Wolembedwa na Mateyo
20 “Ufumu wa kumwamba uli ngati mwinimunda wa mpesa amene analaŵilila m’mamaŵa kukafuna aganyu kuti akagwile nchito m’munda wake wa mpesa. 2 Atapangana nawo aganyuwo malipilo a dinari imodzi pa tsiku, anawatumiza ku munda wake wa mpesa. 3 Ca m’ma 9 koloko m’maŵa,* anapitanso kukafuna aganyu ena, ndipo anaona ena atangoimilila mu msika kusoŵa nchito. 4 Conco iye anawauza kuti, ‘Inunso pitani m’munda wanga wa mpesa ndipo nidzakupatsani malipilo oyenelela.’ 5 Iwo anapitadi. Ndiyeno ca m’ma 12 koloko masana* komanso ca m’ma 3 koloko masana,* mwinimunda uja anapitanso kukacita cimodzimodzi. 6 Pamapeto pake, ca m’ma 5 koloko madzulo,* anapitanso ku msika kuja, ndipo anapeza anthu enanso atangoimilila. Iye anawafunsa kuti, ‘N’cifukwa ciyani mwangoimilila pano tsiku lonse osagwila nchito?’ 7 Iwo anayankha kuti, ‘Cifukwa palibe amene watipatsa ganyu.’ Iye anawauza kuti, ‘Inunso pitani m’munda wanga wa mpesa.’
8 “Madzulo, mwinimunda uja anaitana kapitawo wa aganyu aja n’kumuuza kuti, ‘Itana aganyu aja uwapatse malipilo awo. Uyambe na othela utsilizile oyamba.’ 9 Anthu amene anayamba kugwila nchito pa ola la 11 aja atabwela, aliyense wa iwo analandila dinari imodzi. 10 Ndiye oyamba aja atabwela, anaganiza kuti alandila malipilo oculuka, koma nawonso analandila dinari imodzi-imodzi. 11 Aganyuwo atalandila malipilo awo, anayamba kudandaulila mwinimunda uja 12 kuti, ‘Othelawa angogwila nchito ola limodzi lokha, koma mwawapatsa malipilo ofanana na ife amene takhaula nayo nchito tsiku lonse pa dzuŵa la phwe!’ 13 Koma anauza mmodzi wa iwo kuti, ‘Bwanawe, sin’nakulakwile ciliconse. Tinagwilizana kuti malipilo ako ni dinari imodzi si conco? 14 Tenga malipilo ako uzipita. Nifuna kupatsa othelawa malipilo olingana na ako. 15 Kodi nilibe ufulu wocita zimene nifuna na zinthu zanga? Kapena diso lako lacita kaduka* cifukwa ndine wabwino?’* 16 Conco, othela adzakhala oyamba, ndipo oyamba adzakhala othela.”
17 Ali m’njila kupita ku Yerusalemu, Yesu anatengela ophunzila ake 12 aja pambali n’kuwauza kuti: 18 “Lomba tikupita ku Yerusalemu. Kumeneko Mwana wa munthu akapelekedwa kwa ansembe aakulu na alembi. Iwo adzamuweluza kuti aphedwe, 19 komanso adzamupeleka kwa anthu a mitundu ina kuti akamucite zacipongwe, akamukwapule na kumuphela pa mtengo. Ndipo pa tsiku lacitatu adzaukitsidwa.”
20 Kenako, mkazi wa Zebedayo anafika kwa iye na ana ake aamuna, ndipo anamuŵelamila pofuna kumupempha cinacake. 21 Yesu anamufunsa kuti: “Mufuna ciyani mayi?” Iye anayankha kuti: “Lonjezani kuti mu Ufumu wanu, ana anga aŵiliwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja, wina ku dzanja lanu lamanzele.” 22 Yesu anayankha kuti: “Simudziŵa cimene mukupempha. Kodi mungamwe za m’kapu zimene ine natsala pang’ono kumwa?” Iwo anati: “Inde tingamwe.” 23 Iye anawauza kuti: “Za m’kapu yanga mudzamwadi, koma kusankha munthu wokakhala ku dzanja langa lamanja kapena lamanzele, si udindo wanga. Atate wanga ndiwo adzapeleka malo amenewo kwa anthu amene anawakonzela malowo.”
24 Ophunzila 10 enawo atamva zimenezi, anakwiya kwambili na amuna aŵili apacibalewo. 25 Koma Yesu anawaitana n’kuwauza kuti: “Inu mukudziŵa kuti olamulila a anthu a mitundu ina amapondeleza anthu awo, ndipo akulu-akulu amaonetsa mphamvu zawo pa iwo. 26 Siziyenela kukhala conco pakati panu. Koma aliyense wofuna kukhala wamkulu pakati panu, akhale mtumiki wanu. 27 Ndipo aliyense wofuna kukhala woyamba pakati panu, akhale kapolo wanu. 28 Mofanana na zimenezi, Mwana wa munthu sanabwele kudzatumikilidwa koma kudzatumikila, komanso kudzapeleka moyo wake dipo kuti awombole anthu ambili.”
29 Pamene iwo anali kutuluka mu mzinda wa Yeriko, khamu lalikulu la anthu linamutsatila. 30 Ndiyeno amuna aŵili akhungu amene anali atakhala pansi m’mbali mwa msewu anamva kuti Yesu akudutsa, ndipo anafuula kuti: “Ambuye, Mwana wa Davide, ticitileni cifundo!” 31 Pamenepo khamu la anthulo linawadzudzula kuti akhale cete. Koma m’pamene iwo anafuula kwambili kuti: “Ambuye, Mwana wa Davide, ticitileni cifundo!” 32 Conco Yesu anaima n’kuwaitana, ndipo anati: “Mufuna nikucitileni ciyani?” 33 Iwo anati: “Ambuye, titseguleni maso.” 34 Atagwidwa na cifundo, Yesu anagwila m’maso mwawo. Nthawi yomweyo akhunguwo anayambanso kuona ndipo anam’tsatila.