LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • ol tsa. 2
  • Mau Oyamba

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mau Oyamba
  • Njila ya Kumoyo Wamuyaya—Kodi Mwaipeza?
Njila ya Kumoyo Wamuyaya—Kodi Mwaipeza?
ol tsa. 2

Mau Oyamba

MULUNGU WAMPHAMVUYONSE ni Mfumu ya cilengedwe conse. Moyo wathu, walelo ndi wa mtsogolo, umadalila iye. Ali ndi mphamvu yopeleka mphoto ndi yopeleka cilango. Ali ndi mphamvu yopatsa moyo ndi yolanda moyo. Ngati iye atiyanja, zinthu zidzatiyendela bwino; akaleka kutiyanja, zinthu sizidzatiyendela bwino. Conco kulambila kwathu kuyenela kukhala kovomelezeka kwa iye.

Banja laima pa mphambano ya njila

Anthu amalambila m’njila zosiyana-siyana. Cipembedzo cili ngati njila. Ndiyeno kodi njila zonse za cipembedzo ni zovomelezeka kwa Mulungu? Iyai, si zonse. Yesu, mneneli wa Mulungu, anaonetsa kuti pali njila ziŵili cabe. Iye anati: “Mseu waukulu ndi wotakasuka ukupita kucionongeko, ndipo anthu ambili akuyenda mmenemo. Koma cipata coloŵela kumoyo n’copapatiza komanso mseu wake ndi wopanikiza, ndipo amene akuupeza ndi oŵelengeka.”—Mateyu 7:13, 14.

Pali zipembedzo mitundu iŵili cabe: cina ca kumoyo ndi cina ca kucionongeko. Colinga ca kabuku aka ni kukuthandizani kupeza njila ya kumoyo wamuyaya.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani