Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
4 Ambuye atazindikila kuti Afarisi anamva zakuti iyeyo* akupanga ophunzila ambili ndi kuwabatiza kuposa Yohane, 2 ngakhale kuti si Yesu amene anali kuwabatiza koma ophunzila ake, 3 anacoka ku Yudeya n’kupitanso ku Galileya. 4 Koma anafunika kudzela ku Samariya. 5 Conco, anafika mu mzinda wa Samariya wochedwa Sukari, kufupi ndi munda umene Yakobo anapatsa Yosefe mwana wake. 6 Ndipo kumeneko kunali citsime ca Yakobo. Popeza Yesu anali atalema ndi ulendo, anakhala pansi pacitsimepo.* Apo nthawi ili ca m’ma 12 koloko masana.*
7 Mayi wina wa ku Samariya anabwela kudzatapa madzi. Yesu anapempha mayiyo kuti: “Ndipatsen’koni madzi akumwa.” 8 (Ophunzila ake anali atalowa mumzinda kukagula cakudya.) 9 Conco mayi wacisamariyayo anamufunsa kuti: “Popeza inu ndinu Myuda, n’cifukwa ciyani mukundipempha madzi, ine mayi wacisamariya?” (Cifukwa Ayuda ndi Asamariya sagwilizana.) 10 Yesu anayankha mayiyo kuti: “Mukanadziwa mphatso yaulele ya Mulungu komanso amene akukupemphani kuti, ‘Ndipatsen’koni madzi akumwa,’ mukanamupempha madzi amoyo ndipo akanakupatsani.” 11 Mayiyo anamuyankha kuti: “Bambo, mulibe n’cotapila madzi, ndipo citsimeci n’cozama. Ndiye madzi a moyowo muwatenga kuti? 12 Kodi inu ndinu wamkulu kuposa Yakobo atate wathu, amene anatipatsa citsimeci, cimene iye, ana ake, komanso ng’ombe zake anali kumwapo?” 13 Yesu anamuyankha kuti: “Aliyense wakumwa madzi awa adzamvanso ludzu. 14 Koma aliyense amene adzamwe madzi amene ndidzam’patse sadzamvanso ludzu ngakhale pang’ono. Madzi amene ndidzamupatsewo, mwa iye adzakhala kasupe wotulutsa madzi opatsa moyo wosatha.” 15 Mayiyo anamuuza kuti: “Bambo, ndipatsen’koni madziwo kuti ndisadzamvenso ludzu, ndipo ndisadzabwelenso kuno kudzatapa madzi.”
16 Yesu anauza mayiyo kuti: “Pitani, mukaitane mwamuna wanu kuti abwele kuno.” 17 Mayiyo anayankha kuti: “Ndilibe mwamuna.” Yesu anamuuza kuti: “Mwakamba zoona kuti, ‘Ndilibe mwamuna.’ 18 Cifukwa mwakwatiwapo ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene muli naye pali pano si wanu. Zimene mwakambazi n’zoona.” 19 Mayiyo anati kwa iye: “Bambo, ndadziwa kuti ndinu mneneli. 20 Makolo athu anali kulambilila m’phili ili, koma anthu inu mumakamba kuti ku Yerusalemu n’kumene anthu ayenela kulambilila.” 21 Yesu anauza mayiyo kuti: “Mayi ndikhulupilileni, nthawi idzafika pamene inu simudzalambila Atate m’phili ili kapena ku Yerusalemu. 22 Inu mumalambila cimene simudziwa, koma ife timalambila cimene tidziwa, cifukwa cipulumutso cikuyambila kwa Ayuda. 23 Komabe nthawi ikubwela, ndipo ndi yomwe ino, pamene olambila oona adzalambila Atate motsogoleledwa ndi mzimu komanso coonadi. Pakuti Atate akufunafuna anthu ngati amenewa kuti azimulambila. 24 Mulungu ndi Mzimu, ndipo amene amamulambila ayenela kumulambila motsogoleledwa ndi mzimu komanso coonadi.” 25 Mayiyo anamuuza kuti: “Ndidziwa kuti Mesiya wochedwanso Khristu akubwela. Iyeyo akadzafika adzatifotokozela zinthu zonse poyela.” 26 Yesu anamuuza kuti: “Ndine amene, ineyo amene ndikulankhula nanu.”
27 Nthawi yomweyo ophunzila ake anafika, ndipo anadabwa kuona kuti iye akulankhula ndi mzimayi. Ngakhale n’telo, palibe amene anamufunsa kuti: “Mufunanji kwa iye?” kapena “N’cifukwa ciyani mukukamba ndi mayiyu?” 28 Conco mayiyo anasiya mtsuko wake wa madzi n’kupita mumzinda kukauza anthu kuti: 29 “Tiyeni mukaone munthu amene wandiuza zonse zimene ndinacita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu uja?” 30 Iwo anacoka mu mzindawo n’kupita kumene kunali Yesu.
31 Pa nthawiyi ophunzila ake anali kumupempha kuti: “Mphunzitsi,* idyani.” 32 Koma iye anawauza kuti: “Ndili naco cakudya cimene inu simucidziwa.” 33 Conco ophunzilawo anayamba kufunsana kuti: “Palibe aliyense amene wamubweletsela cakudya, alipo ngati?” 34 Yesu anawauza kuti: “Cakudya canga ndi kucita cifunilo ca amene anandituma, ndi kutsiliza nchito yake. 35 Kodi inu simukuti kwatsala miyezi inayi kuti nthawi yokolola ifike? Taonani! Ndikukuuzani kuti: Kwezani maso anu ndi kuona m’mindamo, mbewu zaca* kale kuti zikololedwe. Moti apa 36 wokolola akulandila malipilo, ndipo akusonkhanitsa zipatso ku moyo wosatha, kuti wofesa mbewu ndi wokololayo asangalalile pamodzi. 37 Ndiye cifukwa cake mawu awa ndi oona akuti: Wina ndi wofesa, ndipo wina ndi wokolola. 38 Ine ndinakutumani kuti mukakolole zimene simunagwililepo nchito. Ena anagwila nchito molimbika, ndipo inu mukupindulilapo pa nchito yawo.”
39 Asamariya ambili a mumzindawo anaika cikhulupililo mwa iye cifukwa ca mawu amene mayi uja anacitila umboni akuti: “Wandiuza zonse zimene ndinacita.” 40 Conco pamene Asamariya anafika kwa iye, anamupempha kuti akhale nawo, ndipo iye anakhala kumeneko masiku awili. 41 Zotsatilapo zake zinali zakuti, anthu ena ambili anakhulupilila cifukwa ca zimene iye ananena. 42 Conco anthuwo anauza mayiyo kuti: “Apa sikuti takhulupilila cabe cifukwa ca zimene iwe watiuza ayi, koma cifukwa tadzionela tokha, ndipo tadziwa kuti munthu ameneyu ndi mpulumutsidi wa dziko.”
43 Pambuyo pa masiku awiliwo, iye anacoka kumeneko n’kupita ku Galileya. 44 Yesu mwiniwakeyo anacitila umboni kuti mneneli salemekezedwa kwawo. 45 Conco iye atapita ku Galileya, Agalileya anamulandila, cifukwa anaona zinthu zonse zimene anacita pacikondwelelo ku Yerusalemu, popeza kuti nawonso anapita ku cikondweleloco.
46 Kenako anabwelelanso ku Kana wa ku Galileya, kuja kumene anasandutsa madzi kukhala vinyo. Kumeneko kunali munthu wina wotumikila mfumu, amene mwana wake wamwamuna anali kudwala ku Kaperenao. 47 Munthu ameneyo atamva kuti Yesu wacoka ku Yudeya ndipo wafika ku Galileya, anapita kwa iye n’kumupempha kuti abwele kudzacilitsa mwana wakeyo, pakuti anali atatsala pang’ono kufa. 48 Koma Yesu anamuuza kuti: “Popanda kuona zizindikilo ndi zodabwitsa, anthu inu simungakhulupilile.” 49 Mtumiki wa mfumuyo anamuuza kuti: “Ambuye, tiyeni mwana wanga asanamwalile.” 50 Yesu anamuuza kuti, “Pita, mwana wako ali moyo.” Munthuyo anakhulupilila mawu amene Yesu anamuuza, moti anapitadi. 51 Koma ali m’njila, akapolo ake anakumana naye kudzamuuza kuti mwana wake wamwamuna uja ali moyo.* 52 Conco iye anawafunsa ola limene mwanayo anacila. Iwo anamuyankha kuti: “Malungo* ake anatha dzulo ca m’ma 1 koloko masana.”* 53 Ndiyeno tateyo anadziwa kuti mwana wake anacila mu ola lomwe lija limene Yesu anamuuza kuti: “Mwana wako ali moyo.” Conco iye pamodzi ndi banja lake lonse anakhulupilila. 54 Ici cinali cizindikilo caciwili cimene Yesu anacita atacoka ku Yudeya n’kupita ku Galileya.