Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
5 Pambuyo pa izi, kunali cikondwelelo ca Ayuda, ndipo Yesu anapita ku Yerusalemu. 2 Ku Yerusalemuko, pa Geti ya Nkhosa panali dziwe limene m’Ciheberi limachedwa Betesida. Dziwelo linali ndi makonde asanu okhala ndi zipilala. 3 Anthu ambili odwala, akhungu, olemala, komanso opuwala* manja ndi miyendo anali kugona mmenemo. 4* —— 5 Kumeneko kunali munthu wina amene anali wodwala kwa zaka 38. 6 Yesu ataona munthu ameneyu ali cigonele, komanso atadziwa kuti wakhala wodwala kwa nthawi yaitali, anamufunsa kuti: “Kodi ufuna kucila?” 7 Munthu wodwalayo anamuyankha kuti: “Bambo, ndilibe munthu aliyense woti andiike m’dziweli madzi akawinduka. Ndipo ndikafuna kulowamo wina amandipitilila n’kulowamo.” 8 Yesu anamuuza kuti: “Nyamuka! Nyamula macila* akowa uyambe kuyenda.” 9 Nthawi yomweyo munthuyo anacila, ndipo ananyamula macila* ake n’kuyamba kuyenda.
Tsiku limenelo linali la Sabata. 10 Ndiye Ayudawo anayamba kuuza munthu amene anacilitsidwayo kuti: “Lelo ndi Sabata, conco sikololeka kuti unyamule macila akowo.”* 11 Koma iye anawayankha kuti: “Munthu amene wandicilitsayo ndi yemwe wandiuza kuti, ‘Nyamula macila* akowa uyambe kuyenda.’” 12 Iwo anamufunsa kuti: “Kodi ndani wakuuza kuti, ‘Nyamula macila akowa uyambe kuyenda’?” 13 Koma munthu wocilitsidwayo sanadziwe kuti anali ndani, cifukwa Yesu anali atalowa m’khamu la anthu limene linali pamenepo.
14 Pambuyo pake, Yesu anapeza munthuyo m’kacisi ndipo anamuuza kuti: “Onatu, wacila tsopano. Usakacimwenso, kuti cinthu coipa kwambili cisakakucitikile.” 15 Munthuyo anapita n’kukauza Ayuda aja kuti ndi Yesu amene wamucilitsa. 16 Pa cifukwa cimeneci, Ayuda anayamba kumuvutitsa Yesu, cifukwa anali kucita zinthu zimenezi pa Sabata. 17 Koma iye anawauza kuti: “Atate wanga akugwilabe nchito mpaka pano, inenso ndikugwilabe nchito.” 18 Mwa ici, Ayudawo anayamba kufunafuna njila yoti amuphele, cifukwa kuwonjezela pa kuphwanya Sabata, iye anali kukambanso kuti Mulungu ndi Atate wake, kudzipanga wofanana ndi Mulungu.
19 Conco Yesu poyankha anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, Mwana sangacite ciliconse congoganiza pa iye yekha, koma zokhazo zimene waona Atate wake akucita. Cifukwa zilizonse zimene Atate amacita, Mwananso amacita zomwezo, mmene Atate wake amazicitila. 20 Pakuti Atate amamukonda Mwanayo, ndipo amamuonetsa zinthu zonse zimene iwo amacita. Iwo adzamuonetsa nchito zazikulu kuposa izi kuti inu mudabwe nazo. 21 Monga mmene Atate amaukitsila akufa n’kuwapatsa moyo, nayenso Mwana amapeleka moyo kwa amene wafuna kumupatsa. 22 Pakuti Atate saweluza munthu aliyense, koma udindo wonse woweluza aupeleka kwa Mwana, 23 kuti onse azilemekeza Mwanayo monga mmene amalemekezela Atate. Munthu aliyense amene salemekeza Mwanayo, salemekezanso Atate amene anamutuma. 24 Ndithu ndikukuuzani, munthu aliyense amene wamva mawu anga ndi kukhulupilila Atate amene anandituma, adzapeza moyo wosatha. Ndipo iye sadzaweluzidwa, koma wacoka ku imfa n’kupita ku moyo.
25 “Ndithu ndikukuuzani, nthawi ikubwela ndipo ndi yomwe ino, pamene akufa adzamva mawu a Mwana wa Mulungu, ndipo amene akumvela adzakhala ndi moyo. 26 Monga mmene Atate alili ndi moyo mwa iwo eni,* alolanso Mwana kuti akhale ndi moyo mwa iye mwini. 27 Ndipo amupatsanso mphamvu zoweluza, cifukwa iye ndi Mwana wa munthu. 28 Musadabwe nazo zinthu zimenezi, cifukwa nthawi ikubwela pamene onse ali m’manda acikumbutso adzamva mawu ake 29 ndipo adzatuluka. Amene anali kucita zabwino adzauka kuti alandile moyo, koma amene anali kucita zoipa adzauka kuti aweluzidwe. 30 Sindingacite ciliconse congoganiza pa ine ndekha. Ndimaweluza mogwilizana ndi zimene ndamva, ndipo ciweluzo canga ndi colungama cifukwa ndimacita cifunilo ca amene anandituma, osati canga.
31 “Ngati ndikudzicitila ndekha umboni, ndiye kuti umboni wangawo si woona. 32 Pali wina amene amacitila umboni za ine, ndipo ndidziwa kuti umboni wokhudza ine umene amapelekawo ndi woona. 33 Munatumiza anthu kwa Yohane, ndipo iye wacitila umboni coonadi. 34 Komabe, ine sindivomeleza umboni wocokela kwa munthu, koma ndikukamba zimenezi kuti mupulumuke. 35 Munthuyo anali nyale yoyaka komanso younikila, ndipo kwa kanthawi kocepa munali ofunitsitsa kukondwela kwambili cifukwa ca kuwala kwakeko. 36 Koma ine ndili ndi umboni waukulu kuposa wa Yohane, cifukwa nchito zimene Atate wanga anandipatsa kuti ndizikwanilitse, nchitozo n’zimene ndikucita, ndipo zikucitila umboni kuti Atate ananditumadi. 37 Komanso Atate amene anandituma iwo eni akundicitila umboni. Inu simunamvepo mawu ake ndi kale lonse, kapenanso kumuona. 38 Mawu a Mulungu sanakhazikike mwa inu, cifukwa simunakhulupilile mthenga amene iye anatumiza.
39 “Mumafufuza Malemba cifukwa muganiza kuti mudzapeza moyo wosatha kudzela m’Malembawo, ndipo Malemba omwewo amacitilanso umboni za ine. 40 Koma inu simufuna kubwela kwa ine kuti mukapeze moyo. 41 Sindikufuna kulandila ulemelelo wocokela kwa anthu, 42 koma ndidziwa bwino kuti mwa inu mulibe cikondi ca Mulungu. 43 Ine ndabwela m’dzina la Atate wanga, koma simukundilandila. Munthu wina akanabwela m’dzina lake mukanamulandila. 44 Kodi mungakhulupilile bwanji pamene mukupatsana ulemelelo wina ndi mnzake, koma simukuyesetsa kupeza ulemelelo wocokela kwa Mulungu yekhayo? 45 Musaganize kuti ndidzakunenezani kwa Atate, pali wina amene amakunenezani, iye ndi Mose, amene inu mumamudalila. 46 Mukanakhulupilila Mose, mukanakhulupililanso ine, cifukwa iye analembanso za ine. 47 Koma ngati simunakhulupilile zimene analemba, mungakhulupilile bwanji mawu anga?”