Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
12 Kutangotsala masiku 6 kuti Pasika acitike, Yesu anafika ku Betaniya kumene kunali Lazaro, uja amene iye anamuukitsa kwa akufa. 2 Conco, anamukonzela cakudya camadzulo kumeneko. Marita anali kuwatumikila, ndipo Lazaro anali mmodzi wa anthu omwe anali kudya* naye. 3 Ndiyeno Mariya anatenga mafuta onunkhila odula kwambili, nado weniweni, ndipo mafutawo anali okwana magalamu 327. Iye anathila mafutawo pamapazi a Yesu n’kuwapukuta ndi tsitsi lake. M’nyumba monsemo munangoti guu kafungo kabwino ka mafuta onunkhilawo. 4 Koma Yudasi Isikariyoti, mmodzi wa ophunzila ake, amene anali atatsala pang’ono kumupeleka, anati: 5 “N’cifukwa ciyani mafuta onunkhilawa sanagulitsidwe madinari 300, ndi kupeleka ndalamazo kwa osauka?” 6 Iye anakamba zimenezi osati cifukwa codela nkhawa osauka ayi, koma cifukwa cakuti anali mbala. Iye ndiye anali kusunga bokosi la ndalama, ndipo anali kubapo pandalama zoikidwa mmenemo. 7 Ndiyeno Yesu anati: “Mulekeni acite mwambo umenewu pokonzekela tsiku la kuikidwa kwanga m’manda. 8 Pakuti osaukawo muli nawo nthawi zonse, koma ine simudzakhala nane nthawi zonse.”
9 Ndiyeno khamu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali ku Betaniya. Conco linabwela osati cabe cifukwa ca Yesu, koma kudzaonanso Lazaro amene anamuukitsa kwa akufa. 10 Tsopano ansembe aakulu anakonza ciwembu cakuti aphenso Lazaro, 11 popeza Ayuda ambili anali kupita ku Betaniya, ndipo anali kukhulupilila mwa Yesu cifukwa ca Lazaroyo.
12 Tsiku lotsatila, khamu lalikulu limene linabwela ku cikondweleloco linamva kuti Yesu akubwela mu Yerusalemu. 13 Conco anatenga nthambi za kanjedza n’kupita kukamucingamila, ndipo anayamba kufuula kuti: “M’pulumutseni! Wodalitsika ndi iye wobwela m’dzina la Yehova, Mfumu ya Isiraeli!” 14 Yesu atapeza bulu wamng’ono anakwela pabuluyo monga mmene Malemba amanenela kuti: 15 “Usacite mantha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni. Taona! Mfumu yako ikubwela, itakwela pa mwana wamphongo wa bulu.” 16 Poyamba ophunzila ake sanamvetse zimenezi. Koma Yesu atapatsidwa ulemelelo, iwo anakumbukila kuti zimene anamucitilazo zinafanana ndendende ndi zimene zinalembedwa zokhudza iye.
17 Tsopano khamu limene linalipo poitana Lazaro kuti atuluke m’manda* ndi kumuukitsa kwa akufa, linapitiliza kumucitila umboni. 18 Ici n’cifukwa cina cimene cinapangitsa khamulo kupita kukamucingamila, popeza anamva kuti iye anacita cozizwitsa* cimeneci. 19 Conco Afarisi anayamba kukambilana kuti: “Mwaona, mapulani athu alephelelatu. Taonani! Dziko lonse lakhamukila kwa iye.”
20 Ndiyeno pa anthu amene anabwela kudzalambila ku cikondweleloco, panalinso Agiriki. 21 Iwo anapita kwa Filipo, wocokela ku Betsaida wa ku Galileya, ndipo anayamba kumupempha kuti: “Bambo, tikufuna kuona Yesu.” 22 Filipo anapita kukauza Andireya. Ndipo Andireya ndi Filipo anapita kukauza Yesu.
23 Koma Yesu anawayankha kuti: “Nthawi yafika yakuti Mwana wa munthu alemekezeke. 24 Ndithudi ndikukuuzani, ngati kambewu ka tiligu sikanagwele m’nthaka n’kufa, kamakhalabe kambewu kamodzi. Koma kakafa, kamabala zipatso zambili. 25 Aliyense wokonda moyo wake akuuwononga, koma aliyense amene amadana ndi moyo wake m’dziko lino akuuteteza kuti akapeze moyo wosatha. 26 Ngati munthu akufuna kunditumikila, anditsatile. Ndipo kumene ine ndidzakhala, mtumiki wanga adzakhalanso komweko. Aliyense wonditumikila, Atate adzamulemekeza. 27 Tsopano ndavutika kwambili mumtima,* kodi ndinene ciyani? Atate, ndipulumutseni ku nthawi iyi. Komabe ndiye cifukwa cake ndinabwela kuti nthawiyi indifikile. 28 Atate lemekezani dzina lanu.” Ndiyeno kunamveka mawu kucokela kumwamba akuti: “Ndalilemekeza ndipo ndidzalilemekezanso.”
29 Gulu la anthu amene anaimilila pamalopo atamva mawuwo, anayamba kukamba kuti kwagunda bingu. Ena anali kunena kuti: “Mngelo wakamba naye.” 30 Yesu anawauza kuti: “Mawuwa amveka osati cifukwa ca ine, koma cifukwa ca inu. 31 Tsopano dzikoli likuweluzidwa. Wolamulila wa dzikoli aponyedwa kunja tsopano. 32 Koma ndikadzakwezedwa* m’mwamba padziko lapansi, ndidzabweletsa anthu a mtundu uliwonse kwa ine.” 33 Ananena zimenezi pofuna kuonetsa mmene adzafela pakangopita nthawi yocepa. 34 Ndiyeno gulu la anthulo linamuyankha kuti: “Tinamva m’Cilamulo kuti Khristu adzakhalako kosatha. Nanga n’cifukwa ciyani mukukamba kuti Mwana wa munthu ayenela kukwezedwa m’mwamba?* Kodi Mwana wa munthu ameneyo ndani?” 35 Yesu anawauza kuti: “Kuwala kudzakhalabe nanu kwa kanthawi kocepa. Yendani pamene kuwala kukalipo kuti mdima usakufikileni. Munthu aliyense woyenda mumdima sadziwa kumene akupita. 36 Pomwe kuwala kukalipo, onetsani kuti mumakhulupilila kuwalako, kuti mukhale ana a kuwala.”
Yesu atanena zimenezo, anacoka n’kukawabisala. 37 Ngakhale kuti iye anacita zozizwitsa* zambili pamaso pawo, iwo sanamukhulupililebe. 38 Zinatelo kuti mawu a mneneli Yesaya akwanilitsidwe. Iye anati: “Yehova, ndani wakhulupilila zimene wamva kwa ife?* Ndipo kodi dzanja la Yehova laonetsedwa kwa ndani?” 39 Cifukwa cimene sanakhulupilile, n’cimene Yesaya ananenso kuti: 40 “Iye wacititsa khungu maso awo, ndipo waumitsa mitima yawo kuti asaone ndi maso awo, komanso kuti mitima yawo isamvetse zinthu n’kutembenuka kuti ine ndiwacilitse.” 41 Yesaya anakamba zimenezi cifukwa anaona ulemelelo wa Khristu, ndipo anafotokoza zokhudza iye. 42 Komabe, ambili anamukhulupilila, ngakhalenso olamulila. Koma iwo sanamuvomeleze poyela cifukwa coopa Afarisi kuti angawacotse m’sunagoge. 43 Pakuti iwo anali kukonda ulemelelo wocokela kwa anthu kuposa ulemelelo wocokela kwa Mulungu.
44 Koma Yesu anafuula kuti: “Aliyense wokhulupilila ine, sakhulupilila cabe ine, koma amakhulupililanso amene anandituma. 45 Ndipo aliyense waona ine, waonanso amene anandituma. 46 Ndabwela monga kuwala m’dzikoli, kuti aliyense wondikhulupilila asapitilize kukhala mumdima. 47 Ngati munthu wamva mawu anga koma osawasunga, sindingamuweluze cifukwa ndinabwela kudzapulumutsa dziko osati kudzaliweluza. 48 Aliyense wondinyalanyaza komanso wosalandila mawu anga, pali mmodzi amene adzamuweluza. Mawu amene ndalankhula ndi amene adzamuweluza pa tsiku lothela. 49 Cifukwa sindinakambepo ciliconse congoganiza pandekha, koma Atate amene anandituma ndi amene anandilamula zimene ndiyenela kukamba ndi zimene ndiyenela kulankhula. 50 Ndipo ndikudziwa kuti lamulo limenelo ndi lothandiza anthu kudzapeza moyo wosatha. Conco, zilizonse zimene ndimakamba, ndimazikamba mogwilizana ndi zimene Atate anandiuza.”