LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp16 na. 3 tsa. 16
  • Kodi Baibulo Limakamba Ciani?

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Kodi Baibulo Limakamba Ciani?
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • Kodi Mulungu ali ndi dzina?
  • Kodi n’kulakwa kuchula dzina la Mulungu?
  • Kodi Dzina la Mulungu N’ndani?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2019
  • Kugwilitsila Nchito Dzina la Mulungu ndi Kudziŵa Tanthauzo Lake
    Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni
  • Kodi Mulungu Woona Ndani?
    Kondwelani Na Moyo Kwamuyaya!—Maphunzilo a Baibo Okambilana Komanso Zocita
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2016
wp16 na. 3 tsa. 16
Dzina la Mulungu lolembedwa pa mpukutu wakale wa Baibulo

Dzina la Mulungu linalembedwa mu mipukutu yakale ya Baibulo

Kodi Baibulo Limakamba Ciani?

Kodi Mulungu ali ndi dzina?

ANTHU ENA AMAKAMBA KUTI alibe dzina, ena amati dzina lake ndi Mulungu kapena Ambuye, ndipo ena amati ali ndi maina ambili. Nanga inu muganiza bwanji?

ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA

“Dzina lanu ndinu Yehova, Inu nokha ndinu Wam’mwambamwamba, wolamulila dziko lonse lapansi.”—Salimo 83:18.

ZINA ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA

  • Ngakhale kuti Mulungu ali ndi maina ambili audindo, iye ali ndi dzina limodzi limene anadzipatsa yekha.—Ekisodo 3:15.

  • Sikuti Mulungu ndi wosamvetsetseka, iye amafuna kuti timudziŵe.—Machitidwe 17:27.

  • Kudziŵa dzina la Mulungu ndi cinthu coyamba cimene mungacite kuti mukhale naye paubwenzi.—Yakobo 4:8.

Kodi n’kulakwa kuchula dzina la Mulungu?

KODI MUNGAYANKHE BWANJI?

  • Inde

  • Iyai

  • Kaya

ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA

“Usagwilitse nchito dzina la Yehova Mulungu wako mosasamala.” (Ekisodo 20:7) Kumakhala kulakwa ngati tiseŵenzetsa dzina la Mulungu mopanda ulemu.—Yeremiya 29:9.

ZINA ZIMENE BAIBULO LIMAKAMBA

  • Yesu anali kudziŵa dzina la Mulungu ndipo analiseŵenzetsa.—Yohane 17:25, 26.

  • Mulungu akutipempha kuseŵenzetsa dzina lake. —Salimo 105:1.

  • Adani a Mulungu amacititsa anthu kuti asadziŵe dzina lake.—Yeremiya 23:27.

Kuti mudziŵe zambili, onani nkhani 1 m’buku ili, Zimene Baibo Imaphunzitsa M’ceni-ceni lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Bukuli likupezekanso pa webusaiti ya www.jw.org

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani