 1:35.

Mwa mapemphelo ake kwa Yehova, Yesu anapeleka citsanzo kwa ophunzila ake. Pa utumiki wake wonse, iye anali kupemphela kaŵili-kaŵili. Kambili, anali kukhala pakati pa anthu, ndipo anali kukhala wotangwanika. Conco anali kucita kupatula nthawi yoti apemphele. (Maliko 6:31, 45, 46) Iye anali kuuka m’mamaŵa kuti akhale na nthawi yopemphela payekha. Panthawi ina, anapemphela usiku wonse kuti apange cisankho cofunika kwambili. (Luka 6:12, 13) Panthawi inanso, Yesu anaika maganizo ake pa kukwanilitsa mbali yovuta ya utumiki wake wa padziko lapansi. Conco anapemphela mobweleza-bweleza usiku woti maŵa lake aphedwa. (Mat. 26:39, 42, 44) Citsanzo ca Yesu citiphunzitsa kuti ngakhale titangwanike bwanji, tiyenela kupatula nthawi yopemphela. Monga Yesu, tingafunike kucita kuipatula nthawi yopemphela. Mwina tingafunike kuuka m’mawa kwambili, kapena kugona mocedwako usiku kuti tipemphele. Tikatelo, timaonetsa Yehova kuti timayamikila mphatso yapadela imeneyi. w23.05 3 ¶4-5

Kusanthula Malemba Tsiku na Tsiku—2025
Takulandilani
Ici ni cida cofufuzila m'mabuku olembewa na Mboni za Yehova mu vitundu volekana-lekana.
Ngati mufuna kucita daunilodi, yendani pa jw.org.
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani