LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 2/1 tsa. 32
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Uthenga Wabwino Ni Wocokeladi kwa Mulungu?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
  • Baibulo Ni Buku Yocokela Kwa Mulungu
    Zimene Baibulo Ingatiphunzitse
  • Kodi Baibo Mumaiona Bwanji?
    Kodi Baibo Mumaiona Bwanji?
  • Baibo ndi Buku Locokela kwa Mulungu
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 2/1 tsa. 32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi Baibulo ndi Maudi a Mulungu?

Baibulo ndi buku lapadela ndipo ndi mmene Mau a Mulungu ayenela kukhalila. Mabaibulo mabiliyoni ambili asindikizidwa m’zinenelo zambili-mbili. Malangizo a m’Baibulo amathandiza anthu kukhala ndi makhalidwe abwino.—Ŵelengani 1 Atesalonika 2:13; 2 Timoteyo 3:16.

Timadziwa kuti Baibulo ndi locokela kwa Mulungu cifukwa limanena molondola zinthu zimene zidzacitika mtsogolo. Palibe munthu amene angakwanitse kutelo pa iye yekha. Mwacitsanzo, ganizilani zimene zili m’buku la Yesaya. Cigawo ca mpukutu wa Yesaya cimene cinalembedwa zaka 100 Yesu asanabadwe, cinapezeka m’phanga pafupi ndi Nyanja Yakufa. Mau a m’cigawo cimeneco amati mzinda wa Babulo udzakhala malo opanda anthu. Mau amenewa anakwanilitsidwa zaka zambili pambuyo pa utumiki wa Yesu wapadziko lapansi.—Ŵelengani Yesaya 13:19, 20; 2 Petulo 1:20, 21.

Kodi Baibulo linalembedwa bwanji?

Kulemba Baibulo kunatenga zaka zoposa 1,600. Baibulo linalembedwa ndi anthu 40. Zimene io analemba zili ndi mfundo yaikulu imodzi ndipo sizitsutsana. Kodi zimenezi zinatheka bwanji? Zinatheka cifukwa cakuti olembawo anauzilidwa ndi Mulungu.—Ŵelengani 2 Samueli 23:2.

Nthawi zina Mulungu anali kulankhula ndi anthu amene analemba Baibulo kupyolela mwa angelo, m’masomphenya ndi m’maloto. Nthawi zambili Mulungu anali kuika maganizo ake mwa olembawo ndi kuwalola kusankha mau oyenelela kuti afotokoze uthenga wake.—Ŵelengani Chivumbulutso 1:1; 21:3-5.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 2 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani