LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 24 tsa. 62-tsa. 63 pala. 2
  • Sanasunge Lonjezo Lawo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Sanasunge Lonjezo Lawo
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Mwana Wa Ng’ombe Wagolide
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Citsamba Coyaka Moto
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Mose Amenya Cimwala Ndi Ndodo
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Yehova Apeleka Malamulo Ake
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Onaninso Zina
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 24 tsa. 62-tsa. 63 pala. 2
Aisiraeli aimba na kuvina mozungulila mwana wa ng’ombe wa golide

PHUNZILO 24

Sanasunge Lonjezo

Yehova anauza Mose kuti: ‘Kwela m’phili muno ubwele kwa ine. Nidzalemba malamulo anga pa miyala yosema na kukupatsa.’ Mose anakwela m’phili, ndipo anakhala mmenemo kwa masiku 40 usana na usiku. Mose ali m’philimo, Yehova analemba Malamulo 10 pa miyala iŵili yosema na kum’patsa.

Mose aponya pansi miyala yosema

Patapita nthawi, Aisiraeli anaganiza kuti Mose anawathaŵa. Conco, anauza Aroni kuti: ‘Tifuna munthu wina wakuti atitsogolele. Tipangile mulungu!’ Aroni anati: ‘Nipatseni golide wanu.’ Iye anasungunula golideyo na kupanga fano la mwana wa ng’ombe. Lomba anthuwo anati: ‘Mwana wa ng’ombe uyu ndiye Mulungu wathu amene anatitulutsa mu Iguputo!’ Anayamba kulambila fano limenelo na kucita cikondwelelo. Kodi izi zinali zolakwika? Inde, cifukwa anthuwo analonjeza kuti adzalambila Yehova yekha cabe. Koma apa lomba anaphwanya lonjezo lawo.

Yehova anaona zimene zinali kucitika. Cotelo anauza Mose kuti: ‘Seluka, pita kuli anthuwo. Iwo sakunimvela ndipo akulambila mulungu wonyenga.’ Mose anaseluka m’philimo atanyamula miyala iŵili yosema.

Atafika pafupi na msasa, anamvela anthu akuimba. Ndiyeno, anaona kuti anthuwo akuvina na kugwadila fano la mwana wa ng’ombe lija. Mose anakwiya kwambili. Pamenepo anaponyela pansi miyala iŵili ija ndipo inaphwanyika. Kenako anaphwanya fano limenelo. Ndiyeno anafunsa Aroni kuti: ‘Kodi anthu awa akunyengelela bwanji kuti ucite cinthu coipa kwambili ici?’ Aroni anati: ‘Musakalipe. Imwe mudziŵa bwino mmene anthu aŵa alili. Iwo anali kufuna mulungu. Conco, n’nasungunula golide wawo pa moto na kupanga mwana wa ng’ombe ameneyu.’ Aroni sanafunikile kucita zimenezo. Pamenepo Mose anabwelela m’phili, kukacondelela Yehova kuti awakhululukile anthuwo.

Yehova anakhululukila aja amene anamumvela na mtima wonse. Kodi waona kuti Aisiraeli anacita bwino kumvelela Mose mtsogoleli wawo?

“Ukalonjeza kwa Mulungu usamacedwe kukwanilitsa lonjezo lako, cifukwa palibe amene amasangalala ndi anthu opusa. Uzikwanilitsa zinthu zimene walonjeza.”—Mlaliki 5:4

Mafunso: Kodi Aisiraeli anacita ciani pamene Mose anali m’phili? Nanga Mose anacita ciani ataseluka m’phili muja?

Ekisodo 24:12-18; 32:1-30

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani