LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • my nkhani 32
  • Milili 10

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Milili 10
  • Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Milili Itatu Yoyambilila
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mlili wa Namba 10
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Milili 6 Yokonkhapo
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mose Ndi Aroni Aonana Ndi Farao
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Onaninso Zina
Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
my nkhani 32

Nkhani 32

Milili 10

YANG’ANA pazithunzi-thunzi izi. Cithunzi-thunzi ciliconse cionetsa mlili umene Yehova anabweletsa mu dziko la Iguputo. Pacithunzi-thunzi coyamba pali Aroni amenya pamtsinje wa Nailo ndi ndodo yake. Pamene anacita zimenezi, madzi a mu mtsinjewo anasanduka magazi. Nsomba zinafa, ndipo mtsinjewo unayamba kununkha moipa.

Cotsatilapo, Yehova anacititsa acule kutuluka mu mtsinje wa Nailo. Acule amenewa anali paliponse, mu mauvuni, mu ziwiya zokanyilamo fulaulo, ndi pa mabedi a anthu. Pamene acule anafa, Aiguputo anawaunjika miyulu miyulu, ndipo dziko lonse linanunkha moipa cifukwa ca acule.

Ndiyeno Aroni anamenya pansi ndi ndodo yake, ndipo fumbi linasanduka nchenche kapena kuti inzi zoluma. Nchenchezo zinali zing’ono-zing’ono koma zoluma. Mlili wanchenche unali wacitatu kucitika mu dziko la Iguputo.

Milili yonse yotsatila inali kugwela Aiguputo okha, osati Aisiraeli. Mlili wacinai unali tudoyo twakumwa magazi tumene tunaloŵa mu nyumba zonse za Aiguputo. Mlili wacisanu unakhudza zinyama. Ng’ombe, nkhosa ndi mbuzi zambili za Aiguputo zinafa.

Ndiyeno, Mose ndi Aroni anatenga phulusa ndi kuliponya m’mwamba. Phulusa limenelo linacititsa anthu ndi zinyama kukhala ndi zilonda zoipa kwambili. Ndipo zilonda zimenezi zinali mlili wa namba 6.

Pambuyo pa zimenezi, Mose ananyamula dzanja lake m’mwamba, ndipo Yehova anatumiza mphezi ndi cimvula ca matalala. Cinali cimvula ca matalala amene sanagwepo mu Iguputo.

Mlili wa namba 8 unali wa dzombe lambili. Kuyambila kale mpaka nthawi imeneyo, sikunagwepo dzombe lambili conco. Linadya zinthu zonse zimene cimvula cija cinasiyako.

Mlili wa namba 9 unali cimdima. Kwa masiku atatu, mu dziko lonse munali cimdima candiweyani, koma kumene Aisiraeli anali kukhala kunali kowala.

Potsilizila pake, Mulungu anauza anthu ake kuti awaze magazi a mwana wa mbuzi, kapena mwana wa nkhosa, pafelemu ya pamwamba pa zitseko zao. Ndiyeno mngelo wa Mulungu anapita mu dziko lonse la Iguputo. Anali kuti akaona magazi pakhomo, sanali kupha munthu aliyense mu nyumbamo. Koma panyumba zonse zimene zinalibe magazi pazitseko, mngelo wa Mulungu anali kupha mwana woyamba wa anthu ndi wa nyama. Umenewu ndio unali mlili wa namba 10

Pambuyo pa mlili wotsilizila umenewu, Farao anauza Aisiraeli kuti apite. Anthu a Mulungu onse anali okonzeka kupita, ndipo usiku umenewo ananyamuka kucoka mu Iguputo.

Ekisodo caputa 7 mpaka 12.

Mafunso Ophunzilila

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani