Wolembedwa na Mateyo
14 Pa nthawiyo, Herode wolamulila cigawo ca Galileya anamva za Yesu. 2 Ndipo anauza atumiki ake kuti: “Ameneyu ni Yohane M’batizi. Anaukitsidwa kwa akufa, ndiye cifukwa cake akucita nchito zamphamvu zimenezi.” 3 Herode* anali atagwila Yohane, anam’manga, na kukamuponya m’ndende cifukwa ca Herodiya mkazi wa Filipo m’bale wake. 4 Pakuti Yohane anali kumuuza kuti: “N’kosaloleka kuti inu mumukwatile mkaziyu.” 5 Koma ngakhale kuti Herode anali kufuna kupha Yohane, anali kuopa khamu la anthu cifukwa iwo anali kumuona kuti ni mneneli. 6 Koma pokondwelela tsiku la kubadwa kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodiya anavina pa cikondweleloco. Ndipo Herode anakondwela ngako na kavinidwe kake, 7 moti anamulonjeza mocita kulumbila kuti adzamupatsa ciliconse cimene angamupemphe. 8 Kenako mtsikanayo, mayi ake atacita kumuuza zoti apemphe anati: “Nipatseni mutu wa Yohane M’batizi m’mbale pompano.” 9 Mfumuyo inamva cisoni cifukwa ca zimenezi. Koma cifukwa ca lumbilo lake komanso anthu amene anali kudya naye, analamula kuti mutuwo upelekedwe. 10 Conco anatuma munthu kukamudula mutu Yohane m’ndende. 11 Mutuwo anaubweletsa m’mbale n’kuupeleka kwa mtsikanayo, ndipo iye anaupeleka kwa amayi ake. 12 Pambuyo pake ophunzila ake anabwela n’kutenga mtembo wake kukauika m’manda. Kenako anapita kukauza Yesu. 13 Yesu atamva zimenezi anakwela bwato n’kucoka kupita ku malo opanda anthu kuti akakhale kwayekha. Koma khamu la anthu litamva zimenezo linam’tsatila wapansi kucokela m’mizinda yawo.
14 Atafika ku mtunda anaona khamu lalikulu la anthu, ndipo anawamvela cisoni na kucilitsa odwala awo. 15 Koma madzulo ophunzila ake anafika kwa iye n’kumuuza kuti: “Kuno tili n’kopanda anthu ndipo nthawi yatha kale. Auzeni anthuwa azipita, akaloŵe m’midzi kuti akadzigulile cakudya.” 16 Koma Yesu anawauza kuti: “Iwo safunika kucoka; inuyo muwapatse cakudya.” 17 Iwo anamuyankha kuti: “Tilibe ciliconse pano, kupatulapo mitanda isanu ya mkate na nsomba ziŵili.” 18 Iye anati: “Zibweletseni kuno.” 19 Ndiyeno anauza khamu la anthulo kuti likhale pansi paudzu. Kenako anatenga mitanda ya mkate isanu ija na nsomba ziŵili zija, ndipo atayang’ana kumwamba anapempha dalitso. Pambuyo pake ananyema-nyema mitandayo n’kuipeleka kwa ophunzila ake, ndipo iwo anagaŵila khamulo. 20 Cotelo onse anadya n’kukhuta. Zotsala anazitola-tola ndipo zinadzala matadza 12. 21 Amene anadya anali amuna pafupi-fupi 5,000, osaŵelengelako akazi komanso ana aang’ono. 22 Ndiyeno mwamsanga anauza ophunzila ake kuti akwele bwato na kupita ku tsidya lina la nyanja, pamene iye anali kuuza anthu kuti azipita.
23 Atauza khamulo kuti lizipita, Yesu anakwela m’phili yekha-yekha kukapemphela. Anakhalabe yekha kumeneko mpaka kunada. 24 Pa nthawiyi n’kuti bwatolo lapita kutali* pakati pa nyanja. Ophunzila ake anali kuvutika kuyendetsa bwatolo cifukwa linali kuwombedwa na mafunde, popeza kunali mphepo yamphamvu. 25 Koma pa nthawi ya ulonda wacinayi m’matandakuca,* iye anafika kwa iwo akuyenda pa madzi. 26 Ophunzilawo atamuona akuyenda pa nyanja, anacita mantha n’kunena kuti: “Ni cipuku!” Ndipo anafuula mwamantha. 27 Koma nthawi yomweyo Yesu anawauza kuti: “Limbani mtima! Ndine, musacite mantha.” 28 Poyankha Petulo anati: “Ambuye, ngati ndinudi, niuzeni niyende pamadzipa kubwela kwa inu.” 29 Iye anati: “Bwela!” Conco Petulo anatuluka m’bwatomo ndipo anayamba kuyenda pamadzi kupita kumene kunali Yesu. 30 Koma atayang’ana cimphepo camphamvu anacita mantha. Ndipo atayamba kumila anakuwa, amvekele: “Ambuye, nipulumutseni!” 31 Mwamsanga Yesu anatambasula dzanja lake n’kumugwila, ndipo anamuuza kuti: “Wa cikhulupililo cocepa iwe, n’cifukwa ciyani wakayikila?” 32 Atakwela m’bwato cimphepoco cinaleka. 33 Ndiyeno amene anali m’bwatomo anamuŵelamila n’kunena kuti: “Ndinudi Mwana wa Mulungu.” 34 Ndipo anawolokela ku mtunda ku Genesareti.
35 Anthu a kumeneko atamuzindikila, anatumiza uthenga m’madela onse ozungulila, ndipo anthu anamubweletsela onse amene anali kudwala. 36 Iwo anamucondelela kuti angogwilako ulusi wopota wa m’mbali mwa covala cake cakunja, ndipo onse amene anagwila ulusiwo matenda awo anathelatu.