LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • lfb masa. 94-95
  • Mawu Oyamba a Cigawo 7

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Mawu Oyamba a Cigawo 7
  • Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Nkhani Zofanana
  • Davide na Sauli
    Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
  • Cifukwa Cake Davide Afunikila Kuthaŵa
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
  • Davide Aikidwa Kukhala Mfumu
    Buku Langa La Nkhani Za M’baibo
Maphunzilo Amene Tingatengemo m’Baibo
lfb masa. 94-95
Davide ateteza nkhosa ku cimbalangondo

Mawu Oyamba a Cigawo 7

Cigawo cino cifotokoza mbili ya Mfumu Sauli na Mfumu Davide, pa zaka pafupi-fupi 80. Poyamba, Sauli anali wodzicepetsa komanso woopa Mulungu, koma m’kupita kwa nthawi anasintha na kuleka kukonkha malangizo a Yehova. Ndipo Yehova anamukana. M’kupita kwa nthawi, iye anauza Samueli kudzoza Davide kuti akhale mfumu ya Aisiraeli. Cifukwa ca nsanje, Sauli anayesa kangapo konse kuti aphe Davide, koma Davide sanabwezele. Mwana wa Sauli, Yonatani, anadziŵa kuti Davide anasankhiwa na Yehova. Conco anali wokhulupilika kwa Davide. Olo kuti Davide anacita macimo aakulu, sanakane uphungu wa Yehova. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kumvetsa kufunika kocilikiza makonzedwe a Mulungu nthawi zonse.

MAPHUNZILO AKULU-AKULU M’CIGAWOCI

  • Kumvela ndiye cinthu cacikulu cimene tingapatse Yehova

  • Tisabwezele coipa, koma tiyembekezele Yehova kuti akakonze zinthu

  • Tikacita chimo yaikulu, tisayese kuibisa

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani