LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 27
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Paulo ayamba ulendo wa panyanja wopita ku Roma (1-12)

      • Namondwe awomba ngalawa (13-38)

      • Ngalawa ipasuka (39-44)

Macitidwe 27:9

Mawu amunsi

  • *

    Nthawiyi inali mwezi wa Tishiri, pomwe mvula imayamba komanso nyanja imawinduka

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yogawila),

    na. 5 2017 tsa. 9

Macitidwe 27:10

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yogawila),

    na. 5 2017 tsa. 9

Macitidwe 27:14

Mawu amunsi

  • *

    Imeneyi ndi mphepo yocokela kumpoto cakum’mawa.

Macitidwe 27:16

Mawu amunsi

  • *

    Bwatoli linali lopulumukilamo.

Macitidwe 27:24

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    9/2016, masa. 15-16

Macitidwe 27:41

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “inatitimila.”

Macitidwe 27:42

Mawu amunsi

  • *

    Ena amati, “kusambila.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
  • 38
  • 39
  • 40
  • 41
  • 42
  • 43
  • 44
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 27:1-44

Macitidwe a Atumwi

27 Tsopano ulendo wathu wa pamadzi wopita ku Italy utatsimikizika, Paulo ndi akaidi ena anapelekedwa m’manja mwa mtsogoleli wa asilikali dzina lake Yuliyo, wa m’gulu la asilikali a Augusito. 2 Tinakwela ngalawa ya ku Adiramutiyo imene inali itatsala pang’ono kunyamuka ulendo wopita ku madoko a m’mbali mwa nyanja m’cigawo ca Asia. Ndiyeno tinanyamuka pamodzi ndi Arisitako Mmakedoniya wa ku Tesalonika. 3 Tsiku lotsatila tinakafika ku Sidoni, ndipo Yuliyo anacita zinthu mokoma mtima kwa Paulo moti anamulola kupita kwa mabwenzi ake kuti akamusamalile.

4 Titapitiliza ulendo wa panyanja kucokela kumeneko, tinayenda m’mbali mwa cisumbu ca Kupuro cimene cinali kutichingila ku mphepo imene inali kuwomba kucokela kumene tinali kupita. 5 Tinayenda panyanja molambalala kupitila ca ku Kilikiya ndi Pamfuliya, ndipo tinakafika pa doko la Mura ku Lukiya. 6 Kumeneko, mtsogoleli wa asilikali anapeza ngalawa ya ku Alekizandiriya yomwe inali kupita ku Italy, ndipo anatiuza kuti tikwele mmenemo. 7 Titayenda pang’onopang’ono kwa masiku angapo tinafika ku Kinido, koma movutikila. Cifukwa ca mphepo imene inali kuwomba kucokela kutsogolo, tinapitila ku Salimone kuti cisumbu ca Kerete cititeteze ku mphepoyo. 8 Titayenda movutikila m’mbali mwa cisumbu cimeneci, tinafika pamalo ena ochedwa Madoko Okoma, amene anali pafupi ndi mzinda wa Laseya.

9 Tsopano panali patapita kale nthawi yaitali, ndipo kuyenda panyanja kunali koopsa cifukwa ngakhale nthawi ya kusala kudya kwa Tsiku la Mwambo Wophimba Macimo* linali litadutsa kale. Conco Paulo anapeleka malangizo. 10 Iye anawauza kuti: “Anthu inu, ndikuona kuti ulendowu tikauyamba palipano utiwonongetsa zambili. Utiwonongetsa katundu, ngalawa, ngakhalenso miyoyo yathu.” 11 Koma mtsogoleli wa asilikali anamvela woyendetsa ngalawa ndi mwini ngalawayo m’malo momvela zimene Paulo anakamba. 12 Popeza kuti dokolo silinali bwino kukhalapo m’nyengo yozizila, ambili anakamba kuti zingakhale bwino atacokako. Iwo anali kufuna kuona ngati zingatheke kukakhala ku Finikesi m’nyengo yozizila. Finikesi linali doko la ku Kerete lopenya kumpoto cakum’mawa, komanso kum’mwela cakum’mawa.

13 Mphepo yakum’mwela itayamba kuwomba pang’onopang’ono, iwo anaganiza kuti colinga cawo cidzatheka. Conco anakweza nangula nʼkuyamba kuyenda mʼmbali mwa cisumbu ca Kerete. 14 Koma posapita nthawi, namondwe wochedwa Yulakilo* anayamba kuwomba ngalawayo. 15 Pomwe ngalawayo inali kuwombedwa ndi mphepo yamphamvu, sitinathe kuiwongolela kuti iziyenda mopenyana ndi mphepoyo. Conco tinagonja ndipo tinatengedwa nayo. 16 Ndiyeno tinayenda mʼmbali mwa cisumbu cina cacingʼono cochedwa Kauda cimene cinali kutiteteza ku mphepoyo. Koma tinavutika kwambili kuti titeteze bwato* laling’ono limene ngalawayo inali kukoka. 17 Koma atakokela bwatolo mʼngalawa, anayamba kumanga ngalawayo ndi zomangila kuti ilimbe. Poopa kuti ngalawayo ingatitimile mu mcenga ku Suriti, iwo anatsitsa nthambo zomangila cinsalu ca ngalawa moti inali kukankhidwa ndi mphepo. 18 Cifukwa cakuti tinali kukankhidwa ndi cimphepo camphamvu, tsiku lotsatila anthu anayamba kutaya katundu kuti ngalawa ipepuke. 19 Tsiku lacitatu, anataya nthambo zokwezela cinsalu ca ngalawayo.

20 Titaona kuti dzuwa komanso nyenyezi sizinaonekele kwa masiku ambili, ndipo namondwe uja anali kutikankha mwamphamvu, tinayamba kukayikila ngati tipulumuka. 21 Anthu aja atakhala nthawi yaitali osadya kalikonse, Paulo anaimilila pakati pawo n’kukamba kuti: “Anthu inu mukanamvela malangizo anga akuti tisanyamuke ulendo kucoka ku Kerete, sitikanavutika conci komanso sitikanawonongetsa katundu. 22 Ngakhale n’telo, ndikukulimbikitsani kuti musataye mtima cifukwa palibe amene adzafa, koma ngalawa yokhayi ndi imene iwonongeke. 23 Lelo usiku, mngelo wa Mulungu wanga amene ndikumucitila utumiki wopatulika, anaimilila pafupi ndi ine. 24 Iye wandiuza kuti: ‘Usaope Paulo. Uyenela kukaima pamaso pa Kaisara. Ndipo dziwa kuti Mulungu adzapulumutsa anthu onse amene uli nawo pa ulendowu cifukwa ca iwe.’ 25 Conco limbani mtima anthu inu, cifukwa ine ndikhulupilila kuti zonse zicitika mmene Mulungu wandiuzila. 26 Komabe, ngalawa yathuyi idzapasuka pafupi ndi cisumbu cinacake.”

27 Pa usiku wa nambala 14, mphepo inali kutikankhila uku ndi uku panyanja ya Adiriya. Kenako pakati pa usiku, oyendetsa ngalawa anayamba kuganiza kuti akuyandikila kumtunda. 28 Iwo anapima kuzama kwa nyanja nʼkupeza kuti ndi mamita 36. Atayendako pangʼono anapimanso kuzama kwake nʼkupeza kuti ndi mamita 27. 29 Poopa kuti tidzagunda miyala, anatsitsa anangula anayi kumbuyo kwa ngalawayo, ndipo anali kungolakalaka kuti kuce. 30 Koma oyendetsa ngalawayo anali kufuna kuthawamo. Conco iwo anayamba kutsitsila bwato laling’ono lija panyanja ponamizila kuti akufuna kutsitsa anangula amene anali kutsogolo kwa ngalawayo. 31 Conco Paulo anauza mtsogoleli wa asilikali ndi asilikaliwo kuti: “Ngati anthu awa acoke mʼngalawa ino, simupulumuka.” 32 Kenako asilikali aja anadula nthambo za bwatolo nʼkulileka kuti lipite.

33 Kutatsala pangʼono kuca, Paulo analimbikitsa anthu onsewo kuti adye cakudya. Anati: “Lelo ndi tsiku la 14 kucokela pamene munayamba kuyembekezela muli ndi nkhawa, ndipo simunadye kalikonse. 34 Conco, ndikukulimbikitsani kuti mudye kuti mukhalebe ndi moyo. Pakuti ngakhale tsitsi limodzi la m’mutu mwanu siliwonongeka.” 35 Atakamba izi, anatenga mkate n’kuyamika Mulungu pamaso pa onse. Kenako anaunyemanyema n’kuyamba kudya. 36 Conco onse analimba mtima n’kuyamba kudya. 37 Tonse pamodzi tinalimo anthu 276 m’ngalawamo. 38 Atadya n’kukhuta, anataila tiligu panyanja kuti ngalawayo ipepuke.

39 Kutaca, sanadziwe kuti ali kuti, koma anaona gombe linalake lamchenga ndipo anali ofunitsitsa kuti ngati angathe akaimitse ngalawayo kumeneko. 40 Conco anadula nthambo za anangula n’kuwaleka kuti agwele m’nyanja. Anamasulanso nthambo zomangila nkhafi zopalasila. Atakweza m’mwamba nsalu yakutsogolo kwa ngalawa, anayamba kuyenda molowela ku gombelo. 41 Kenako anagunda cimulu ca mcenga comwe mafunde anali kuciwomba mbali zonse. Mbali ya kutsogolo ya ngalawayo inajomba* mu mcengawo osasunthika, ndipo mafunde amphamvu anayamba kuwomba kumbuyo kwa ngalawayo n’kuyamba kuipasula zidutswazidutswa. 42 Zitatelo, asilikali anaganiza zopha akaidi kuti pasapezeke wina aliyense wonyaya* n’kuthawa. 43 Koma mtsogoleli wa asilikali anali kufunitsitsa kuti Paulo akafike naye bwinobwino, conco anawaletsa kucita zimene anali kufunazo. Ndiyeno analamula kuti amene angathe kunyaya alumphile m’nyanja kuti akhale woyamba kukafika kumtunda. 44 Ndipo ena onse awatsatila m’mbuyo. Ena anakwela pa matabwa, ndipo ena pa zidutswa za ngalawayo. Conco onse anafika bwinobwino ku mtunda.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani