LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Atesalonika 2
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Atesalonika

      • Utumiki wa Paulo ku Tesalonika (1-12)

      • Atesalonika analandila mau a Mulungu (13-16)

      • Paulo anali kulakalaka kuona Atesalonika (17-20)

1 Atesalonika 2:2

Mawu amunsi

  • *

    Ma Baibo ena amati, “imene tinali kubvutika kwambili.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 59

1 Atesalonika 2:8

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “tinali osangalala.”

1 Atesalonika 2:13

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 5

1 Atesalonika 2:17

Mawu amunsi

  • *

    Kucokela ku Cigiriki, “kuti tione nkhope zanu.”

1 Atesalonika 2:19

Mawu amunsi

  • *

    Kucokela ku Cigiriki, “Kodi cisoti caulemelelo cimene tidzacinyadile.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Atesalonika 2:1-20

Kalata Yoyamba kwa Atesalonika

2 Abale, inu mukudziwa bwino kuti ulendo wathu wobwela kwa inu unali waphindu. 2 Monga mukudziwila, ngakhale kuti poyamba tinabvutika komanso anthu anaticita zacipongwe ku Filipi, Mulungu wathu anatithandiza kuti tilimbe mtima kuti tikuuzeni uthenga wabwino wa Mulungu panthawi imene anthu anali kutitsutsa kwambili.* 3 Zimene tikukulimbikitsani kuti mucite sizikucokela m’maganizo olakwika kapena odetsedwa, ndipo sitikuzikamba mwacinyengo. 4 Koma tikutelo cifukwa Mulungu wabvomeleza kutipatsa nchito yolalikila uthenga wabwino. Conco tikulankhula kuti tikondweletse Mulungu amene amasanthula mitima yathu, osati kuti tikondweletse anthu.

5 Inu mukudziwa kuti sitinalankhulepo mau oshashalika, kapena kucita zaciphamaso ndi zolinga zadyela. Ndipo pa nkhani imeneyi, Mulungu ndiye mboni yathu. 6 Komanso sitinali kungodzifunila ulemelelo wocokela kwa anthu ai, kaya kwa inu kapena kwa anthu ena. Sitinacite zimenezo ngakhale kuti monga atumwi a Khristu tikanakhala mtolo woonongetsa ndalama zambili. 7 M’malomwake, tinakhala odekha ngati mmene mai woyamwitsa amacitila posamalila ana ake. 8 Cifukwa timakukondani kwambili, tinacita khama* kukupatsani uthenga wabwino wa Mulungu, ngakhale kupeleka miyoyo yathu yeniyeniyo kuti tikuthandizeni, pakuti tinakukondani kwabasi.

9 Mukudziwa bwino abale, kuti pamene tinali pakati panu, tinayesetsa kugwila nchito mwakhama ndi mphamvu zathu zonse. Tinali kugwila nchito usana ndi usiku kuti tisasenzetse mtolo aliyense wa inu wotilipilila kalikonse pofuna kutithandiza, pamene tinali kulalikila uthenga wabwino wa Mulungu kwa inu. 10 Pamene tinali ndi inu okhulupilila, tinacita zinthu mokhulupilika, mwacilungamo, ndipo tinalibe cifukwa cotinenezela. Inu komanso Mulungu ndinu mboni zathu pa nkhaniyi. 11 Mukudziwanso bwino kuti aliyense wa inu tinali kumulimbikitsa, kumutonthoza, komanso kumulangiza ngati mmene tate amacitila ndi ana ake. 12 Tinali kucita zimenezi kuti mupitilize kuyenda m’njila imene Mulungu amafuna. Iye ndi amene anakuitanani ku Ufumu wake ndi ulemelelo wake.

13 Ndithudi, mpake kuti ifenso timayamika Mulungu mosalekeza, cifukwa pamene munalandila mau a Mulungu amene munamva kwa ife, simunawalandile monga mau a anthu ai, koma mmene alilidi, monga mau a Mulungu. Mau amenewa akugwilanso nchito mwa inu okhulupilila. 14 Pakuti inu abale munatengela citsanzo ca mipingo ya Mulungu imene ili mu mgwilizano ndi Khristu Yesu ku Yudeya. Tikutelo cifukwa anthu akwanu anakuzunzani, monga mmene Ayuda akuzunzila Akhristu a ku Yudeyawo. 15 Ayudawo anafika popha Ambuye Yesu komanso aneneli, ndipo ife anatizunza. Kuonjezela pamenepo, iwo sakondweletsa Mulungu, koma amatsekeleza zimene anthu onse afunikila. 16 Amacita zimenezi poyesa kutiletsa kuti tisauze anthu a mitundu ina uthenga umene ungawapulumutse. Pocita zimenezi, iwo nthawi zonse amaonjezela macimo ao. Koma tsopano mkwiyo wake wawafikila.

17 Pamene tinasiyana nanu abale kwa nthawi yocepa (pamaso-m’pamaso osati mumtima mwathu), tinayesetsa mwamphamvu kuti tikuoneni pamaso-m’pamaso* cifukwa ndi zimene tinali kulakalaka kwambili. 18 N’cifukwa cake tinali kufuna kubwela kwa inu, ndipo ine Paulo ndinayesetsa kuti ndibwele, osati kamodzi kokha koma kawili konse, kungoti Satana anachinga njila yathu. 19 Kodi ciyembekezo cathu kapena cimwemwe cathu n’ciani? Kodi mphoto imene tidzainyadile* pamaso pa Ambuye wathu Yesu, pa nthawi ya kukhalapo kwake n’ciani? Kodi si inuyo? 20 Ndithudi, inu ndinu ulemelelo wathu komanso cimwemwe cathu.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2026)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani