LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 6
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • Akhristu kutengelana ku makhoti (1-8)

      • Amene sadzalowa mu Ufumu wa Mulungu (9-11)

      • Lemekezani Mulungu ndi matupi anu (12-20)

        • “Thawani ciwelewele!” (18)

1 Akorinto 6:9

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “musanyengedwe.”

  • *

    Onani Matanthauzo a Mau Ena, “ciwelewele.”

  • *

    Kapena kuti, “amathanyula.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 31

1 Akorinto 6:10

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “olankhula monyoza.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 31

1 Akorinto 6:11

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 31

1 Akorinto 6:13

Mawu amunsi

  • *

    M’Cigiriki, por.nei’a. Onani Matanthauzo a Mau Ena.

1 Akorinto 6:18

Mawu amunsi

  • *

    M’Cigiriki, por.nei’a. Onani Matanthauzo a Mau Ena.

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 41

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 6:1-20

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

6 Wina wa inu akakangana ndi mnzake, kodi amalimba mtima kupita ku khoti kukaonekela pamaso pa anthu osalungama, m’malo mopita kwa oyelawo? 2 Kapena kodi simukudziwa kuti oyelawo adzaweluza dziko? Ngati inu mudzaweluza dziko, kodi simungakwanitse kuweluza milandu yaing’ono kwambili imeneyo? 3 Kodi inu simukudziwa kuti tidzaweluza angelo? Ndiye tingalephele bwanji kuweluza nkhani za mu umoyo uno? 4 Ndiye ngati muli ndi nkhani za mu umoyo uno zofunika kuweluza, kodi anthu amene mpingo sungawadalile ndiwo amene mwapatsa udindo woweluza? 5 Ndikulankhula izi kuti ndikucititseni manyazi. Kodi pakati panu palibe ngakhale mmodzi wanzelu amene angaweluze milandu ya abale ake? 6 Kodi zoona m’bale azipeleka m’bale wake kukhoti kwa anthu osakhulupilila?

7 Kukamba zoona, ngati mumatengelana kukhoti ndiye kuti mwalephela kale. Bwanji osangololela kulakwilidwa? Bwanji osangololela kubeledwa? 8 M’malomwake, inu mumacita zoipa komanso m’mabela ena ndipo m’mabelanso ngakhale abale anu.

9 Kodi inu simukudziwa kuti anthu osalungama sadzalowa mu Ufumu wa Mulungu? Musasoceletsedwe.* Anthu aciwelewele,* olambila mafano, acigololo, amuna amene amalola kugonedwa ndi amuna anzawo, amuna ogona amuna anzawo,* 10 akuba, anthu adyela, zidakwa, olalata,* kapena olanda, sadzalowa mu Ufumu wa Mulungu. 11 Ndipo ena a inu munali otelo, koma mwasambikidwa n’kukhala oyela. Mwayeletsedwa, ndipo mwaonedwa monga olungama m’dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, komanso ndi mzimu wa Mulungu wathu.

12 Zinthu zonse ndi zololeka kwa ine, koma si zonse zopindulitsa. Zinthu zonse ndi zololeka kwa ine, koma sindidzalola cinthu ciliconse kuti cizindilamulila. 13 Cakudya ndi ca mimba, ndipo mimba ndi ya cakudya, koma Mulungu adzaziononga zonsezi. Thupi ndi la Ambuye, si locitila ciwelewele,* ndipo Ambuye ndiwo amapeleka zofunikila za thupilo. 14 Koma Mulungu anaukitsa Ambuye ndipo adzaukitsanso ife mwa kugwilitsa nchito mphamvu zake.

15 Kodi inu simukudziwa kuti matupi anu ndi ziwalo za Khristu? Ndiye kodi nditenge ziwalo za Khristu n’kuzilumikiza kwa hule? Sindingayese! 16 Kodi simukudziwa kuti aliyense wogonana ndi hule amakhala thupi limodzi ndi hulelo? Pakuti Mulungu anati, “Awiliwo adzakhala thupi limodzi.” 17 Koma aliyense wogwilizana ndi Ambuye amakhala naye thupi limodzi mu mzimu. 18 Thawani ciwelewele.* Chimo lililonse limene munthu angacite ndi la kunja kwa thupi lake, koma munthu amene amacita ciwelewele amacimwila thupi lake. 19 Kodi simukudziwa kuti thupi lanu ndi kacisi wa mzimu woyela umene uli mwa inu, womwe Mulungu anakupatsani? Ndipo inu ndinu wa Mulungu, 20 popeza munagulidwa pa mtengo wokwela. Yesetsani kulemekeza Mulungu ndi matupi anu mmene mungathele.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani