LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • w14 3/1 masa. 16-32
  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kuyankha Mafunso a m’Baibulo
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Nkhani Zofanana
  • Kuyankha Mafunso A m’Baibulo
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • N’cifukwa Ciani Yesu Anavutika Ndi Kutifela?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Imfa ndi Kuukitsidwa kwa Yesu Kodi Zili ndi Tanthauzo Lotani kwa Inu?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Yesu Kristu Ndani?
    Uthenga Wabwino Wocokela kwa Mulungu
Onaninso Zina
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
w14 3/1 masa. 16-32

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi timapindula bwanji ndi imfa ya Yesu?

Mulungu atalenga anthu, anafuna kuti io akhale padziko lapansi kwamuyaya ndi kuti asamadwale kapena kufa. Koma munthu woyamba Adamu, sanamvele Mlengi ndipo anataya mwai wokhala ndi moyo wamuyaya. Popeza ndife ana a Adamu, timafa cifukwa iye anacimwa. (Aroma 5:8, 12; 6:23) Conco, Mulungu woona Yehova, anatuma Mwana wake Yesu padziko lapansi kuti adzapeleke moyo wake ndi kuombola moyo umene Adamu anataya.—Ŵelengani Yohane 3:16.

Yesu anafa kotelo kuti anthu akapeze moyo wosatha. Kodi muganiza kuti moyo wosatha padziko lapansi udzakhala wotani?

Cifukwa ca imfa ya Yesu, machimo athu amakhululukidwa ndipo timakhala ndi ciyembekezo ca moyo wamuyaya. Baibulo limatiuza mmene moyo padziko lapansi udzakhalila pamene sikudzakhala ukalamba, matenda ndi imfa.—Ŵelengani Yesaya 25:8; 33:24; Chivumbulutso 21:4, 5.

Kodi tiyenela kukumbukila bwanji imfa ya Yesu?

Usiku wakuti maŵa aphedwa, Yesu anauza otsatila ake kuti azikumbukila imfa yake mwa kucita mwambo wosavuta. Kukumbukila imfa ya Yesu caka ciliconse mwa njila imeneyi kumatipatsa mwai woyamikila cikondi cacikulu cimene Yehova ndi Yesu anationetsa.—Ŵelengani Luka 22:19, 20; 1 Yohane 4:9, 10.

Caka cino, Cikumbutso ca imfa ya Yesu cidzakhalako pa Mande, April 14 dzuŵa litaloŵa. Tikupemphani kuti mukasonkhane ndi Mboni za Yehova kumene mukhala.—Ŵelengani Aroma 1:11, 12.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 4 ndi 5 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mungatenge buku limeneli pa www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani