Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
19 Kenako Pilato anatenga Yesu n’kumukwapula. 2 Ndipo asilikali analuka cisoti cacifumu caminga n’kumuveka kumutu. Anamuvekanso mkanjo wa mtundu wapepo. 3 Iwo anali kupita kwa iye n’kumakamba kuti: “Moni,* inu Mfumu ya Ayuda!” Analinso kumuwaza mambama kumaso. 4 Pilato anapitanso panja n’kuwauza kuti: “Onani! Ine ndamubweletsa panja kwa inu kuti mudziwe kuti sindinamupeze ndi mlandu uliwonse.” 5 Conco Yesu anatuluka panja atavala cisoti cacifumu caminga cija, ndi mkanjo wa mtundu wapepo. Kenako Pilato anawauza kuti: “Onani! Munthu uja ndi uyu!” 6 Koma pamene ansembe aakulu ndi alonda anamuona, anafuula kuti: “Apacikidwe! Apacikidwe ndithu!”* Pilato anawauza kuti: “Mutengeni inuyo mukamuphe nokha,* cifukwa ine sindikumupeza ndi mlandu uliwonse.” 7 Ayudawo anamuyankha kuti: “Ife tili ndi malamulo. Malinga ndi malamulowo, iye ayenela kufa cifukwa anali kunena kuti ndi mwana wa Mulungu.”
8 Pilato atamva zimene iwo anali kukamba, anacita mantha kwambili, 9 ndipo iye analowanso m’nyumba ya bwanamkubwa ndi kufunsa Yesu kuti: “Kodi unacokela kuti?” Koma Yesu sanamuyankhe ciliconse. 10 Conco Pilato anamufunsa kuti: “Kodi sufuna kukamba ndi ine? Kodi sudziwa kuti ndili ndi mphamvu zokumasula komanso mphamvu zokupha?”* 11 Yesu anamuyankha kuti: “Simukanakhala ndi mphamvu pa ine ngakhale pang’ono ngati simunapatsidwe mphamvuzo kucokela kumwamba. Ndiye cifukwa cake munthu amene anandipeleka kwa inu ali ndi chimo lalikulu zedi.”
12 Pa cifukwa cimeneci, Pilato anayamba kuyesayesa kupeza njila yakuti amumasule, koma Ayudawo anafuula kuti: “Mukam’masula munthu uyu, ndiye kuti sindinu bwenzi la Kaisara. Aliyense wodzipanga kukhala mfumu amatsutsana ndi Kaisara.” 13 Ndiyeno Pilato atamva mawu amenewa, anatulutsa Yesu panja, ndipo anakhala pampando woweluzila milandu pa malo ochedwa Bwalo la Miyala, koma mu Ciheberi amachedwa, Gab′ba·tha. 14 Tsopano linali tsiku la Cikonzekelo ca Pasika, ndipo nthawi inali ca m’ma 12 koloko masana.* Pilato anauza Ayudawo kuti: “Onani! Mfumu yanu iyi!” 15 Koma iwo anafuula kuti: “Anyongedwe! Anyongedwe! Apacikidwe ndithu ameneyo!”* Ndiyeno Pilato anawafunsa kuti: “Kodi mufuna ndiphe mfumu yanu?” Ansembe aakulu anayankha kuti: “Ife tilibe mfumu ina koma Kaisara.” 16 Kenako anamupeleka kwa iwo kuti akaphedwe pamtengo.
Conco Yesu anakhala m’manja mwawo. 17 Atadzinyamulila yekha mtengo wozunzikilapo,* anatuluka n’kupita kumalo ochedwa Cibade, amene m’Ciheberi anali kuchedwa Gologota. 18 Kumeneko anamukhomelela pamtengo pamodzi ndi amuna ena awili, wina kumbali iyi, wina kumbali inayi. Ndipo Yesu anali pakati. 19 Nayenso Pilato analemba dzina laudindo n’kuliika pamtengo wozunzikilapowo.* Analembapo kuti: “Uyu ndi Yesu Mnazareti, Mfumu ya Ayuda.” 20 Ayuda ambili anawelenga mawuwo, cifukwa kumene Yesu anamukhomelela pamtengo kunali kufupi ndi mzinda, ndipo mawuwo analembedwa m’Ciheberi, m’Cilatini, ndi m’Cigiriki. 21 Koma ansembe aakulu a Ayuda anauza Pilato kuti: “Musalembe kuti, ‘Mfumu ya Ayuda,’ koma kuti iye anati, ‘Ndine Mfumu ya Ayuda.’” 22 Pilato anawayankha kuti: “Zimene ndalemba, ndalemba.”
23 Asilikaliwo atamukhomelela Yesu pa mtengo, anatenga zovala zake zakunja n’kuzigawa panayi, ndipo msilikali aliyense anatengako mbali imodzi. Iwo anatenganso covala camkati. Koma covala camkatico cinalibe msoko. Cinali nsalu imodzi kucokela pamwamba mpaka pansi. 24 Conco asilikaliwo anauzana kuti: “Tisacing’ambe covalaci, m’malo mwake tiyeni ticite maele kuti tidziwe amene angacitenge.” Izi zinacitika kuti lemba likwanilitsidwe limene limati: “Iwo adzagawana zovala zanga, ndipo adzacita maele pa covala canga.” Ndipo asilikaliwo anacitadi zimenezi.
25 Koma pafupi ndi mtengo wozunzikilapo wa Yesu, panaimilila amayi ake ndi m’bale wawo, Mariya mkazi wa Kulopa, komanso Mariya Mmagadala. 26 Yesu ataona amayi ake komanso wophunzila uja amene anali kumukonda ataimilila pafupi, anauza amayi akewo kuti: “Mayi, kuyambila lelo, uyu ndi mwana wanu.” 27 Anauzanso wophunzila uja kuti: “Kuyambila lelo, awa ndi mayi ako.” Ndipo kuyambila nthawiyo wophunzilayo anatenga mayiwo n’kupita nawo kunyumba kwake.
28 Pambuyo pa izi, Yesu atadziwa kuti zonse zacitika, kuti malemba akwanilitsidwe, ananena kuti: “Ndamva ludzu.” 29 Pamalopo panali mtsuko wodzala ndi vinyo wowawasa. Conco iwo anaviika siponji mu vinyo wowawasayo, ndipo anaisomeka ku kamtengo ka hisope, kenako anakanyamula kamtengoko n’kukafikitsa pakamwa pa Yesu. 30 Yesu atalandila vinyo wowawasayo, anati: “Zakwanilitsidwa!” Ndipo atawelamitsa mutu, anapeleka mzimu wake.*
31 Limeneli linali tsiku la Cikonzekelo. Conco Ayuda sanafune kuti mitemboyo ikhalebe pamitengo yozunzikilapo pa tsiku la Sabata (cifukwa Sabatalo linali lalikulu). Cotelo Ayudawo anapempha Pilato kuti awalole kukawathyola miyendo ndi kucotsa mitembo yawo. 32 Ndiyeno asilikali anabwela n’kuthyola miyendo ya munthu woyamba, komanso ya munthu winayo amene anapacikidwa pambali pake. 33 Koma atafika pa Yesu anapeza kuti wafa kale, conco iwo sanathyole miyendo yake. 34 Koma mmodzi wa asilikaliwo analasa Yesu m’nthiti ndi mkondo, ndipo nthawi yomweyo magazi ndi madzi anatuluka. 35 Munthu amene anaona zimenezo anacitila umboni, ndipo umboni wake ndi woona. Iye akudziwa kuti zimene amakamba ndi zoona, kuti inu mukhulupilile. 36 Ndipo izi zinacitika kuti lemba likwanilitsidwe limene limati: “Sadzathyoledwa fupa ngakhale limodzi.”* 37 Komanso lemba lina limati: “Iwo adzayang’ana kwa munthu amene anamulasa.”
38 Pambuyo pa zinthu zimenezi, Yosefe wa ku Arimateya, amene anali wophunzila wa Yesu wamseli cifukwa coopa Ayuda, anapempha Pilato kuti akacotse mtembo wa Yesu, ndipo Pilatoyo anamulola. Conco iye anabwela n’kutenga mtembowo. 39 Nikodemo, munthu amene anapita kwa Yesu usiku nthawi yoyamba, nayenso anabwela atanyamula mule wosakaniza ndi aloye, wolemela makilogalamu pafupifupi 32.7. 40 Conco iwo anatenga mtembo wa Yesu n’kuukulunga mu nsalu zamalilo zonunkhila, malinga ndi mwambo wa Ayuda woika malilo. 41 Kumene anamuphela* kunali munda, ndipo m’mundamo munali manda* atsopano omwe munali musanaikidwepo munthu cikhalile. 42 Popeza linali tsiku la Cikonzekelo ca Ayuda, komanso poti mandawo anali pafupi, iwo anaika Yesu mmenemo.