Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
10 “Ndithudi ndikukuuzani, amene amalowa m’khola la nkhosa osadzela pakhomo, koma mocita kukwelela pamalo ena ake, ameneyo ndi wakuba komanso wolanda zinthu za ena. 2 Koma wolowela pakhomo ndi m’busa wa nkhosazo. 3 Mlonda wapakhomo amamutsegulila ameneyu, ndipo nkhosa zimamva mawu ake. Iye amaitana nkhosa zake mwa kuzichula maina ndi kuzitsogolela kuti zituluke. 4 Akazitulutsa nkhosa zake zonse, amazitsogolela. Ndipo nkhosazo zimamutsatila cifukwa zimadziwa mawu ake. 5 Mlendo sizingam’tsatile nkhosazo, koma zidzamuthawa, cifukwa sizidziwa mawu a alendo.” 6 Yesu anawauza fanizoli, koma iwo sanamvetse tanthauzo la zimene anali kuwauzazo.
7 Conco Yesu anakambanso kuti: “Ndithudi ndikukuuzani, ine ndine khomo la nkhosa. 8 Onse amene abwela n’kumanamizila kuti ndi abusa enieni, ndi mbala komanso olanda, ndipo nkhosa sizinawamvele. 9 Ine ndine khomo. Munthu aliyense wolowa kupitila mwa ine, adzapulumutsidwa. Ameneyo adzalowa ndi kutuluka, ndipo adzapeza msipu. 10 Mbala sibwelela cina koma kuba, kupha, ndi kuwononga. Koma ine ndabwela kuti iwo akhale ndi moyo, inde moyo wosatha. 11 Ine ndine m’busa wabwino. Ndipo m’busa wabwino amapeleka moyo wake kaamba ka nkhosa. 12 Munthu waganyu amene si m’busa komanso amene nkhosazo si zake, akaona mmbulu ukubwela amasiya nkhosazo n’kuthawa. Ndiyeno mmbuluwo umagwilapo nkhosa zina, ndipo zina zonse zimathawa n’kumwazikana. 13 Iye amatelo cifukwa ndi waganyu cabe, ndipo sasamala za nkhosazo. 14 Ine ndine m’busa wabwino. Nkhosa zanga ndimazidziwa, ndipo nazonso zimandidziwa, 15 monga mmene Atate amandidziwila, inenso ndimawadziwa. Cotelo ndikupeleka moyo wanga kaamba ka nkhosazo.
16 “Ndili ndi nkhosa zina zimene si zam’khola ili. Nazonso ndiyenela kuzibweletsa m’khola ili, ndipo zidzamvela mawu anga. Zidzakhala gulu limodzi, ndipo m’busa wawo adzakhala mmodzi. 17 Ndiye cifukwa cake Atate amandikonda cifukwa ndikupeleka moyo wanga kuti ndikaulandilenso. 18 Kulibe munthu amene angacotse moyo wanga, koma ndikuupeleka mwa kufuna kwanga. Ndili ndi mphamvu zoupeleka komanso ndili ndi mphamvu zoulandilanso. Izi n’zimene Atate wanga anandilamula kucita.”*
19 Ayuda anagawikananso cifukwa ca mawu amenewa. 20 Ambili a iwo anali kukamba kuti: “Ali ndi ciwanda ndipo wacita misala. N’cifukwa ciyani mukumumvetsela?” 21 Ena anati: “Mawu awa si a munthu wogwidwa ndi ciwanda. Kodi ciwanda cingatsegule maso a anthu akhungu?”
22 Pa nthawiyi, ku Yerusalemu kunali Cikondwelelo ca Kupatulila Kacisi. Inali nyengo yozizila, 23 ndipo Yesu anali kuyenda m’kacisimo m’khonde lokhala ndi zipilala la Solomo. 24 Ndiyeno Ayuda anamuzungulila n’kuyamba kumufunsa kuti: “Kodi udzativutitsa maganizo mpaka liti? Tiuze mosapita m’mbali ngati ndiwe Khristu.” 25 Yesu anawayankha kuti: “Ndakuuzani kale, koma simukukhulupilila. Nchito zimene ndikuzicita m’dzina la Atate wanga, zikundicitila umboni. 26 Koma simukukhulupililabe, cifukwa si ndinu nkhosa zanga. 27 Nkhosa zanga zimamvela mawu anga. Ndipo ndimazidziwa komanso zimanditsatila. 28 Ndidzazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongedwa konse. Palibenso amene adzazitsomphola m’dzanja langa. 29 Nkhosa zimene Atate andipatsa n’zofunika kwambili kuposa zinthu zina zonse, ndipo palibe amene angazitsomphole m’dzanja la Atate. 30 Ine ndi Atate ndife amodzi.”*
31 Apanso Ayuda anatola miyala kuti amuponye nayo. 32 Yesu anawauza kuti: “Ndakuonetsani nchito zabwino zambili zocokela kwa Atate. Pa nchitozo, ndi iti imene mufuna kundiponyela miyala?” 33 Ayudawo anamuyankha kuti: “Sitikufuna kukuponya miyala cifukwa ca nchito yabwino ayi, koma cifukwa conyoza Mulungu. Pakuti iwe ukudzipanga mulungu, pamene ndiwe munthu cabe.” 34 Yesu anawayankha kuti: “Kodi m’Cilamulo canu simunalembedwe kuti, ‘Ine ndinati: “Inu ndinu milungu”’?* 35 Tidziwa kuti Malemba sangathe mphamvu. Conco ngati Mulungu anachula anthu otsutsidwa ndi mawu ake kuti ‘milungu,’ 36 kodi mukuuza ine amene Atate anandiyeletsa n’kunditumiza m’dzikoli kuti, ‘Ukunyoza Mulungu,’ cifukwa ndinati, ‘Ndine Mwana wa Mulungu’? 37 Ngati sindicita nchito za Atate wanga, musandikhulupilile. 38 Koma ngati ndikuzicita, ngakhale kuti simundikhulupilila, khulupililani nchitozo, kuti mudziwe ndi kupitiliza kudziwa kuti ine ndi Atate ndife ogwilizana.” 39 Iwo anafunanso kumugwila, koma anawathawa mozemba.
40 Yesu anawolokanso Yorodano n’kupita kumalo kumene Yohane anali kubatizila anthu poyamba, ndipo anakhala kumeneko. 41 Anthu ambili anabwela kwa iye n’kuyamba kunena kuti: “Yohane sanacite cozizwitsa* ciliconse, koma zonse zimene Yohane anakamba zokhudza munthu uyu zinali zoona.” 42 Conco ambili kumeneko anamukhulupilila.