LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 19
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Paulo ku Efeso; ena abatizika kaciwili (1-7)

      • Nchito yophunzitsa ya Paulo (8-10)

      • Apeza cipambano ngakhale kuti ena anali kukhulupilila zamizimu (11-20)

      • Cipolowe ku Efeso (21-41)

Macitidwe 19:9

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “anaumitsa mitima yawo, ndipo sanakhulupilile.”

Macitidwe 19:12

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “maepuloni.”

Macitidwe 19:19

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 24

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    4/2019, masa. 22-23

Macitidwe 19:38

Mawu amunsi

  • *

    Bwanamkubwa wa cigawo ca Roma.

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
  • 38
  • 39
  • 40
  • 41
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 19:1-41

Macitidwe a Atumwi

19 Apolo ali ku Korinto, Paulo anadzela ku madela a kumtunda mpaka anafika ku Efeso. Kumeneko iye anapeza ophunzila ena, 2 ndipo anawafunsa kuti: “Kodi munalandila mzimu woyela mutakhala okhulupilila?” Iwo anamuyankha kuti: “Sitinamvepo kuti kuli mzimu woyela.” 3 Iye anawafunsanso kuti: “Ndiye kodi munabatizidwa ubatizo wotani?” Iwo anayankha kuti: “Ubatizo wa Yohane.” 4 Ndiyeno Paulo anati: “Yohane anali kubatiza anthu ndipo ubatizowo unali cizindikilo cakuti munthu walapa. Anali kuuza anthu kuti akhulupilile amene anali kubwela m’mbuyo mwake, kutanthauza Yesu.” 5 Atamva izi, anthuwo anabatizika m’dzina la Ambuye Yesu. 6 Ndiyeno Paulo ataika manja ake pamutu pawo, iwo analandila mzimu woyela, ndipo anayamba kukamba zinenelo zina komanso kulosela. 7 Onse pamodzi anali amuna pafupifupi 12.

8 Kwa miyezi itatu, Paulo anali kulowa m’sunagoge ndipo anali kulankhula molimba mtima. Kumeneko anali kukamba nkhani ndi kuwafotokozela mfundo zogwila mtima za Ufumu wa Mulungu. 9 Koma ena anakana mwamwano kukhulupilila,* ndipo anali kukamba zinthu zonyoza Njilayo pamaso pa khamu la anthu. Conco iye anacoka n’kucotsanso ophunzila pakati pawo. Ndipo tsiku ndi tsiku anali kukamba nkhani mu holo ya pa sukulu ya Turano. 10 Izi zinacitika kwa zaka ziwili, moti anthu onse okhala m’cigawo ca Asia, anamva mawu a Ambuye, onse Ayuda ndi Agiriki.

11 Ndipo kupitila mwa Paulo, Mulungu anapitiliza kucita zinthu zamphamvu komanso zodabwitsa, 12 cakuti anthu anali kutenga ngakhale tunsalu ndi zovala* zimene zinakhudza thupi la Paulo n’kupita nazo kwa odwala, ndipo matenda awo anali kuthelatu. Mizimu yoipa nayonso inali kutuluka. 13 Koma Ayuda ena amene anali kuyendayenda n’kumatulutsa ziwanda, nawonso anayesa kuchula dzina la Ambuye Yesu pofuna kucilitsa anthu amene anali ndi mizimu yoipa. Iwo anali kunena kuti: “Ndikukulamula m’dzina la Yesu amene Paulo amalalikila za iye.” 14 Tsopano panali ana aamuna 7 a Sikeva, wansembe wamkulu waciyuda, amene anali kucita zimenezi. 15 Koma mzimu woipa unawauza kuti: “Yesu ndimamudziwa, komanso Paulo ndimamudziwa bwino. Nanga inu ndinu ndani?” 16 Ndiyeno munthu uja amene anali ndi mzimu woipa anawalumphila. Analimbana nawo mmodzi mmodzi ndipo anawagonjetsa onsewo, moti anathawa m’nyumbamo ali malisece komanso atavulazidwa. 17 Izi zinadziwika kwa onse, kwa Ayuda ndi Agiriki amene anali kukhala ku Efeso. Onsewo anagwidwa ndi mantha, ndipo dzina la Ambuye Yesu linapitiliza kulemekezedwa. 18 Anthu ambili mwa amene anakhala okhulupilila anali kubwela kudzaulula macimo awo, ndiponso kudzafotokoza poyela zoipa zimene anali kucita. 19 Anthu ambili amene anali kucita zamatsenga anasonkhanitsa mabuku awo n’kuwatentha anthu onse akuona. Ndipo atawelengetsela mtengo wake, anapeza kuti anali okwana ndalama zasiliva 50,000. 20 Conco mawu a Yehova anapitiliza kufalikila ndipo sanagonjetsedwe.

21 Izi zitacitika, Paulo anatsimikiza mu mtima mwake kuti atadzela ku Makedoniya ndi ku Akaya, apite ku Yerusalemu. Iye anakamba kuti: “Ndikakafika kumeneko, ndidzapitanso ku Roma.” 22 Conco ku Makedoniya anatumizako awili mwa amene anali kumutumikila, iwo anali Timoteyo ndi Erasito. Koma iye anakhalabe m’cigawo ca Asia kwa kanthawi ndithu.

23 Panthawiyo, panali patabuka msokonezo waukulu wokhudza Njila ya Ambuye. 24 Panali munthu wina dzina lake Demetiriyo, wopanga zinthu zasiliva. Amisili anali kupeza phindu kwambili cifukwa ca nchito yake yopanga tuakacisi twasiliva twa Atemi. 25 Demetiriyo anasonkhanitsa amisiliwo, limodzi ndi ena amene anali kugwila nchito ngati zimenezi n’kuwauza kuti: “Anthu inu, mukudziwa kuti timapeza cuma kucokela m’bizinesi imeneyi. 26 Tsopano mukuona ndi kumva mmene Paulo ameneyu wakopela anthu ambili kuti ayambe kukhulupilila zinthu zina. Iye wacita zimenezi osati mu Efeso mokha, koma pafupifupi m’cigawo conse ca Asia. Iye akukamba kuti milungu yopangidwa ndi manja si milungu yeniyeni. 27 Komanso cimene cikuopsa kwambili si kunyozeka kwa bizinesi yathuyi ayi, koma kacisi wa mulungu wamkazi Atemi adzaonedwa wacabecabe. Atemi ameneyu amene amalambilidwa m’cigawo conse ca Asia, komanso kulikonse kumene kuli anthu pa dziko lapansi adzaleka kupatsidwa ulemelelo wake.” 28 Anthuwo atamva zimenezi anakwiya kwambili, ndipo anayamba kufuula kuti: “Wamkulu ndi Atemi mulungu wa Aefeso!”

29 Zitatelo, mu mzindawo munadzala cisokonezo, ndipo anthu onse anathamangila m’bwalo la masewela, n’kukokela Gayo ndi Arisitako m’bwalomo. Gayo ndi Arisitako amene anali kuyenda ndi Paulo kwawo kunali ku Makedoniya. 30 Paulo anali kufuna kulowa mkati m’gulu la anthulo, koma ophunzila sanamulole. 31 Ngakhale ena mwa oyang’anila zikondwelelo ndi masewela, amene anali anzake a Paulo, anatumiza uthenga kumucondelela kuti asaike moyo wake pangozi mwa kulowa m’bwalo la masewelalo. 32 Kukamba zoona, khamu lonse linali litasokonezeka, ena anali kufuula zinthu zina pamene ena zinthu zina. Ndipo ambili a iwo sanadziwe kuti n’cifukwa ciyani anasonkhana kumeneko. 33 Conco anatulutsa Alekizanda m’khamulo ndipo Ayuda anali kumukankhila kutsogolo. Ndiyeno Alekizanda anakweza dzanja lake kuti alankhule podziteteza kwa anthuwo. 34 Koma atazindikila kuti ndi Myuda, anayamba kufuula capamodzi kwa maola pafupifupi awili kuti: “Wamkulu ndi Atemi mulungu wa Aefeso!”

35 Woyang’anila mzindawo atauza khamulo kuti likhale cete anati: “Anthu inu a mu Efeso, kodi pali amene sadziwa kuti mzinda wa Aefeso ndi umene umayang’anila kacisi wamkulu wa Atemi ndi cifanizilo cimene cinagwa kucokela kumwamba? 36 Popeza palibe amene angatsutse zimenezi, muyenela kudekha, ndipo musacite zinthu mopupuluma. 37 Cifukwa anthu amene mwabweletsa kunowa si akuba akacisi kapena onyoza mulungu wathu wamkaziyo. 38 Conco ngati Demetiriyo ndi amisili awa akuimba mlandu munthu winawake, pali masiku osamalila milandu ndipo abwanamkubwa* alipo. Apite akafole kumeneko. 39 Koma ngati mukufuna zina zoposa pamenepa, cigamulo cake ciyenela kukapelekedwa pa bwalo lovomelezeka. 40 Pakuti zimene zacitikazi n’zoopsa kwambili cifukwa tingaimbidwe nazo mlandu woukila boma. Pakuti palibe cifukwa comveka cimene tingapeleke pa cipolowe cimene cacitikaci.” 41 Atanena zimenezi, anauza anthuwo kuti acoke pamalopo.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani