Wolembedwa na Mateyo
1 Buku lofotokoza mbili ya* Yesu Khristu* mwana wa Davide, mwana wa Abulahamu:
2 Abulahamu anabeleka Isaki;
Isaki anabeleka Yakobo;
Yakobo anabeleka Yuda na abale ake;
3 Yuda anabeleka Perezi na Zera mwa Tamara;
Perezi anabeleka Hezironi;
Hezironi anabeleka Ramu;
4 Ramu anabeleka Aminadabu;
Aminadabu anabeleka Nasoni;
Nasoni anabeleka Salimoni;
5 Salimoni anabeleka Boazi mwa Rahabe;
Boazi anabeleka Obedi mwa Rute;
Obedi anabeleka Jese;
6 Jese anabeleka Davide mfumu.
Davide anabeleka Solomo mwa mkazi yemwe anali wa Uriya;
7 Solomo anabeleka Rehabiyamu;
Rehabiyamu anabeleka Abiya;
Abiya anabeleka Asa;
8 Asa anabeleka Yehosafati;
Yehosafati anabeleka Yehoramu;
Yehoramu anabeleka Uziya;
9 Uziya anabeleka Yotamu;
Yotamu anabeleka Ahazi;
Ahazi anabeleka Hezekiya;
10 Hezekiya anabeleka Manase;
Manase anabeleka Amoni;
Amoni anabeleka Yosiya;
11 Yosiya anabeleka Yekoniya na abale ake, Ayuda atatsala pang’ono kutengedwa ukapolo kupita ku Babulo.
12 Ku Babuloko, Yekoniya anabeleka Salatiyeli;
Salatiyeli anabeleka Zerubabele;
13 Zerubabele anabeleka Abiyudi;
Abiyudi anabeleka Eliyakimu;
Eliyakimu anabeleka Azoro;
14 Azoro anabeleka Zadoki;
Zadoki anabeleka Akimu;
Akimu anabeleka Eliyudi;
15 Eliyudi anabeleka Eliyezara;
Eliyezara anabeleka Matani;
Matani anabeleka Yakobo;
16 Yakobo anabeleka Yosefe mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabeleka Yesu, wochedwa Khristu.
17 Conco mibadwo yonse, kucokela pa Abulahamu kukafika pa Davide inalipo 14; kucokela pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babulo, panali mibadwo 14; ndipo kucokela pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babulo, mpaka kukafika pa Khristu panali mibadwo 14.
18 Koma kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motele: Pa nthawi imene Mariya mayi ake anali wotomeledwa kwa Yosefe, Mariyayo anapezeka kuti ali na pathupi mwa mzimu woyela* asanatengane. 19 Komabe, cifukwa mwamuna* wake Yosefe anali wolungama, ndipo sanafune kumunyazitsa kwa anthu, anaganiza zomusudzula mwamseli. 20 Koma ataiganizila mofatsa nkhaniyi, mngelo wa Yehova* anaonekela kwa iye m’maloto, n’kumuuza kuti: “Yosefe, mwana wa Davide, usaope kutengela mkazi wako Mariya ku nyumba, cifukwa pathupi pamene alinapo pakhala mwa mzimu woyela. 21 Iye adzabeleka mwana wamwamuna ndipo udzamuche Yesu,* cifukwa iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku macimo awo.” 22 Zonsezi zinacitikadi, ndipo zinakwanilitsa mawu amene Yehova anakamba kudzela mwa mneneli wake, akuti: 23 “Tamvelani! Namwali adzakhala na pathupi n’kubeleka mwana wamwamuna, ndipo adzamucha Emanuweli.” Dzinali polimasulila limatanthauza kuti “Mulungu Ali Nafe.”
24 Kenako Yosefe anauka n’kucita zimene mngelo wa Yehova anamulangiza. Anatengela mkazi wakeyo ku nyumba. 25 Koma sanagone naye mkaziyo kufikila atabeleka mwana wamwamuna, ndipo Yosefe anacha mwanayo dzina lakuti Yesu.