Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
11 Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anali kudwala. Anali wa m’mudzi wa Betaniya, mmenenso munali kukhala Mariya ndi m’bale wake Marita. 2 Mariyayu ndi uja amene anathila mafuta onunkhila Ambuye ndi kupukuta mapazi awo ndi tsitsi lake. Lazaro amene anali kudwala anali mlongo wake. 3 Conco azilongo akewo anatumiza uthenga kwa Yesu kuti: “Ambuye! munthu uja amene mumamukonda akudwala.” 4 Koma Yesu atamva zimenezi anakamba kuti: “Kudwalaku mapeto ake sadzakhala imfa cabe ayi, koma kudzapangitsa kuti Mulungu alandile ulemelelo, kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe cifukwa ca kudwalako.”
5 Yesu anali kukonda Marita, Mariya, ndi Lazaro. 6 Koma atamva kuti Lazaro akudwala, anakhalabe kumalo kumene anali, kwa masiku ena awili. 7 Pambuyo pa masiku awiliwo, iye anauza ophunzila ake kuti: “Tiyeni tipitenso ku Yudeya.” 8 Ndiyeno ophunzilawo anamuuza kuti: “Mphunzitsi,* posacedwapa anthu a ku Yudeya anali kufuna kukuponyani miyala, ndiye mufunanso kupita kumeneko?” 9 Yesu anayankha kuti: “Masana ali ndi maola 12 si conco? Ngati munthu akuyenda masana, sapunthwa ndi ciliconse cifukwa amaona kuwala kwa dzikoli. 10 Koma munthu akamayenda usiku, amapunthwa cifukwa mwa iye mulibe kuwala.”
11 Pambuyo pokamba zimenezi, iye ananenanso kuti: “Lazaro bwenzi lathu ali m’tulo, koma ndipita kumeneko kukamuutsa.” 12 Ndiyeno ophunzilawo anamuuza kuti: “Ambuye ngati akugona ndiye kuti adzakhala bwino.” 13 Apa Yesu anali kukamba za imfa ya Lazaro. Koma ophunzilawo anaganiza kuti anali kukamba za kugona kopumula cabe. 14 Kenako Yesu anawauza mosapita m’mbali kuti: “Lazaro wamwalila, 15 ndipo ndine wokondwa cifukwa ca inu kuti sindinali kumeneko, kuti mukhulupilile. Koma tiyeni tipite kwa iye.” 16 Conco Thomasi, wochedwanso Didimo, anauza ophunzila anzake kuti: “Nafenso tiyeni tipite, kuti tikafele naye limodzi.”
17 Pamene Yesu anali kufika kumeneko, anapeza kuti Lazaro wakhala kale m’manda* masiku anayi. 18 Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pamtunda wa makilomita pafupifupi atatu.* 19 Ndipo Ayuda ambili anabwela kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza kaamba ka imfa ya mlongo wawo. 20 Marita atamva kuti Yesu akubwela, anapita kukamucingamila, koma Mariya anatsala kunyumba. 21 Kenako Marita anauza Yesu kuti: “Ambuye, mukanakhala kuno, mlongo wanga sakanamwalila. 22 Koma ngakhale pano, ndikudziwa kuti ciliconse cimene mungamupemphe Mulungu, iye adzakupatsani.” 23 Yesu anamuuza kuti: “Mlongo wako adzauka.” 24 Marita anamuuza kuti: “Ndidziwa kuti adzauka pa kuuka kwa akufa m’tsiku lothela.” 25 Yesu anamuuza kuti: “Ine ndine kuuka ndi moyo. Aliyense wokhulupilila ine, ngakhale atamwalila adzakhalanso ndi moyo. 26 Komanso aliyense amene ali ndi moyo ndipo amandikhulupilila, sadzafa ayi. Kodi ukhulupilila zimenezi?” 27 Marita anayankha kuti: “Inde Ambuye. Ndimakhulupilila kuti ndinu Khristu Mwana wa Mulungu, amene ananenedwelatu kuti adzabwela m’dzikoli.” 28 Iye atanena zimenezi, anapita kukaitana m’bale wake n’kumuuza mseli kuti: “Mphunzitsi wabwela, ndipo akukuitana.” 29 Mariya atamva izi, ananyamuka mwamsanga n’kupita kwa Yesu.
30 Apa n’kuti Yesu asanalowe m’mudzimo. Koma anali akali pamalo pomwe Marita anakumana naye. 31 Ayuda amene anali kutonthoza Mariya m’nyumbamo ataona kuti mwamsanga watuluka n’kupita panja, anamutsatila. Iwo anaganiza kuti anali kupita kumanda* kukalila. 32 Mariya atafika kumene kunali Yesu ndi kumuona, anagwada mpaka nkhope yake pansi kumapazi a Yesu n’kumuuza kuti: “Ambuye, mukanakhala kuno, mlongo wanga sakanamwalila.” 33 Yesu ataona Mariya ndi Ayuda amene anabwela naye akulila, anadzuma cifukwa covutika mumtima* ndi kumva cisoni. 34 Iye anafunsa kuti: “Mwamuika kuti?” Iwo anayankha kuti: “Ambuye, tiyeni mukaone.” 35 Yesu anagwetsa misozi. 36 Ayuda ataona zimenezi anayamba kunena kuti: “Taonani, anali kumukonda kwambili!” 37 Koma ena a iwo anati: “Kodi munthu uyu amene anatsegula maso a munthu wakhungu uja, sakanacitapo kanthu kuti mnzakeyu asamwalile?”
38 Kenako Yesu atadzumanso cifukwa covutika mumtima, anafika kumandako.* Kwenikweni mandawo anali phanga. Ndipo analitseka ndi cimwala. 39 Yesu anati: “Cotsani cimwalaci.” Marita, mlongo wa womwalilayo anamuuza kuti: “Ambuye, apa ayenela kuti wayamba kununkha, cifukwa papita masiku anayi tsopano.” 40 Yesu anamuuza kuti: “Kodi sindinakuuze kuti ngati ukhulupilila udzaona ulemelelo wa Mulungu?” 41 Conco iwo anacotsa cimwalaco. Ndiyeno Yesu anakweza maso ake kumwamba n’kunena kuti: “Atate, ndikukuyamikani kuti mwandimva. 42 Inde, ndidziwa kuti mumandimva nthawi zonse, koma ndanena izi cifukwa ca khamu la anthu limene laimilila panoli, kuti akhulupilile kuti ndinu amene munandituma.” 43 Atakamba zimenezi, anafuula mokweza mawu kuti: “Lazaro, tuluka!” 44 Pamenepo, munthu amene anali wakufa uja anatuluka, ndipo mapazi ndi manja ake anali okulungidwa ndi nsalu, nkhope yake nayonso inali yokulungidwa ndi nsalu. Yesu anawauza kuti: “M’masuleni kuti akwanitse kuyenda.”
45 Conco, Ayuda ambili amene anabwela kwa Mariya n’kuona zimene Yesu anacitazo, anamukhulupilila. 46 Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi n’kukawauza zimene Yesu anacita. 47 Conco, ansembe aakulu ndi Afarisi anasonkhanitsa Khoti Yaikulu ya Ayuda* n’kukamba kuti: “Kodi ticite ciyani popeza munthu uyu akucita zozizwitsa* zambili? 48 Ngati tingamulekelele, onse adzamukhulupilila, ndipo Aroma adzabwela n’kudzatilanda malo* athu ndi mtundu wathu.” 49 Koma mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe caka cimeneco, anawauza kuti: “Palibe cimene mudziwa inu, 50 ndipo simukuona kuti n’caphindu kwa inu kuti munthu mmodzi afele anthu ambili m’malo mwakuti mtundu wonse uwonongeke.” 51 Iye sanakambe zimenezi mongoganiza pa iye yekha, koma cifukwa anali mkulu wa ansembe caka cimeneco, analosela kuti Yesu adzafela mtunduwo. 52 Ndipo osati cabe kufela mtundu, koma kusonkhanitsanso pamodzi ana a Mulungu amene anamwazikana. 53 Cotelo kuyambila tsiku limenelo anamukonzela ciwembu cakuti amuphe.
54 Conco, Yesu sanali kuyendanso moonekela pakati pa Ayuda, koma anacoka kumeneko n’kupita kucigawo cakufupi ndi cipululu, mumzinda wochedwa Efuraimu, ndipo anakhala kumeneko pamodzi ndi ophunzila ake. 55 Tsopano Pasika wa Ayuda anali atayandikila, ndipo anthu ambili ocokela kumadela a kumidzi anapita ku Yerusalemu Pasikayo asanayambe, kuti akacite mwambo wa kudziyeletsa. 56 Iwo anali kusakila Yesu, ndipo ataimilila m’kacisimo, anali kukambilana kuti: “Muganiza bwanji? Kodi ameneyu sabwela ku cikondweleloci?” 57 Koma ansembe aakulu ndi Afarisi analamula kuti ngati wina wadziwa kumene Yesu ali, awadziwitse kuti akamugwile.*