LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w15 11/15 tsa. 15
  • Mafunso Ocokela Kwa Aŵelengi

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mafunso Ocokela Kwa Aŵelengi
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Zofanana
  • Mpanda Wa Yeriko
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Tizidalila Mtsogoleli Wathu —Khristu
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2018
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 11/15 tsa. 15
Ansembe akuliza malipenga, Yoswa akufuula mfuu yankhondo, ndipo mpanda wa Yeriko wayamba kugwa

Mafunso Ocokela Kwa Aŵelengi

N’ciani cimene akatswili ofufuza zinthu zakale apeza cimene cionetsa kuti mzinda wa Yeriko unaonongedwa m’nthawi yocepa?

Lemba la Yoswa 6:10-15, 20 limakamba kuti asilikali a Isiraeli anazungulila mzinda wa Yeriko kamodzi pa tsiku kwa masiku 6. Pa tsiku la 7, asilikaliwo anazungulila mzindawo nthawi zokwana 7. Ndiyeno Mulungu anacititsa kuti mpanda wolimba wa Yeriko ugwe, ndipo Aisiraeli analanda mzindawo. Kodi akatswili ofufuza zinthu zakale apeza umboni uliwonse wosonyeza kuti mzindawo unagonjetsedwa m’nthawi yocepa, monga mmene Baibulo limanenela?

M’nthawi zakale, asilikali anali kuzungulila mpanda wa mzinda kuti aulande. Ngati asilikali azungulila mzindawo kwa nthawi yaitali, anthu mumzindawo anali kukakamizika kudya zakudya zimene anasunga. Ndiyeno asilikali akalanda mzinda, anali kutenga ciliconse cimene afuna, kuphatikizapo cakudya ciliconse cimene catsala. Ndiye cifukwa cake akatswili ofufuza zinthu zakale anapeza cakudya cocepa m’mabwinja a mizinda ya ku Palesitina imene inagongetsedwa mwa njila imeneyi, ndipo m’mizinda ina sanapezemo cakudya ciliconse. Koma zimene anapeza m’mabwinja a Yeriko n’zosiyana ndi zimenezi. Buku lina lofotokoza zinthu zakale limati: “M’mabwinja a Yeriko anapezamo zinthu zambili zoumba. Koma kuonjezela pamenepo, anapezamonso zakudya zambili.” Bukuli limanenanso kuti: “N’zodabwitsa kuti m’mabwinja a Yeriko anapezamo zakudya zambili.”—Biblical Archaeology Review.

Baibulo limakamba kuti Aisiraeli sanatenge cakudya ciliconse mumzinda wa Yeriko cifukwa Yehova anawalamula kuti sayenela kutelo. (Yoswa 6:17, 18) Limakambanso kuti Aisilaeli anaononga mzinda wa Yeriko m’nyengo yokolola, nthawi imene mumzindawo munali zakudya zambili. (Yoswa 3:15-17; 5:10) Monga mmene tanenela, mumzinda wa Yeriko munapezeka zakudya zambili. Izi zionetsa kuti mzindawo unaonongedwadi m’kanthawi kocepa monga mmene Baibulo limanenela.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani