LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w16 May tsa. 2
  • Zamkati

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Zamkati
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2016
w16 May tsa. 2

Zamkati

MLUNGU WA JUNE 27, 2016–JULY 3, 2016

3 Tizithetsa Mikangano Mwamtendele

Popeza ndife opanda ungwilo, nthawi zina timasemphana maganizo ndi abale ndi alongo athu. M’nkhaniyi, tidzaphunzila mfundo za m’Baibulo zimene zingatithandize kuthetsa mikangano ndi kukhala pa mtendele ndi anthu ena.

MLUNGU WA JULY 4-10, 2016

9 “Pitani Mukaphunzitse Anthu a Mitundu Yonse Kuti Akhale Ophunzila”

Nkhaniyi idzatithandiza kumvetsetsa cifukwa cake timakamba kuti Mboni za Yehova ndizo zokha padziko lapansi zimene zikukwanilitsa ulosi wa Yesu wa pa Mateyu 24:14. Tidzaphunzilanso zimene kukhala “asodzi a anthu” kumatanthauza.—Mateyu 4:19.

MLUNGU WA JULY 11-17, 2016

15 Kodi Mumasankha Bwanji Zocita?

Pamene mukupanga zosankha, kodi mumangosankha zimene muona kuti n’zoyenela? Kapena mumapempha ena kuti akuuzeni zocita? Nkhaniyi ifotokoza mmene tingapangile zosankha zabwino mwa kuganizila mmene Yehova Mulungu amaonela zinthu.

MLUNGU WA JULY 18-24, 2016

21 Kodi Baibulo Likusinthabe Umoyo Wanu?

N’kutheka kuti munapanga masinthidwe aakulu musanabatizidwe. Koma kodi muona kuti masiku ano zimakuvutani kusintha zinthu zing’onozing’ono kuti mutengele citsanzo ca Yehova ndi Yesu? Nkhaniyi ifotokoza cifukwa cake zingakhale zovuta kusintha ndiponso mmene Baibulo lingatithandizile.

MLUNGU WA JULY 25-31, 2016

27 Pindulani Mokwanila ndi Cakudya Cakuuzimu Cimene Yehova Amapeleka

M’nkhani ino, tikambilana maganizo amene tiyenela kupewa, ndiponso mmene tingapindulile ndi cakudya cakuuzimu cimene Yehova amatipatsa.

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani