Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
13 Tsopano cikondwelelo ca Pasika cisanafike, Yesu anadziwilatu kuti nthawi yake yakuti acoke m’dzikoli n’kupita kwa Atate wake yakwana. Iye anawakonda kwambili ophunzila ake amene anali m’dzikoli, moti anawakonda mpaka pamapeto a moyo wake. 2 Cakudya camadzulo cili mkati, Mdyelekezi anali ataika kale maganizo ofuna kupeleka Yesu mumtima mwa Yudasi Isikariyoti, mwana wa Simoni. 3 Conco Yesu podziwa kuti Atate wake anapeleka zinthu zonse m’manja mwake, ndiponso kuti anacokela kwa Mulungu komanso kuti anali kupita kwa Mulungu, 4 ananyamuka pa cakudya camadzuloco, ndipo anavula malaya ake akunja n’kuwaika pambali. Ndiyeno anatenga thaulo n’kulimanga m’ciuno mwake. 5 Atatelo, anaika madzi m’beseni n’kuyamba kusambika mapazi a ophunzila ake, ndi kuwapukuta ndi thaulo limene anamanga m’ciuno lija. 6 Kenako anafika pa Simoni Petulo. Iye anafunsa Yesu kuti: “Ambuye, mufuna kusambika mapazi anga?” 7 Yesu anamuyankha kuti: “Zimene ndikucita sungazimvetse pakali pano, koma udzazimvetsa pambuyo pake.” 8 Petulo anamuuza kuti: “Koma sindilola m’pang’ono pomwe kuti musambike mapazi anga.” Yesu anamuyankha kuti: “Ngati sindikusambika, ulibe gawo kwa ine.” 9 Simoni Petulo anamuuza kuti: “Ambuye, musangosambika mapazi anga okha ayi, koma mundisambikenso manja ndi mutu womwe.” 10 Yesu anamuuza kuti: “Amene wasamba m’thupi amangofunika kusamba mapazi okha basi, cifukwa thupi lonse ndi loyela. Ndipo inu ndinu oyela, koma osati nonsenu.” 11 Iye anali kudziwa munthu amene anali kudzamupeleka. N’cifukwa cake anati: “Sikuti nonsenu ndinu oyela.”
12 Atatsiliza kuwasambika mapazi, n’kuvalanso malaya ake akunja, anakhalanso pathebulo n’kuwafunsa kuti: “Kodi mwadziwa cifukwa cake ndasambika mapazi anu? 13 Inu mumandichula kuti ‘Mphunzitsi’ komanso ‘Ambuye,’ ndipo mumalondola cifukwa ndinedi Mphunzitsi komanso Ambuye. 14 Conco, ngati ine Ambuye komanso Mphunzitsi ndasambika mapazi anu, inunso muyenela kusambikana mapazi wina ndi mnzake. 15 Cifukwa ndakupatsani citsanzo, kuti monga mmene ine ndacitila kwa inu, inunso muzicita cimodzimodzi. 16 Ndithudi ndikukuuzani, kapolo saposa mbuye wake, ndiponso wotumidwa saposa womutuma. 17 Ngati mumazidziwa zinthu zimenezi, mudzakhala acimwemwe mukamazicita. 18 Sindikunena nonsenu, ndidziwa amene ndawasankha. Koma zimenezi zacitika kuti lemba likwanilitsidwe, limene limati: ‘Amene anali kudya cakudya canga, wanyamula kadenene kake n’kundiukila.’* 19 Tsopano ndikukuuzani izi zisanacitike, kuti zikadzacitika mukakhulupilile kuti munthu uja munali kuyembekezela ndine. 20 Ndithudi ndikukuuzani, aliyense wolandila munthu wotumidwa ndi ine walandilanso ine, ndipo aliyense amene walandila ine, walandilanso iye amene anandituma.”
21 Atakamba zimenezi, Yesu anavutika mumzimu, ndipo anacitila umboni kuti: “Ndithudi ndikukuuzani, mmodzi wa inu andipeleka.” 22 Ophunzila ake anayamba kupenyanapenyana, cifukwa sanadziwe kuti iye anali kukamba ndani. 23 Mmodzi wa ophunzilawo, amene Yesu anali kumukonda, anali khale pafupi ndi Yesu.* 24 Ndiyeno Simoni Petulo anamugumulila mutu ameneyo n’kumuuza kuti: “Tiuze, akunena ndani.” 25 Wophunzilayo anatsamila pacifuwa ca Yesu n’kumufunsa kuti: “Ambuye, mukukamba ndani?” 26 Yesu anayankha kuti: “Ndi amene ndipatse cidutswa ca mkate cimene ndisunse.” Atasunsa cidutswaco anapatsa Yudasi, mwana wa Simoni Isikariyoti. 27 Yudasi atalandila cidutswa ca mkateco, Satana analowa mwa iye. Pamenepo Yesu anamuuza kuti: “Zimene ufuna kucita uzicite mwamsanga.” 28 Koma amene anali nawo pathebulopo sanadziwe cifukwa cimene anamuuzila zimenezi. 29 Ena anaganiza kuti, popeza Yudasi anali kusunga bokosi la ndalama, ndiye kuti Yesu anali kumuuza kuti, “Ugule zofunikila pacikondwelelo,” kapena ayenela kupeleka kenakake kwa osauka. 30 Conco Yudasi atalandila cidutswa ca mkateco, anatuluka panja nthawi yomweyo ndipo unali usiku.
31 Yudasi atatuluka, Yesu anati: “Tsopano Mwana wa munthu walemekezedwa, ndipo Mulungu walemekezedwa kudzela mwa iye. 32 Mulungu iye mwini amulemekeza, ndipo amulemekeza nthawi yomwe ino. 33 Inu anzanga apamtima, ndikhala nanu kwa kanthawi kocepa cabe. Mudzandifunafuna, ndipo monga ndinauzila Ayuda kuti, ‘Kumene ndidzapite, inu simudzakwanitsa kufikako,’ inunso ndikukuuzani zimenezi. 34 Ndikukupatsani lamulo latsopano kuti muzikondana, monga mmene ine ndakukondelani, inunso muzikondana cimodzimodzi. 35 Mukamakondana wina ndi mnzake, onse adzadziwa kuti ndinu ophunzila anga.”
36 Simoni Petulo anamufunsa kuti: “Ambuye, mukupita kuti?” Yesu anayankha kuti: “Kumene ndikupita, simungandilondole pali pano, koma mudzandilondola m’tsogolo.” 37 Petulo anamufunsanso kuti: “Ambuye, n’cifukwa ciyani sindingakulondoleni pali pano? Ine ndidzapeleka moyo wanga cifukwa ca inu.” 38 Yesu anayankha kuti: “Kodi udzapeleka moyo wako cifukwa ca ine? Ndithudi ndikukuuza, tambala asanalile, iwe undikana katatu.”