Zamkati
N’CIFUKWA CIANI MUYENELA KUBWELELA KWA YEHOVA?
Anthu a Yehova ochulidwa m’Baibulo, anakumanapo ndi zopinga zofanana ndi zathu, ndipo Yehova anawathandiza. Masiku ano, iye akulonjezanso kuti adzatithandiza. Mofanana ndi Mbusa wachelu ndiponso wacikondi, Yehova amafunafuna nkhosa zake zosocela ndipo amaziitana kuti zibwelele kwa iye.
Mbali 1 “Nkhosa Zosocela Ndidzazifunafuna”
MBALI 2-4 N’CIANI CIMALEPHELETSA ENA KUBWELELA KWA YEHOVA?
Alambili ena okhulupilika a Mulungu panthawi ina anakhalapo ndi nkhawa, anakhumudwapo, anaziimba mlandu, ndipo zimenezi zinakhudza umoyo wao wakuuzimu. Onani mmene Yehova anawathandizila kuti akhalenso olimba, ayambenso kugwilizana ndi anthu ake, ndi kuti akhalenso acimwemwe.
Mbali 2 Nkhawa “Timapanikizidwa Mwamtundu Uliwonse”
Mbali 3 Kukhumudwa Tikakhala Ndi “Cifukwa Codandaulila”
Mbali 4 Kudziimba Mlandu “Ndiyeletseni ku Chimo Langa”
MBALI 5 ZOCITA KUTI MUBWELELE KWA YEHOVA
Onani umboni umene uonetsa kuti Yehova afuna kuti mubwelele kwa iye. Dziŵani zimene zinathandiza Akristu ambili kubwelela kwa Yehova, mmene mpingo unawalandilila, ndi mmene akulu anawathandizila kuti akhalenso acangu mwakuuzimu.
Mbali 5 Bwelelani kwa “Mbusa Wanu ndi Woyang’anila Miyoyo Yanu”