LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w25 September tsa. 32
  • Yesu “Anaphunzira Kumvera”

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yesu “Anaphunzira Kumvera”
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2025
w25 September tsa. 32

MAU A M’BAIBO

Yesu “Anaphunzira Kumvera”

Yesu nthawi zonse wakhala akumvera Yehova. (Yoh. 8:29) Ndiye n’cifukwa ciani Baibo imakamba kuti: “[Iye] anaphunzira kumvera cifukwa ca mabvuto amene anakumana nao”?​—Aheb. 5:8.

Yesu ali padziko lapansi, anakhala umoyo wosiyana ndi umene anali nao kumwamba. Analeredwa ndi makolo opanda ungwiro amene anali odzipereka kwa Mulungu. (Luka 2:51) Iye anapirira pamene anali kuzunzidwa ndi atsogoleri acinyengo a cipembedzo ndi akulu-akulu a boma opanda cilungamo. (Mat. 26:59; Maliko 15:15) Kuonjezera apo, iye “anadzicepetsa ndipo anakhala womvera mpaka imfa,” inde, imfa yowawa.​—Afil. 2:8.

Zimene Yesu anakumana nazozi zinam’phunzitsa kukhala womvera m’njira imene sanaphunzirepo ali kumwamba. Izi zinam’cititsa kuti akhale Mfumu komanso Mkulu wa Ansembe wabwino koposa, wokhoza kumvetsa mabvuto athu. (Aheb. 4:15; 5:9) Yesu anakhala wamtengo wapatali kwambiri kwa Yehova ataphunzira kumvera cifukwa ca mabvuto amene anakumana nao. Nafenso tingakhale a mtengo wapatali kwambiri kwa Yehova komanso ofunika kwa iye tikakhalabe omvera tikakumana ndi mabvuto.​—Yak. 1:4.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani