LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 23
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Paulo alankhula pamaso pa Khoti Yaikulu ya Ayuda (1-10)

      • Ambuye alimbikitsa Paulo (11)

      • Ciwembu cofuna kupha Paulo (12-22)

      • Paulo atumizidwa ku Kaisareya (23-35)

Macitidwe 23:1

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “Sanihedirini.”

Macitidwe 23:8

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “amalengeza poyela.”

Macitidwe 23:11

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    11/2020, tsa. 13

Macitidwe 23:16

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu Kabuku ka Misonkhano,

    1/2019, tsa. 3

Macitidwe 23:23

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “mahosi.”

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “pafupifupi ola lacitatu.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 23:1-35

Macitidwe a Atumwi

23 Paulo anayang’anitsitsa Bungwe Lalikulu la Ayuda,* ndipo anati: “Amuna inu, abale, ndacita zinthu popanda cikumbumtima canga kunditsutsa ngakhale pang’ono, pamaso pa Mulungu mpaka lelo.” 2 Atamva izi, Hananiya mkulu wa ansembe analamula anthu amene anaimilila naye pafupi kuti amubwanyule kukamwa. 3 Kenako Paulo anamuuza kuti: “Uona, Mulungu akukantha, cipupa copaka laimu iwe. Wakhala apo kuti undiweluze motsatila Cilamulo, kodi ukuphwanyanso Cilamuloco polamula kuti andimenye?” 4 Amene anaimilila pafupi naye anati: “Kodi ukunyoza mkulu wa ansembe wa Mulungu?” 5 Ndiyeno Paulo anati: “Abale, sindinadziwe kuti ndi mkulu wa ansembe. Pakuti Malemba amati, ‘Usanenele zacipongwe wolamulila wa anthu a mtundu wako.’”

6 Lomba Paulo ataona kuti ena a iwo anali Asaduki, koma ena anali Afarisi, anafuula m’Bungwe Lalikulu la Ayuda kuti: “Amuna inu, abale anga, ine ndine Mfarisi, mwana wa Afarisi. Pano ndikuweluzidwa cifukwa ca ciyembekezo cakuti akufa adzauka.” 7 Cifukwa cakuti anakamba zimenezi, mkangano waukulu unabuka pakati pa Afarisi ndi Asaduki, ndipo gululo linagawikana. 8 Pakuti Asaduki amakamba kuti kulibe ciukitso, komanso kulibe angelo kapena colengedwa cauzimu. Pamene Afarisi amakhulupilila* kuti zonsezi zilipo. 9 Conco panabuka ciphokoso, ndipo alembi ena a m’gulu la Afarisi anaimilila n’kuyamba kutsutsa mwaukali kuti: “Munthu uyu sitinamupeze ndi mlandu wina ulionse, koma ngati mzimu kapena mngelo wakamba naye—.” 10 Mkanganowo utakula kwambili, mkulu wa asilikali anaopa kuti anthuwo adzamukhadzulakhadzula Paulo. Conco analamula asilikali kuti apite akamucotse pa gululo n’kupita naye kumalo okhala asilikali.

11 Koma tsikulo usiku, Ambuye anaimilila pafupi ndi Paulo n’kumuuza kuti: “Limba mtima! Cifukwa wandicitila umboni mokwanila mu Yerusalemu, ndipo uyenela kukandicitilanso umboni ku Roma.”

12 Kutaca, Ayuda anakonza ciwembu ndipo analumbila mocita kudzitembelela kuti sadzadya kapena kumwa kalikonse mpaka atapha Paulo. 13 Panali amuna opitilila 40 amene anakonza ciwembu cocita kulumbilaci. 14 Amunawa anapita kwa ansembe aakulu ndi akulu n’kuwauza kuti: “Ife talumbila mocita kudzitembelela kuti sitidzadya kalikonse mpaka titapha Paulo. 15 Tsopano inu ndi Bungwe Lalikulu la Ayuda muuze mkulu wa asilikali kuti abweletse Paulo kwa inu ngati kuti mukufuna kumvetsa bwino nkhani yake. Koma asanafike, ife tidzakhala okonzeka kumupha.”

16 Koma mwana wamwamuna wa mlongosi wake wa Paulo atamva za ciwembuci, cakuti akamukhalizila panjila, anapita kumalo okhala asilikali kukam’tsina khutu Paulo za ciwembuco. 17 Ndiyeno Paulo anaitana mmodzi wa atsogoleli a asilikali n’kumuuza kuti: “Tengani mnyamatayu mupite naye kwa mkulu wa asilikali, cifukwa ali naye mawu.” 18 Conco anamutenga n’kupita naye kwa mkulu wa asilikali, ndipo anamuuza kuti: “Paulo mkaidi uja anandiitana n’kundipempha kuti ndibweletse mnyamatayu kwa inu cifukwa ali nanu mawu.” 19 Mkulu wa asilikali uja anamugwila dzanja mnyamatayo nʼkupita naye pambali ndi kumufunsa kuti: “Kodi ukufuna kundiuza ciyani?” 20 Iye anati: “Ayuda agwilizana zokupemphani kuti mawa mukapeleke Paulo ku Bungwe Lalikulu la Ayuda ngati kuti akufuna kumvetsa bwino mlandu wake. 21 Koma musalole kuti akunyengeleleni, cifukwa amuna opitilila 40 afuna kumubisalila panjila. Iwo alumbila mocita kudzitembelela kuti sadzadya kapena kumwa kalikonse mpaka atamupha. Panopa ndi okonzeka, ndipo akungoyembekezela cilolezo canu.” 22 Mkulu wa asilikaliyo anauza mnyamatayo kuti azipita atamulamula kuti: “Usauze aliyense kuti wandidziwitsa zimenezi.”

23 Ndiyeno anaitanitsa atsogoleli awili a asilikali nʼkuwauza kuti: “Uzani asilikali 200 kuti akonzekele kupita ku Kaisareya. Muuzenso amuna 70 okwela pa mahachi* ndi asilikali 200 onyamula mikondo kuti apite ca m’ma 9 koloko* usiku uno. 24 Mupelekenso mahosi oti Paulo akwelepo kuti akafike ali wotetezeka kwa bwanamkubwa Felike.” 25 Ndipo analembanso kalata yokhala ndi mawu akuti:

26 “Ine Kalaudiyo Lusiya, ndikulembela inu Wolemekezeka Bwanamkubwa Felike: Landilani moni! 27 Munthu uyu Ayuda anamugwila ndipo anatsala pangʼono kumupha. Koma ine ndinabwela mwamsanga ndi asilikali anga n’kumupulumutsa, cifukwa ndinamva kuti iye ndi nzika ya Roma. 28 Ndipo pofuna kudziwa cimene analakwa, ndinapita naye ku Bungwe Lalikulu la Ayuda. 29 Ndinapeza kuti iwo akumuimba mlandu pa nkhani zokhudza Cilamulo cawo. Koma analibe mlandu ulionse woti n’kuphedwa nawo kapena kumutsekela m’ndende. 30 Koma cifukwa cakuti ciwembu cimene anakonzela munthuyu ine ndacidziwa, ndikumutumiza kwa inu, ndipo ndalamula omuimba mlanduwo kuti adzanene mlandu wake pamaso panu.”

31 Conco asilikaliwo anatenga Paulo mogwilizana ndi zimene analamulidwa n’kupita naye ku Antipatiri usiku. 32 Tsiku lotsatila analola amuna okwela pa mahachi kuti apitebe naye, koma iwo anabwelela kumalo okhala asilikali. 33 Amuna okwela pa mahachi aja anafika ku Kaisareya n’kupeleka kalata ija kwa bwanamkubwa ndipo anapelekanso Paulo kwa iye. 34 Conco iye anaiwelenga kalatayo, ndipo anafunsa Paulo cigawo cimene anali kucokela. Iye anamuuza kuti anali kucokela ku Kilikiya. 35 Kenako iye anati: “Ndimvetsela mlandu wako wonse anthu okuimba mlanduwo akafika.” Ndipo analamula kuti amusunge m’nyumba ya Mfumu Herode n’kumamulonda.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani