LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • Macitidwe 10
  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

Za m’Buku la Macitidwe

      • Masomphenya a Koneliyo (1-8)

      • Petulo aona masomphenya a nyama zoyeletsedwa (9-16)

      • Petulo apita kunyumba kwa Koneliyo (17-33)

      • Petulo alengeza uthenga wabwino kwa anthu a mitundu ina (34-43)

        • “Mulungu alibe tsankho” (34, 35)

      • Anthu a mitundu ina alandila mzimu woyela ndipo abatizidwa (44-48)

Macitidwe 10:1

Mawu amunsi

  • *

    Anali kuyang’anila asilikali 100.

  • *

    Gulu la asilikali a Ciroma amene anali kukhala 600.

Macitidwe 10:3

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “ola la 9.”

Macitidwe 10:9

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “ola la 6.”

Macitidwe 10:30

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “ola la 9.”

Macitidwe 10:34

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 5

    Galamuka!,

    na. 1 2021 tsa. 7

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2018, tsa. 9

Macitidwe 10:35

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!, phunzilo 5

    Galamuka!,

    na. 1 2021 tsa. 7

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    8/2018, tsa. 9

    sanja ya Mlonda,

    10/1/2010, tsa. 11

Macitidwe 10:38

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yophunzila),

    7/2020, tsa. 31

    Maphunzilo a m’Baibo, masa. 186-187

Macitidwe 10:40

Amlongoza a Zofalitsa

  • Buku Lofufuzila Nkhani

    Nsanja ya Mlonda (Yogawila),

    na. 6 2017 tsa. 9

Macitidwe 10:45

Mawu amunsi

  • *

    Kapena kuti, “Mulungu anaipungulilanso.”

Macitidwe 10:46

Mawu amunsi

  • *

    M’cinenelo coyambilila, “malilime.”

  • Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
  • 36
  • 37
  • 38
  • 39
  • 40
  • 41
  • 42
  • 43
  • 44
  • 45
  • 46
  • 47
  • 48
Baibo ya Cimasulilo ca Dziko Latsopano
Macitidwe 10:1-48

Macitidwe a Atumwi

10 Tsopano ku Kaisareya kunali munthu wina dzina lake Koneliyo, kapitawo wa asilikali* a m’gulu la asilikali a ku Italy.* 2 Iye anali kukonda zopemphela, ndipo anali kuopa Mulungu pamodzi ndi onse a m’banja lake. Anali kukondanso kupatsa anthu mphatso zambili zacifundo ndipo anali kupemphela mocondelela nthawi zonse kwa Mulungu. 3 Tsiku lina ca m’ma 3 koloko masana,* anaona mngelo wa Mulungu m’masomphenya akubwela kwa iye n’kunena kuti: “Koneliyo!” 4 Koneliyo anayang’anitsitsa mngeloyo mwamantha ndipo ananena kuti: “Ndili pano Ambuye.” Mngeloyo anati: “Mulungu wamva mapemphelo ako komanso waona mphatso zako zacifundo ndipo akuzikumbukila. 5 Conco tumiza anthu ku Yopa kuti akaitane munthu wina dzina lake Simoni, wodziwikanso kuti Petulo. 6 Munthu ameneyu ndi mlendo kunyumba kwa Simoni wofufuta zikumba, amene ali ndi nyumba m’mbali mwa nyanja.” 7 Mngelo amene anali kulankhula naye atangocoka, Koneliyo anaitana atumiki ake awili, komanso msilikali wake wina wokonda kupemphela pakati pa atumiki ake. 8 Iye anawafotokozela zinthu zonse ndi kuwatumiza ku Yopa.

9 Tsiku lotsatila, ulendo wawo uli mkati, komanso atatsala pafupi kufika mumzindawo, Petulo anakwela pamtenje ca m’ma 12 koloko masana* kukapemphela. 10 Koma iye anamva njala kwambili, ndipo anali kufuna kudya. Pamene cakudya cinali kukonzedwa, iye anayamba kuona masomphenya. 11 M’masomphenyawo anaona kumwamba kutatseguka, ndiponso cinthu cinacake cooneka ngati cinsalu cacikulu cikutsika. Cinthuco anacigwila m’makona onse anayi pocitsitsila padziko lapansi. 12 Pa cinthuco panali nyama za mitundu yonse za miyendo inayi, komanso nyama zokwawa za padziko lapansi ndi mbalame za mumlengalenga. 13 Ndiyeno anamva mawu omuuza kuti: “Petulo, nyamuka uphe ndi kudya zinthu zimenezi.” 14 Koma Petulo anati: “Ayi Ambuye, ine sindinadyepo codetsedwa komanso conyansa ciliconse.” 15 Koma anamvanso mawu olankhula ndi iye kaciwili kuti: “Ulekeletu kuchula zinthu zimene Mulungu waziyeletsa kuti ndi zodetsedwa.” 16 Anamvanso mawu kacitatu, ndipo nthawi yomweyo cinthu cooneka ngati cinsalu cija cinatengedwa kupita kumwamba.

17 Petulo ali wodabwa kwambili posamvetsa tanthauzo la masomphenya amene anaonawo, anthu aja amene Koneliyo anatuma anafunsa kumene kuli nyumba ya Simoni ndipo anaimilila pageti. 18 Iwo anafunsa mofuula ngati Simoni wochedwanso Petulo anali mlendo kumeneko. 19 Petulo akuganizila za masomphenyawo, mzimu wa Mulungu unamuuza kuti: “Taona! Amuna atatu akukufuna. 20 Conco nyamuka, tsika upite nawo. Usakayikile ngakhale pang’ono, cifukwa ndine ndawatuma.” 21 Petulo anatsika kukakumana ndi amunawo ndipo anati: “Munthu amene mukumufunayo ndine. Ndingakuthandizeni bwanji?” 22 Iwo anati: “Tatumidwa ndi Koneliyo, mtsogoleli wa asilikali. Iye ndi munthu wolungama komanso woopa Mulungu amene ali ndi mbili yabwino pakati pa mtundu wonse wa Ayuda. Mngelo woyela anamupatsa malangizo ocokela kwa Mulungu kuti atume anthu kudzakutengani kuti mupite kunyumba kwake, akamve zimene inu mukanene.” 23 Conco anawalowetsa m’nyumba ndipo anawasamalila monga alendo ake.

Tsiku lotsatila ananyamuka n’kupita nawo, ndipo abale ena a ku Yopa anapita naye limodzi. 24 Tsiku lotsatila anafika ku Kaisareya. Koneliyo anali kuwayembekezela, ndipo anali atasonkhanitsa acibale ake ndi mabwenzi ake apamtima. 25 Pamene Petulo anali kulowa, Koneliyo anakumana naye ndipo anagwada pansi kumapazi ake n’kumuwelamila. 26 Koma Petulo anamuimilitsa n’kumuuza kuti: “Nyamuka, inenso ndine munthu ngati iwe.” 27 Kenako, analowa uku akukambilana naye, ndipo anapeza anthu ambili atasonkhana mmenemo. 28 Ndiyeno Petulo anawauza kuti: “Inu mukudziwa bwino kuti sikololeka kuti Myuda aziceza ndi munthu wa mtundu wina, kapena kumuyandikila. Komabe Mulungu wandionetsa kuti sindifunika kuchula munthu aliyense kuti wodetsedwa kapena wonyansa. 29 Ndiye cifukwa cake ndabwela mosanyinyilika nditaitanidwa. Conco ndiuzeni, n’cifukwa ciyani mwandiitana?”

30 Ndiyeno Koneliyo anati: “Masiku anayi apitawa, ndinali kupemphela m’nyumba mwanga ca m’ma 3 koloko masana,* basi ndinangoona munthu wovala zovala zowala ataimilila kutsogolo kwanga, 31 n’kundiuza kuti: ‘Koneliyo, Mulungu wamva pemphelo lako, ndipo waona mphatso zako zacifundo n’kuzikumbukila. 32 Conco tumiza anthu ku Yopa kuti akaitane Simoni wodziwikanso kuti Petulo. Munthuyo ndi mlendo m’nyumba ya Simoni wofufuta zikumba amene amakhala m’mbali mwa nyanja.’ 33 Ndiyeno nthawi yomweyo ndinatuma anthu kuti adzakuitaneni, ndipo mwatikomela mtima n’kubwela. Conco tonse tili pano pamaso pa Mulungu kuti timve zonse zimene Yehova wakulamulani kuti mutiuze.”

34 Petulo atamva izi, anayamba kukamba kuti: “Tsopano ndadziwa ndithu kuti Mulungu alibe tsankho. 35 Koma munthu wocokela mu mtundu uliwonse, amene amamuopa ndi kucita cilungamo, ndi wovomelezeka kwa iye. 36 Mulungu anatumiza mawu kwa Aisiraeli, ndipo analengeza kwa iwo uthenga wabwino wa mtendele kupitila mwa Yesu Khristu. Ameneyu ndi Ambuye wa onse. 37 Inu mukuidziwa nkhani imene inafala kwambili kuyambila ku Galileya mpaka ku Yudeya konse, pambuyo pa ubatizo umene Yohane analalikila. 38 Nkhaniyo inali yokamba za Yesu wa ku Nazareti, amene Mulungu anamudzoza ndi mzimu woyela ndi kumupatsa mphamvu. Iye anayenda m’dziko lonse, ndipo anali kucita zabwino komanso kucilitsa onse amene anali kusautsidwa ndi Mdyelekezi cifukwa Mulungu anali naye. 39 Ndipo ife ndife mboni za zinthu zonse zimene iye anacita m’dziko la Ayuda komanso ku Yerusalemu. Koma iwo anamupha mwa kumupacika pamtengo. 40 Mulungu anamuukitsa iyeyo pa tsiku lacitatu, ndipo analola kuti anthu amuone. 41 Sanaonekele kwa anthu onse, koma kwa mboni zimene Mulungu anasankhilatu, ifeyo amene tinadya ndi kumwa naye limodzi ataukitsidwa. 42 Komanso anatilamula kuti tilalikile kwa anthu, ndi kupeleka umboni wokwanila wakuti iyeyu ndi amene Mulungu anamuika kukhala woweluza wa anthu amoyo ndi akufa. 43 Aneneli onse amacitila umboni za iye, kuti aliyense wokhulupilila iye, Mulungu adzamukhululukila macimo kupitila m’dzina lake.”

44 Petulo ali mkati mokamba zimenezi, anthu onse amene anali kumvetsela mawuwo analandila mzimu woyela. 45 Ndipo okhulupilila odulidwa, amene anabwela ndi Petulo anadabwa kwambili cifukwa mphatso yaulele ya mzimu woyela inapelekedwanso* kwa anthu a mitundu ina. 46 Cifukwa anawamva akulankhula zinenelo* zina ndiponso kutamanda Mulungu. Ndiyeno Petulo ananena kuti: 47 “Kodi pali aliyense amene angaletse kuti anthu awa amene alandila mzimu woyela ngati ife asabatizidwe m’madzi?” 48 Atatelo, iye anawalamula kuti abatizidwe m’dzina la Yesu Khristu. Kenako iwo anamupempha kuti akhalebe nawo kwa masiku angapo.

Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
Tulukani
Loŵani
  • Cinyanja
  • Gawilani
  • Makonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenela Kutsatila
  • Mfundo Yosunga Cisinsi
  • Kusunga Cinsinsi
  • JW.ORG
  • Loŵani
Gawilani