Uthenga Wabwino Wolembedwa ndi Yohane
2 Pa tsiku lacitatu, ku Kana wa ku Galileya kunali phwando la ukwati, ndipo amayi ake a Yesu analinso kumeneko. 2 Yesu ndi ophunzila ake nawonso anaitanidwa ku phwando la ukwati limenelo.
3 Vinyo atatsala pang’ono kutha, amayi ake a Yesu anauza Yesuyo kuti: “Vinyo waathela.” 4 Koma Yesu anauza mayi akewo kuti: “Mayi, ife zikutikhudza bwanji?* Nthawi yanga sinafike.” 5 Amayi ake anauza amene anali kutumikila kuti: “Mucite zilizonse zimene angakuuzeni.” 6 Tsopano pamalopo panali mbiya zamiyala 6 mogwilizana ndi malamulo a Ayuda a kudziyeletsa. Mbiya iliyonse inali kukwana malita pafupifupi 44 mpaka 66. 7 Yesu anawauza kuti: “Dzazani mbiyazi ndi madzi.” Iwo anadzaza mbiyazo mpaka pakamwa. 8 Kenako iye anawauza kuti: “Tapam’moni mupeleke kwa woyang’anila phwandoli.” Ndipo iwo anapelekadi. 9 Woyang’anila phwando uja analawa madzi amene anasandutsidwa vinyo. Iye sanadziwe kumene vinyoyo anacokela (ngakhale kuti otumikila omwe anatapa madziwo anadziwa). Conco woyang’anila phwandoyo anaitana mkwati 10 n’kumuuza kuti: “Munthu aliyense amatulutsa vinyo wabwino coyamba, ndipo anthu akaledzela m’pamene amatulutsa vinyo amene si wabwino kwenikweni. Koma iwe wasunga vinyo wabwino mpaka pano.” 11 Yesu anacita zimenezi ku Kana wa ku Galileya monga ciyambi ca zozizwitsa zake.* Iye anacititsa kuti ulemelelo wake uonekele, ndipo ophunzila ake anayamba kumukhulupilila.
12 Pambuyo pa izi, Yesu, amayi ake, abale ake, pamodzi ndi ophunzila ake, anapita ku Kaperenao, koma sanakhaleko masiku ambili.
13 Tsopano Pasika wa Ayuda atayandikila, Yesu anapita ku Yerusalemu. 14 Kumeneko anapeza kuti m’kacisi muli ogulitsa ng’ombe, nkhosa, nkhunda, komanso osintha ndalama, atakhalakhala m’mipando yawo. 15 Conco Yesu anapanga mkwapulo wazingwe, ndi kuwathamangitsila panja pa kacisi onse ogulitsa nkhosa ndi ng’ombe. Kenako anakhuthula makobili a osintha ndalama n’kugudubula matebulo awo. 16 Ndiyeno anauza amene anali kugulitsa nkhundawo kuti: “Zicotseni muno izi! Mulekeletu kusandutsa nyumba ya Atate wanga kukhala nyumba yamalonda!”* 17 Ophunzila ake anakumbukila zimene Malemba amanena kuti: “Cangu canga pa nyumba yanu cidzayaka ngati moto mumtima mwanga.”
18 Koma Ayudawo anamuuza kuti: “Kodi ungationetse cizindikilo cotani coonetsa kuti uli ndi ulamulilo wocita zimenezi?” 19 Yesu anawayankha kuti: “Gwetsani kacisi uyu, ndipo ndidzamumanganso m’masiku atatu.” 20 Kenako Ayudawo anakamba kuti: “Panatenga zaka 46 kuti kacisiyu amangidwe, ndiye iwe ukuti udzamumanga m’masiku atatu cabe?” 21 Koma iye ponena za kacisi anali kutanthauza thupi lake. 22 Conco, iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzila ake anakumbukila kuti anali kukonda kunena zimenezi, ndipo anakhulupilila Malemba komanso mawu amene Yesu anakamba.
23 Ndiyeno pamene iye anali ku Yerusalemu pacikondwelelo ca Pasika, anthu ambili anamukhulupilila* ataona zozizwitsa* zimene anali kucita. 24 Koma Yesu sanawadalile kwenikweni, cifukwa anali kuwadziwa bwino onsewo, 25 ndipo iye sanafunikile wina kucita kumuuza za anthu, cifukwa anali kudziwa za mumtima mwa anthu.