LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • 1 Akorinto 11
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la 1 Akorinto

      • “Tengelani citsanzo canga” (1)

      • Umutu komanso kubvala cophimba kumutu (2-16)

      • Kucita mwambo wa Mgonelo wa Ambuye (17-34)

1 Akorinto 11:3

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    2/2021, masa. 2-3

    Nsanja ya Mlonda,

    11/15/2015, tsa. 22

1 Akorinto 11:5

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 209-210

1 Akorinto 11:10

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    “m’Cikondi ca Mulungu,” masa. 211-212

1 Akorinto 11:14

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “sicikukuphunzitsani.”

1 Akorinto 11:20

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Cakudya Camadzulo ca Ambuye.”

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 28

1 Akorinto 11:24

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    12/1/2013, masa. 25-26

1 Akorinto 11:25

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    12/1/2013, tsa. 26

1 Akorinto 11:26

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/2018, tsa. 16

1 Akorinto 11:27

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/2020, masa. 27-28

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    1/15/2016, masa. 21-22

    Nsanja ya Mlonda,

    1/15/2015, masa. 15-16

1 Akorinto 11:28

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    1/15/2015, masa. 15-16

1 Akorinto 11:30

Mawu amunsi

  • *

    Ayenela kuti akutanthauza kufa kuuzimu.

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda,

    1/15/2015, masa. 15-16

1 Akorinto 11:33

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Cakudya Camadzulo ca Ambuye.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
1 Akorinto 11:1-34

Kalata Yoyamba kwa Akorinto

11 Tengelani citsanzo canga, mmenenso ine ndikutengela citsanzo ca Khristu.

2 Ndikukuyamikilani cifukwa cakuti mumandikumbukila mu zinthu zonse, ndipo mukusunga mosamala miyambo monga mmene ndinaipelekela kwa inu. 3 Koma ndikufuna mudziwe kuti mutu wa mwamuna aliyense ndi Khristu. Mutu wa mkazi ndi mwamuna, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu. 4 Mwamuna aliyense amene akupemphela kapena kulosela atabvala cinacake kumutu amacititsa manyazi mutu wake. 5 Koma mkazi aliyense amene akupemphela kapena kulosela popanda kubvala cakumutu amacititsa manyazi mutu wake, cifukwa kutelo zikhala ngati kuti wameta mpala. 6 Pakuti ngati mkazi sabvala cophimba kumutu, azimeta tsitsi lake. Koma ngati izi n’zocititsa manyazi kwa mkazi kuti amete tsitsi lake kapena kumeta mpala, azibvala cophimba kumutu.

7 Mwamuna sayenela kubvala cophimba kumutu, cifukwa ndiye cifanizilo komanso ulemelelo wa Mulungu, koma mkazi ndi ulemelelo wa mwamuna. 8 Pakuti mwamuna sanacokele kwa mkazi, koma mkazi ndiye anacokela kwa mwamuna. 9 Kuonjezela apo, mwamuna sanalengedwele mkazi, koma mkazi ndiye analengedwela mwamuna. 10 N’cifukwa cake mkazi ayenela kukhala ndi cizindikilo kumutu kwake coonetsa kuti ali pansi pa ulamulilo wa mwamuna monga cizindikilo coonekela kwa angelo.

11 Mwa Ambuye, mkazi amadalila mwamuna, ndiponso mwamuna amadalila mkazi. 12 Mkazi amacokela kwa mwamuna, cimodzi-modzinso mwamuna amacokela kwa mkazi. Koma zinthu zonse zimacokela kwa Mulungu. 13 Weluzani nokha: Kodi m’poyenela kuti mkazi azipemphela kwa Mulungu popanda kubvala cophimba kumutu? 14 Kodi cibadwa sicikukuuzani* kuti zimakhala zocititsa manyazi mwamuna kukhala ndi tsitsi lalitali? 15 Ngati mkazi ali ndi tsitsi lalitali, umenewo umakhala ulemelelo wake. Pakuti iye anapatsidwa tsitsi m’malo mwa cophimba kumutu. 16 Ngati wina akufuna kutsutsa zimenezi pofuna cikhalidwe cina, ife komanso mpingo wa Mulungu tilibe cikhalidwe cina.

17 Koma sikuti pokupatsani malangizo amenewa ndikukuyamikilani ai, cifukwa mumasonkhana pamodzi osati pa zifukwa zabwino koma zoipa. 18 Coyamba, ndamva kuti mukasonkhana pamodzi mumpingo, pakati panu pamakhala magawano. Kumbali ina ndikhulupilila kuti zimenezi n’zoona. 19 Pakati panu payeneladi kukhala magulu ampatuko, kuti amene ndi obvomelezeka pakati panu adziwike.

20 Mukasonkhana pamalo amodzi kuti mudye Mgonelo wa Ambuye,* simucita zimenezo m’njila yoyenela. 21 Cifukwa nthawi ya cakudyaco isanafike, aliyense wa inu amakhala atadyelatu cakudya cake camadzulo. Wina amakhala ndi njala koma wina amakhala woledzela. 22 Kodi inu mulibe nyumba zimene mungadyeleko ndi kumwa? Kapena mukunyozela mpingo wa Mulungu, ndipo mukucititsa manyazi amene alibe kanthu? Ndikuuzeni ciani pamenepa? Ndikuyamikileni? Pa izi zokha ai, sindingakuyamikileni.

23 Pakuti zimene ndinalandila kwa Ambuye, n’zimenenso ndinakuphunzitsani kuti usiku umene Ambuye Yesu anapelekedwa anatenga mkate, 24 ndipo atayamika anaunyema-nyema n’kukamba kuti: “Mkate uwu ukuimila thupi langa limene likupelekedwa kaamba ka inu. Muzicita zimenezi pondikumbukila.” 25 Anacitanso cimodzi-modzi ndi kapu pambuyo pa cakudya camadzulo. Iye anati: “Kapu iyi ikuimila cipangano catsopano pamaziko a magazi anga. Muzicita zimenezi mukamamwa za m’kapuyi pondikumbukila.” 26 Pakuti nthawi zonse mukamadya mkatewu ndi kumwa za m’kapuyi, mumalengeza za imfa ya Ambuye mpaka pamene adzabwele.

27 Conco, aliyense amene akudya mkate, kapena kumwa za m’kapu ya Ambuye mosayenelela, adzakhala ndi mlandu wokhudza thupi komanso magazi a Ambuye. 28 Cotelo munthu ayenela kudzifufuza coyamba, pambuyo pake m’pomwe angadye mkate ndi kumwa za m’kapuyi. 29 Pakuti munthu amene amadya ndi kumwa popanda kuzindikila kuti zinthuzo zikuimila thupilo, amadzibweletsela cilango. 30 N’cifukwa cake ambili a inu ndinu ofooka komanso odwala, ndipo ambilinso afa.* 31 Koma ngati tingathe kuzindikila mmene tilili, sitingaweluzidwe. 32 Komabe, tikaweluzidwa ndiye kuti tikulangizidwa ndi Yehova, kuti tisaweluzidwile pamodzi ndi dzikoli. 33 Conco abale, mukasonkhana pamodzi kuti mudye Mgonelo wa Ambuye,* muziyembekezana. 34 Ngati wina ali ndi njala, azidya kunyumba, kuti mukasonkhana pamodzi musaweluzidwe. Koma nkhani zimene zatsala ndidzazisamalila ndikadzafika kumeneko.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani