LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 10
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Zitsanzo zoticenjeza zokhudza mbili ya Aisiraeli (1-13)

      • Cenjezo pa nkhani ya kulambila mafano (14-22)

        • Thebulo la Yehova komanso thebulo la ziwanda (21)

      • Ufulu komanso kuganizila ena (23-33)

        • “Muzicita zonse kuti zipeleke ulemelelo kwa Mulungu” (31)

1 Akorinto 10:4

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “linali.”

1 Akorinto 10:8

Mawu amunsi

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena.

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 97-98

1 Akorinto 10:10

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “mngelo woononga.”

1 Akorinto 10:13

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu Kabuku ka Misonkhano,

    4/2019, tsa. 3

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    2/2017, masa. 29-30

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    4/2016, masa. 10-11

    Nsanja ya Mlonda,

    4/15/2015, tsa. 26

    4/1/2014, tsa. 21

1 Akorinto 10:21

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 24

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    10/2019, tsa. 30

1 Akorinto 10:23

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 35

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, masa. 84-85

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 72-73

1 Akorinto 10:24

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 35

    Tikhalebe mu Cikondi ca Mulungu, masa. 84-85

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    10/2017, tsa. 11

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 72-73

1 Akorinto 10:31

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 43

1 Akorinto 10:32

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 43

1 Akorinto 10:33

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 52

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 10:1-33

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

10 Tsopano ndikufuna kuti mudziwe abale, kuti makolo athu akale onse anali pansi pa mtambo, ndipo anaoloka nyanja. 2 Komanso onse anabatizidwa mwa Mose kupitila mu mtambo komanso nyanja. 3 Ndipo onse anali kudya cakudya cauzimu cofanana. 4 Onse anali kumwa madzi auzimu ofanana. Cifukwa anali kumwa kucokela pathanthwe lauzimu limene linali kuwatsatila, ndipo thanthwelo litanthauza* Khristu. 5 Ngakhale n’telo, Mulungu sanakondwele ndi ambili a iwo, moti anaphedwa m’cipululu.

6 Tsopano izi zinacitika kuti zikhale citsanzo kwa ife, kuti tisamalakelake zinthu zoipa mmene iwo anacitila. 7 Komanso kuti tisamalambile mafano mmene ena a iwo anacitila, monga mmene Malemba amakambila kuti: “Anthuwo anakhala pansi kuti adye ndi kumwa, kenako anaimilila kuti asangalale.” 8 Musamacite ciwelewele* monga mmene ena a iwo anacitila, zimene zinacititsa kuti anthu 23,000 aphedwe pa tsiku limodzi. 9 Tisamamuyese Yehova mmene ena a iwo anamuyesela, iwo analumidwa ndi njoka ndipo anafa. 10 Tisakhale ong’ung’udza ngati mmene ena a iwo anang’ung’udzila, n’kuphedwa ndi mngelo wa Mulungu.* 11 Zinthuzi zinawacitikila kuti zikhale citsanzo kwa ife, ndipo zinalembedwa monga cenjezo kwa ife amene mapeto a nthawi ino atifikila.

12 Conco amene akuona kuti ali cilili asamale kuti asagwe. 13 Palibe mayeselo amene mumakumana nao osiyana ndi amene anthu ena amakumana nao. Koma Mulungu ndi wokhulupilika, ndipo sadzalola kuti muyesedwe kuposa mlingo umene simungathe kupilila. Koma pamene mukukumana ndi mayeselowo, iye adzakonza njila yopulumukila kuti mukwanitse kupilila.

14 Conco okondedwa anga, thawani kupembedza mafano. 15 Ndikukamba ndi inu ngati anthu ozindikila. Weluzani nokha ngati zimene ndikukamba ndi zoona kapena ai. 16 Kodi kapu ya madalitso imene timadalitsa, siitanthauza kugawana magazi a Khristu? Kodi mkate umene timaubenthula-benthula, sutanthauza kugawana thupi la Khristu? 17 Cifukwa cakuti pali mtanda umodzi wa mkate, ngakhale kuti ife tilipo ambili, ndife thupi limodzi. Pakuti tonse timadya mtanda umodzi wa mkatewo.

18 Ganizilani za Aisiraeli: Kodi sikuti aja amene amadya zopelekedwa nsembe amagawana ndi guwa la nsembe? 19 Ndiye ndi kukamba ciani? Kodi zopelekedwa nsembe kwa mafano ndi zaphindu, kapena fano ndi laphindu? 20 Ayi, koma ndikunena kuti, nsembe zimene anthu a mitundu ina amapeleka, amazipeleka kwa ziwanda, osati kwa Mulungu. Ndipo sindikufuna kuti inu muzigwilizana ndi ziwanda. 21 N’zosatheka kuti muzimwa za m’kapu ya Yehova ndi za m’kapu ya ziwanda. N’zosatheka kumadya “pathebulo la Yehova” komanso pathebulo la ziwanda. 22 Kodi ‘tikufuna kuti Yehova acite nsanje’?

23 Ife si ndife amphamvu kuposa iye, si conco? Zinthu zonse n’zololeka, koma si zonse zopindulitsa. Zinthu zonse n’zololeka, koma si zonse zolimbikitsa. 24 Munthu aliyense asamangofuna zopindulila iye yekha koma zopindulilanso anthu ena.

25 Muzidya ciliconse cogulitsidwa pamsika wa nyama, musamafunse mafunso pocitila cikumbumtima canu. 26 Pakuti “dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zokhala mmenemo.” 27 Ngati munthu wosakhulupilila wakuitanani, ndipo mukufuna kupita, muzidya zilizonse zimene akupatsani popanda kufunsa mafunso pocitila cikumbumtima canu. 28 Koma ngati wina wakuuzani kuti, “Izi zinapelekedwa nsembe,” musadye kucitila amene wakuuzani komanso cikumbumtima. 29 Sindikutanthauza cikumbumtima cako, koma ca munthu winayo. N’cifukwa ciani ufulu wanga uziimbidwa mlandu ndi cikumbutima ca munthu wina? 30 Ngakhale nditadya ndi kuyamika Mulungu kaamba ka cakudyaco, kodi ndicitebe zimenezo ngati sindingapangitse ena kunditsutsa?

31 Cotelo, kaya mukudya kapena kumwa, kapena kucita cina ciliconse, citani zonse kuti mupeleke ulemelelo kwa Mulungu. 32 Conco, muzipewa kukhala copunthwitsa kwa Ayuda, kwa Agiriki, komanso ku mpingo wa Mulungu. 33 Cifukwa inenso ndikuyesetsa kukondweletsa anthu onse m’zinthu zonse. Sindikucita zopindulila ine ndekha, koma zopindulilanso anthu ambili kuti apulumutsidwe.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani