LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb phunzilo 56 tsa. 134-tsa. 135 pala. 1
  • Yosiya Anali Kukonda Cilamulo ca Mulungu

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Yosiya Anali Kukonda Cilamulo ca Mulungu
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Yosiya Anali ndi Anzake Abwino
    Phunzitsani Ana Anu
  • Mfumu Yabwino Yotsilizila Ya Isiraeli
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Acinyamata—Kodi Mudzakhala na Tsogolo Lotani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzila)—2023
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb phunzilo 56 tsa. 134-tsa. 135 pala. 1
Safani aŵelengela Mfumu Yosiya mpukutu

PHUNZILO 56

Yosiya Anali Kukonda Cilamulo ca Mulungu

Yosiya anakhala mfumu ya Yuda pamene anali na zaka 8 cabe. M’masiku amenewo, anthu anali kucita zamatsenga na kulambila mafano. Yosiya atafika zaka 16, analimbikila kuphunzila mmene angalambilile Yehova m’njila yoyenela. Atafika zaka 20, anayamba kuwononga mafano na maguwa ansembe m’dziko lawo. Ndipo pamene anafika zaka 26, analinganiza zakuti kacisi wa Yehova akonzedwe.

Hilikiya mkulu wansembe, anapeza mpukutu wa Cilamulo ca Yehova m’kacisi. Mwina mpukutuwo ni umene uja unalembewa na Mose. Kalembela wa mfumu, Safani, anabweletsa mpukutuwo kwa Yosiya na kuyamba kumuŵelengela mokweza. Pamene Yosiya anali kumvetsela, anazindikila kuti kwa zaka zambili anthu akhala akuphwanya malamulo a Yehova. Conco anauza Hilikiya kuti: ‘Yehova watikwiila kwambili. Pitani mukakambe naye. Adzatiuza zimene tiyenela kucita.’ Yehova anayankha kupitila mwa mneneli wamkazi Hulida. Iye anati: ‘Ayuda asiya kutsatila malamulo anga. Conco nidzawalanga, koma osati pamene Yosiya akulamulila monga mfumu, cifukwa iye waonetsa kudzicepetsa.’

Hilikiya apeza mpukutu wa Cilamulo ca Yehova

Mfumu Yosiya atamva uthengawu, anapita kukacisi na kusonkhanitsa Ayuda onse. Ndiyeno anaŵelengela anthu onsewo mokweza Cilamulo ca Yehova. Yosiya pamodzi ndi anthu onse analonjeza kuti adzamvela Yehova na mtima wawo wonse.

Kwa zaka zambili, Ayuda sanali kucita cikondwelelo ca Pasika. Koma Yosiya ataŵelenga m’Cilamulo, anapeza kuti cikondwelelo ca Pasika cifunika kucitika caka ciliconse. Ndiyeno anauza anthuwo kuti: ‘Tidzacitila Yehova cikondwelelo ca Pasika.’ Kenako Yosiya anakonzekela kupeleka nsembe zambili. Anakonzanso gulu lokaimba pakacisi. Anthu anacita cikondwelelo ca Pasika. Pambuyo pake anacita cikondwelelo ca mikate yopanda cofufumitsa kwa masiku 7. Kucokela m’masiku a Samueli, sipanacitikepo cikondwelelo ca Pasika monga cimeneci. Yosiya anali kukondadi Cilamulo ca Mulungu. Kodi iwe umakonda kuphunzila za Yehova?

“Mawu anu ndi nyale younikila kumapazi anga, ndi kuwala kounikila njila yanga.” —Salimo 119:105

Mafunso: Kodi Mfumu Yosiya inacita ciani itamvetsela ku Cilamulo ca Yehova? Nanga Yehova anali kumvela bwanji akaona Yosiya?

2 Mafumu 21:26; 22:1–23:30; 2 Mbiri 34:1–35:25

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani