LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 26
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Paulo adziteteza pamaso pa Agiripa (1-11)

      • Paulo afotokoza mmene anakhalila Mkhristu (12-23)

      • Zimene Fesito ndi Agiripa anacita (24-32)

Macitidwe 26:8

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “mukuweluza.”

Macitidwe 26:14

Mawu amunsi

  • *

    Cisonga cotokosela, ndi ndodo yosongoka imene anali kutokosela nyama za pa joko kuti ziziyenda mofulumila.

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 26:1-32

Macitidwe a Atumwi

26 Agiripa anauza Paulo kuti: “Ungalankhule mbali yako kuti udziteteze.” Ndiyeno Paulo anatambasula dzanja lake n’kuyamba kulankhula modziteteza kuti:

2 “Inu Mfumu Agiripa, ine ndine wokondwa kuti lelo ndidziteteza pa maso panu, pa zinthu zonse zimene Ayuda akundineneza. 3 Makamaka cifukwa cakuti ndinu katswili pa miyambo yonse komanso pa zimene Ayuda amakangana. Cotelo, ndikukupemphani kuti mundimvetsele moleza mtima.

4 “Ndithudi, umoyo umene ndakhala kuyambila ndili mnyamata, pakati pa anthu a mtundu wanga ndiponso mu Yerusalemu, ndi wodziwika bwino kwa Ayuda onse 5 amene akhala akundidziwa kwa nthawi yaitali. Ngati afuna angandicitile umboni, kuti ndinalidi Mfarisi wa m’gulu lokhwimitsa zinthu kwambili pa kulambila kwathu. 6 Koma cifukwa ca ciyembekezo ca zimene Mulungu analonjeza makolo athu akale ndikuimbidwa mlandu. 7 Mafuko athu 12 nawonso akuyembekezela kuona kukwanilitsidwa kwa lonjezo limeneli mwa kucita utumiki wopatulika modzipeleka usana ndi usiku. Inu Mfumu, Ayuda akundiimba mlandu cifukwa ca ciyembekezo cimeneci.

8 “N’cifukwa ciyani mukuona* kuti n’zosatheka Mulungu kuukitsa akufa? 9 Ine ndinali wotsimikiza mtima kuti ndiyenela kucita zambili zotsutsana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti. 10 Izi n’zimene ndinacitadi ku Yerusalemu. Ndipo ndinatsekela m’ndende oyela ambili cifukwa ndinapatsidwa mphamvu ndi ansembe aakulu. Akaweluzidwa kuti aphedwe, ine ndinalikuponya voti yovomeleza. 11 Nthawi zambili ndinali kuwapatsa cilango m’masunagoge onse pofuna kuwakakamiza kuti ataye cikhulupililo cawo. Popeza ndinali nditawakwiyila kwambili, ndinafika ngakhale powazunza m’mizinda yakutali.

12 “Ndili mkati mocita zimenezi, ndinanyamuka ulendo wopita ku Damasiko, nditapatsidwa mphamvu komanso cilolezo ndi ansembe aakulu. 13 Dzuwa lili paliwombo, kuwala kwakukulu koposa kuwala kwa dzuwa kunandiunika kucokela kumwamba, kunandizungulila ndipo kunazungulilanso anthu amene ndinali nawo pa ulendowo. 14 Ndiyeno tonse titagwa pansi, ndinamva mawu m’Ciheberi ondiuza kuti: ‘Saulo! Saulo! n’cifukwa ciyani ukundizunza? Ukudzivulaza wekha ngati nyama imene ikumenya zisonga zotokosela.’* 15 Koma ine ndinati: ‘Ndinu ndani Ambuye?’ Ndipo Ambuyewo anayankha kuti: ‘Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza. 16 Komabe, uka uimilile. Ndiye cifukwa cake ndaonekela kwa iwe kuti ndikusankhe kukhala mtumiki wanga, ndiponso ukhale mboni ya zinthu zimene waona komanso zinthu zimene ndidzakuonetsa zokhudza ine. 17 Ndipo ndidzakupulumutsa kwa anthu awa komanso kwa anthu a mitundu ina kumene ndikukutumizako, 18 kuti ukawatsegule maso kuwacotsa mu mdima n’kuwapititsa kowala, ndiponso kuwacotsa m’manja mwa Satana n’kuwapititsa kwa Mulungu. Ukacite zimenezi kuti macimo awo akhululukidwe, komanso kuti akalandile colowa pamodzi ndi oyeletsedwa cifukwa condikhulupilila.’

19 “Conco inu Mfumu Agiripa, ine ndinamvela masomphenya akumwambawo. 20 Kuyambila kwa anthu a ku Damasiko, ku Yerusalemu, ndiponso m’dziko lonse la Yudeya kuphatikizapo anthu a mitundu ina, ndinali kuwauza uthenga wakuti ayenela kulapa ndi kubwelela kwa Mulungu mwa kucita nchito zoonetsa kulapa. 21 Ici ndico cifukwa cimene Ayuda anandigwilila m’kacisi n’kumafuna kundipha. 22 Koma cifukwa ndaona Mulungu akundithandiza, ine ndapitiliza kucitila umboni mpaka lelo kwa anthu otsika ndiponso ochuka. Sindikunena ciliconse kupatulapo zimene aneneli komanso Mose ananena kuti zidzacitika. 23 Zakuti Khristu adzavutika, ndipo monga woyamba kuukitsidwa kwa akufa, adzalalikila kwa anthu awa komanso kwa a mitundu ina za kuwala.”

24 Pamene Paulo anali kulankhula zinthu zimenezi podziteteza, Fesito analankhula mokweza mawu kuti: “Iwe Paulo, wacita misala eti! Kuphunzila kwambili kwakufunthitsa!” 25 Koma Paulo anayankha kuti: “Inu Wolemekezeka a Fesito, ine sindinacite misala, koma ndikulankhula mawu a coonadi ndipo ndili bwinobwino. 26 Pakuti mfumu imene ndikulankhula nayo momasuka ikudziwa bwino zinthu zimenezi. Ine ndine wotsimikiza kuti palibe ngakhale cimodzi mwa zinthu zimenezi cimene sakucidziwa, cifukwa palibe ciliconse cimene cinacitika mobisa. 27 Kodi inu, Mfumu Agiripa, mumakhulupilila zimene aneneli analemba? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupilila.” 28 Koma Agiripa anauza Paulo kuti: “M’kanthawi kocepa ukhoza kundikopa kuti ndikhale Mkhristu.” 29 Paulo atamva izi anati: “Pemphelo langa kwa Mulungu ndi lakuti, kaya m’kanthawi kocepa kapena kwa nthawi yaitali, onse amene akundimvetsela lelo osati inu nokha, akhale ngati ine kupatulapo maunyolo okhawa.”

30 Ndiyeno mfumuyo, bwanamkubwa, komanso Berenike ndi anthu omwe anakhala nawo pamodzi anaimilila. 31 Koma pamene anali kucoka, iwo anayamba kukambilana kuti: “Munthu uyu sanacite ciliconse coyenela kumuphela kapena com’mangila.” 32 Ndiyeno Agiripa anauza Fesito kuti: “Munthu uyu akanapanda kucita apilo kwa Kaisara, akanamasulidwa.”

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani