LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • wp18 na. 1 masa. 12-13
  • 3 Thandizo pa Kupilila Mavuto

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • 3 Thandizo pa Kupilila Mavuto
  • Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
  • Tumitu
  • Nkhani Zofanana
  • MATENDA OSACILITSIKA
  • IMFA YA MUNTHU AMENE TIMAM’KONDA
  • Kodi Mapemphelo Angakuthandizeni Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2021
  • Pemphelo—Kodi Lingakuthandizeni Bwanji?
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawila)—2018
wp18 na. 1 masa. 12-13
Mkazi ali kumanda ndipo alila; mkazi ali pa njinga ya olemala amvetsela uthenga wa m’Baibo

3 Thandizo pa Kupilila Mavuto

Pali mavuto amene lomba sitingawapewe kapena kuwathetsa. Mwacitsanzo, ngati munthu amene mumam’konda anamwalila kapena ngati mudwala matenda osacilitsika, palibe mocitila koma kungopeza njila zokuthandizani kupilila. Kodi Baibo ingakuthandizeni pa mavuto aakulu ngati amenewa?

MATENDA OSACILITSIKA

Rose anakamba kuti: “N’nabadwa na matenda osacilitsika, amene amacititsa kuti nthawi zonse nizimvela kuŵaŵa maningi. Thanzi yanga siili bwino olo pang’ono.” Cimodzi mwa zinthu zimene zinali kum’detsa nkhawa kwambili, n’cakuti nthawi zina anali kulephela kuika maganizo ake pa zimene anali kuŵelenga m’Baibo na pa zinthu zina zauzimu. Koma analimbikitsidwa kwambili na mau a Yesu apa Mateyu 19:26, pamene pamati: “Zinthu zonse n’zotheka kwa Mulungu.” Rose anazindikila kuti palinso njila zina zoŵelengela Baibo. Nthawi zina anali kulephela kuŵelenga cifukwa ca matendawo, conco anayamba kumvetsela mau ojambulidwa a m’Baibo ndi a m’mabuku ophunzilila Baibo.a Iye anakamba kuti: “Ngati kuti kunalibe njila zimenezi, sinidziŵa kuti nikanacita bwanji kuti nikhalebe olimba kuuzimu.”

Rose akayamba kudzimvela cisoni cifukwa colephela kucita zimene kale anali kucita, amapeza citonthozo pa lemba la 2 Akorinto 8:12, limene limati: “Mphatso yocokela pansi pa mtima ndi imene Mulungu amakondwela nayo, cifukwa Mulungu amafuna kuti munthu apeleke zimene angathe, osati zimene sangathe.” Mau amenewa amam’kumbutsa Rose kuti ngakhale ali na matenda, Mulungu amasangalala na zimene amacita cifukwa ndiye zimene angakwanitse.

IMFA YA MUNTHU AMENE TIMAM’KONDA

Delphine amene tam’chula kuciyambi anati: “Mwana wanga wa zaka 18 atamwalila, n’nali na cisoni cacikulu cakuti siinali kukhulupilila kuti nidzapitiliza kukhala na moyo. Zinthu zinasinthilatu mu umoyo wanga.” Koma anapeza citonthozo cacikulu pa mau apa Salimo 94:19. Pa lembali wamasalimo anauza Mulungu kuti: “Malingalilo osautsa atandiculukila mumtima mwanga, mau anu otonthoza anayamba kusangalatsa moyo wanga.” Delphine anati: “N’napemphela kwa Yehova kuti anithandize kupeza zocita zimene zinganitonthoze.”

Iye anayamba kukhala bize kugwila nchito yofunika yodzipeleka. Anayambanso kudziyelekezela na coko, cimene munthu amatha kuciseŵenzetsa olo n’cophwanyika. Iye anazindikila kuti ngakhale kuti anali kudzimva monga munthu wophwanyika, akanatha kuthandiza ena. Iye anati: “N’naona kuti pamene niseŵenzetsa mfundo za m’Baibo kutonthoza anthu amene nimaphunzila nawo Baibo, imakhalanso njila imene Yehova amanitonthozela na kunilimbikitsa.” Delphine analemba maina a anthu ochulidwa m’Baibo amene panthawi inayake anavutika na cisoni cacikulu. Iye anazindikila kuti, “Onsewo anali kukonda kupemphela kwa Mulungu.” Anazindikilanso kuti munthu “sangakwanitse kupilila ngati saŵelenga Baibo.”

Kuphunzila Baibo kwam’thandizanso Delphine kusumika maganizo ake pa zam’tsogolo osati pa zakumbuyo. Kuganizila lonjezo la pa Machitidwe 24:15 kumam’tonthoza. Lembali limakamba kuti: “Kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama omwe.” Kodi iye amakhulupililadi kuti Yehova adzaukitsa mwana wake? Delphine anati: “M’maganizo mwanga, nimayelekezela kuti nikumuona mwana wanga ataukitsidwa. Cili monga kuti Mulungu analembelatu pa kalenda tsiku limene tidzakumana na mwana wanga m’dziko latsopano. Nimayelekezela kuti nikumuona tili limodzi m’munda wathu, ndipo nikumuonetsa cikondi ngati cimene n’namuonetsa atangobadwa.”

a Zomvetsela zambili monga zimenezi zimapezeka pa webusaiti ya jw.org.

Baibo ingakuthandizeni kupeza citonthozo ngakhale pa nthawi zovuta kwambili

KODI MULUNGU ANGATITHANDIZE BWANJI?

Baibo imayankha momveka bwino kuti: “Yehova ali pafupi ndi onse oitanila pa iye. Iye ali pafupi ndi onse amene amamuitana m’coonadi, ndipo anthu amene amamuopa adzawacitila zokhumba zawo, adzamva kufuula kwawo kopempha thandizo ndipo adzawapulumutsa.” (Salimo 145:18, 19) Mau awa ni olimbikitsa, si conco? Koma kodi Mulungu amayankha bwanji mapemphelo a anthu amene amapempha citsogozo kwa iye?

Mavuto akhoza kutifooketsa mwakuthupi na mwauzimu, ndi kuticititsa kukhala na nkhawa. (Miyambo 24:10) Koma Yehova “amapeleka mphamvu kwa munthu wotopa, ndipo wofooka amam’patsa nyonga zoculuka.” (Yesaya 40:29) Mtumwi Paulo amene anapilila mayeselo aakulu anakamba kuti: “Pa zinthu zonse, ndimapeza mphamvu kucokela kwa iye amene amandipatsa mphamvu.” (Afilipi 4:13) Paulo analimbikitsidwa na mzimu woyela wa Mulungu. Naimwe mungapemphe Mulungu kuti akupatseni mzimu woyela.—Luka 11:13.

Nanga bwanji ngati mufuna thandizo kuti mumvetse na kuseŵenzetsa malangizo a m’Baibo? Mtumwi Yakobo analemba kuti: “Ngati wina akusowa nzelu, azipempha kwa Mulungu, ndipo adzamupatsa, popeza iye amapeleka mowolowa manja kwa onse ndiponso amapeleka mosatonza.” (Yakobo 1:5) Mukhoza kucita zinthu mogwilizana na mapemphelo anu mwa kuŵelenga Baibo na kuseŵenzetsa zimene mwaphunzila. (Yakobo 1:23-25) Pamene mucita zimenezi, mudzaona kuti malangizo ake ni othandiza.

Ngakhale pamene muli na nkhawa yaikulu, Yehova angakuthandizeni kukhala na mtendele wa mu mtima. Mau ake amakamba kuti: “Musamade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa ciliconse, mwa pemphelo ndi pembedzelo, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. Mukatelo, mtendele wa Mulungu umene umaposa kuganiza mozama kulikonse, udzateteza mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.” (Afilipi 4:6, 7) Inde, mukhoza kum’pempha Yehova kuti akupatseni mtendele.

Koma bwanji ngati mavuto amene mukumana nawo sakutha mwamsanga? Musaganize kuti Mulungu wakusiyani. Ngati mavuto anu sakutha, musataye mtima cifukwa Mulungu adzakulimbitsani na kukupatsani mphamvu kuti mupilile. (1 Akorinto 10:13) Baibo imatilonjeza kuti idzafika nthawi pamene mavuto athu adzatha, ndipo sadzakhalaponso!

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani