Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
17 Yesu atakamba zinthu zimenezi, anakweza maso ake kumwamba n’kunena kuti: “Atate, nthawi yafika tsopano. Lemekezani mwana wanu kuti mwana wanuyo akulemekezeni, 2 monga mmene mwamupatsila ulamulilo pa anthu onse kuti iye apeleke moyo wosatha kwa onse amene munamupatsa. 3 Iwo adzapeza moyo wosatha akamadziwa za inu* Mulungu yekhayo woona, komanso za Yesu Khristu amene inu munamutuma. 4 Ndakulemekezani pa dziko lapansi, cifukwa cakuti ndatsiliza nchito imene munandipatsa. 5 Tsopano Atate, ndiloleni ndikhale pambali panu, ndipo mundipatse ulemelelo umene ndinali nawo pambali panu dziko lisanakhalepo.
6 “Anthu amene munandipatsa kucokela m’dzikoli ndawadziwitsa dzina lanu. Anali anu, koma munawapeleka kwa ine, ndipo iwo asunga* mawu anu. 7 Zonse zimene munandipatsa n’zocokela kwa inu, 8 cifukwa ndawapatsa mawu amene inu munandipatsa. Iwo awalandila, ndipo adziwadi kuti ndinabwela monga wokuimilani, ndipo akhulupilila kuti ndinu munandituma. 9 Conco ndikuwapemphelela. Sindikupemphelela dzikoli, koma aja amene inu munandipatsa cifukwa ndi anu. 10 Zinthu zanga zonse ndi zanu, ndipo zanu ndi zanga. Ine ndalemekezeka pakati pawo.
11 “Ine ndikucoka m’dzikoli, koma iwo akali m’dzikoli, ndipo ine ndikubwela kwa inu. Atate woyela, ayang’anileni cifukwa ca dzina lanu limene munandipatsa, kuti akhale amodzi* mmenenso inu ndi ine tilili amodzi.* 12 Pamene ndinali nawo, ndinali kuwayang’anila cifukwa ca dzina lanu limene munandipatsa. Ine ndawateteza, ndipo palibe ngakhale mmodzi amene wawonongeka kupatulapo mwana wa ciwonongeko, kuti lemba likwanilitsidwe. 13 Koma tsopano ndikubwela kwa inu, ndipo ndikukamba zimenezi m’dzikoli kuti akhale ndi cimwemwe cosefukila ngati cimene ine ndili naco. 14 Ndawapatsa mawu anu, koma dzikoli limadana nawo, cifukwa iwo sali a dzikoli, mmenenso ine sindili wa dzikoli.
15 “Sindikupempha kuti muwacotse m’dzikoli, koma kuti muwayang’anile cifukwa ca woipayo. 16 Iwo sali a dzikoli mmenenso ine sindili wa dzikoli. 17 Ayeletseni* ndi coonadi, mawu anu ndiwo coonadi. 18 Monga mmene inu munanditumizila m’dziko, inenso ndawatumiza m’dziko. 19 Ndipo ine ndikudziyeletsa cifukwa ca iwo, kuti nawonso ayeletsedwe ndi coonadi.
20 “Sindikupemphelela awa okha ayi, koma ndikupemphelelanso aliyense amene amakhulupilila mwa ine pambuyo pomvetsela zimene iwo amaphunzitsa. 21 Ndikucita izi kuti onsewo akhale amodzi monga mmene ine ndi inu Atate tilili ogwilizana, kuti nawonso akhale ogwilizana ndi ife, n’colinga coti dzikoli likhulupilile kuti ndinu munandituma. 22 Ine ndawapatsa ulemelelo umene munandipatsa kuti akhale amodzi, mmenenso ife tilili amodzi. 23 Ine ndikhale wogwilizana ndi iwo, ndipo inu mukhale wogwilizana ndi ine, n’colinga coti iwo akhale ogwilizana kwambili, kuti dziko lidziwe kuti ndinu munandituma, komanso kuti mumawakonda mmene inu mumandikondela. 24 Atate, ndikufuna kuti amene mwandipatsa akakhale kumene ine ndidzakhala, kuti iwo akaone ulemelelo umene inu mwandipatsa, cifukwa munandikonda dziko lisanakhalepo. 25 Atate Wolungama, dzikoli silikudziwani ayi, koma ine ndimakudziwani, ndipo iwowa afika podziwa kuti ndinu munandituma. 26 Ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiliza kuwadziwitsa dzinalo, kuti iwo azionetsa cikondi ngati cimene inu munandionetsa, kuti inenso ndikhale wogwilizana nawo.”