LAIBULALI YA PA INTANETI ya Watchtower
Watchtower
LAIBULALI YA PA INTANETI
Cinyanja
  • BAIBO
  • ZOFALITSA
  • MISONKHANO
  • mwb17 March tsa. 6
  • Thandizani a m’Banja Lanu Kukumbukila Yehova

Palibe vidiyo yake.

Pepani, vidiyo yakanga kulila.

  • Thandizani a m’Banja Lanu Kukumbukila Yehova
  • Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
  • Nkhani Zofanana
  • Kulambila kwa Pabanja—Zimene Mungacite Kuti Kukhale Kosangalatsa Kwambili
    Nsanja ya Mlonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2014
  • Lambilani Yehova Monga Banja
    N’zotheka Banja Lanu Kukhala Lacimwemwe
Umoyo na Utumiki Wathu Wacikhristu—Kabuku ka Misonkhano —2017
mwb17 March tsa. 6

UMOYO WATHU WACIKHRISTU

Thandizani a m’Banja Lanu Kukumbukila Yehova

Yeremiya anapatsidwa nchito yocenjeza Ayuda za ciwonongeko cimene cinali kubwela pa iwo cifukwa anali ataiŵala Mulungu wawo, Yehova. (Yer. 13:25) Cinacitika n’ciani kuti umoyo wakuuzimu wa mtunduwu ufike poipa conco? Mabanja aciisiraeli sanalinso auzimu. N’zoonekelatu kuti mitu ya mabanja siinali kutsatila malangizo a Yehova a pa Deuteronomo 6:5-7.

Banja la kholo limodzi likucita Kulambila kwa Pabanja; banja likucita Kulambila kwa Pabanja poseŵenzetsa mapu oonetsa malo a m’nthawi za m’Baibo

Mabanja olimba kuuzimu amapangitsa mipingo kukhala yolimba. Mitu ya mabanja ingathandize mabanja awo kukumbukila Yehova mwa kumacititsa Kulambila kwa Pabanja kwa phindu nthawi zonse. (Sal. 22:27) Pambuyo potamba vidiyo yakuti “Mau Awa . . . Azikhala Pamtima Pako”​—Kufunsa Mafunso Mabanja, yankhani mafunso aya:

  • N’ciani cathandiza mabanja ena kuthetsa zopinga zofala zimene zimalepheletsa kulambila kwa pabanja?

  • Kodi pali mapindu anji ngati tikhala na Kulambila kwa Pabanja kokhazikika?

  • Pa nkhani ya kulambila kwa pabanja, n’zovuta ziti zimene ine pacanga nimakhala nazo? Nanga nakonzekela kuzithetsa bwanji?

    Mabuku a m’Cinyanja (2000-2025)
    Tulukani
    Loŵani
    • Cinyanja
    • Gawilani
    • Makonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenela Kutsatila
    • Mfundo Yosunga Cisinsi
    • Kusunga Cinsinsi
    • JW.ORG
    • Loŵani
    Gawilani